< II Królewska 6 >
1 I synowie proroków powiedzieli do Elizeusza: Oto miejsce, w którym mieszkamy wraz z tobą, jest zbyt ciasne dla nas.
Ana a aneneri anati kwa Elisa, “Taonani malo amene timakhala ndi inu atichepera kwambiri.
2 Pozwól, że pójdziemy aż nad Jordan, weźmiemy stamtąd każdy po jednej belce i zbudujemy tam sobie miejsce na mieszkanie. Odpowiedział: Idźcie.
Tiloleni tipite ku Yorodani kumene aliyense wa ife akadule mtengo umodzi, kuti timange malo woti tizikhalamo.” Ndipo Elisa anati, “Pitani.”
3 Jeden z nich powiedział: Racz, proszę, pójść ze swoimi sługami. Odpowiedział: Pójdę.
Mmodzi wa iwo anati, “Chonde mulole kutsagana nawo atumiki anu.” Elisa anayankha kuti, “Ndipita nanu.”
4 I poszedł z nimi. Kiedy przybyli nad Jordan, zaczęli ścinać drzewa.
Ndipo anapita nawo. Anapita ku Yorodani nayamba kudula mitengo.
5 I zdarzyło się, że jednemu z nich przy ścinaniu drzewa [siekierą] żelazo wpadło do wody. Zawołał wtedy: Ach, mój panie! Ta [była] pożyczona.
Pamene wina ankadula mtengo, nkhwangwa yake inaguluka nigwera mʼmadzi. Iye anafuwula kuti, “Mayo! Mbuye wanga! Popeza ndi yobwereka!”
6 Mąż Boży zapytał: Gdzie wpadło? I wskazał mu miejsce. A on uciął drewno, wrzucił tam i żelazo wypłynęło.
Ndipo munthu wa Mulungu uja anafunsa, “Yagwera pati?” Pamene anamuonetsa malowo, Elisa anadula kamtengo nakaponya pamenepo, ndipo nkhwangwayo inayandama.
7 I powiedział: Weź [je] sobie. Wyciągnął więc rękę i wziął je.
Elisa anati, “Itenge.” Ndipo munthuyo anatambalitsa dzanja lake nayitenga.
8 Potem, gdy król Syrii prowadził wojnę z Izraelem, naradzał się ze swoimi sługami, mówiąc: W tym a w tym miejscu będzie mój obóz.
Tsono mfumu ya ku Aramu inali pa nkhondo ndi Israeli. Itakambirana ndi atsogoleri ake ankhondo inati, “Ndidzamanga misasa yanga pamalo akutiakuti.”
9 Wtedy mąż Boży posłał do króla Izraela wiadomość: Strzeż się przechodzić przez to miejsce, bo tam Syryjczycy zrobili zasadzkę.
Munthu wa Mulungu anatumiza mawu kwa mfumu ya ku Israeli kuti “Musamale podutsa malo akuti, chifukwa Aaramu akupita kumeneko.”
10 Posłał więc król Izraela na to miejsce, o którym mu powiedział mąż Boży, ostrzegając go, i [król] uratował się nie raz i nie dwa.
Choncho mfumu ya ku Israeli inatuma anthu kumalo kumene munthu wa Mulunguyo ananena. Nthawi ndi nthawi Elisa ankachenjeza mfumu, kotero kuti ankakhala tcheru ku malo amenewo.
11 Serce króla Syrii zatrwożyło się z tego powodu. Zwołał więc swoje sługi i zapytał ich: Czemu mi nie powiecie, kto z nas [donosi] królowi Izraela?
Zimenezi zinakwiyitsa kwambiri mfumu ya ku Aramu. Mfumuyo inayitanitsa atsogoleri ake ankhondo ndipo inawafunsa kuti, “Kodi simungandiwuze munthu amene pakati pathu pano ali mbali ya mfumu ya ku Israeli?”
12 Jeden z jego sług odpowiedział: Nikt, mój panie, królu. To prorok Elizeusz, który jest w Izraelu, oznajmia królowi Izraela słowa, które wypowiadasz w swoim pokoju sypialnym.
Mmodzi mwa atsogoleri a ankhondowo anati, “Palibe ndi mmodzi yemwe pakati pathu, inu mbuye wanga, koma Elisa mneneri amene ali ku Israeli amawuza mfumu ya ku Israeli mawu enieni amene inu mumayankhula ku chipinda kwanu.”
13 [On] odpowiedział: Idźcie i dowiedzcie się, gdzie on jest, abym posłał [po niego] i pojmał go. I doniesiono mu: Oto jest w Dotan.
Choncho mfumu inalamula kuti, “Pitani, kafufuzeni kumene akukhala kuti ine nditume anthu kukamugwira.” Anthuwo anabweretsa mawu oti, “Taonani, Elisa ali ku Dotani.”
14 Posłał więc tam konie i rydwany, i znaczny [oddział] wojska. Wyruszyli w nocy i oblegli miasto.
Ndipo mfumu inatumizako magaleta ndi akavalo ndiponso gulu lankhondo lamphamvu. Anapita usiku nakawuzungulira mzindawo.
15 Kiedy sługa męża Bożego wstał wcześnie rano i wyszedł, oto wojsko otoczyło miasto razem z końmi i rydwanami. Jego sługa powiedział do niego: Ach, mój panie! Cóż mamy czynić?
Mtumiki wa munthu wa Mulungu atadzuka mmamawa ndi kutuluka panja, gulu la ankhondo pamodzi ndi akavalo ndi magaleta anali atazungulira mzindawo. Mtumikiyo anafunsa kuti, “Kalanga mbuye wanga, tidzachita chiyani?”
16 Odpowiedział: Nie bój się, bo więcej jest tych, którzy [są] z nami, niż tych, którzy [są] z nimi.
Mneneri anamuyankha kuti, “Usachite mantha. Amene ali mbali yathu ndi ambiri kupambana amene ali mbali yawo.”
17 Wtedy modlił się Elizeusz: PANIE, otwórz, proszę, jego oczy, aby widział. PAN otworzył oczy tego sługi i ten zobaczył: oto góra była pełna koni i ognistych rydwanów wokół Elizeusza.
Ndipo Elisa anapemphera kuti, “Inu Yehova tsekulani maso ake kuti aone.” Pamenepo Yehova anatsekula maso a mtumikiyo, ndipo anayangʼana naona kuti phiri lonse linali lodzaza ndi akavalo ndi magaleta a moto atazungulira Elisa.
18 A gdy [Syryjczycy] zeszli do niego, Elizeusz modlił się do PANA i powiedział: Proszę, dotknij ten lud ślepotą. I [PAN] dotknął go ślepotą według słowa Elizeusza.
Pamene adaniwo ankabwera kudzalimbana naye, Elisa anapemphera kwa Yehova kuti, “Achititseni khungu anthu awa.” Kotero Yehova anawachititsa khungu monga anapemphera Elisa.
19 Wtedy Elizeusz powiedział do nich: To nie ta droga ani nie to miasto. Pójdźcie za mną, a zaprowadzę was do człowieka, którego szukacie. I zaprowadził ich do Samarii.
Elisa anawawuza ankhondowo kuti, “Njira si imeneyi ndipo mzinda sumenewunso. Tsateni, ndipo ndidzakutengerani kwa munthu amene mukumufunayo.” Ndipo anawatengera ku Samariya.
20 A gdy weszli do Samarii, Elizeusz powiedział: PANIE, otwórz im oczy, aby przejrzeli. PAN otworzył im oczy i zobaczyli, że [są] w środku Samarii.
Atalowa mu mzinda wa Samariya, Elisa anati, “Yehova tsekulani maso a anthu awa kuti aone.” Choncho Yehova anatsekula maso awo ndipo anangoona kuti ali mʼkati mwenimweni mwa Samariya.
21 Gdy król Izraela zobaczył ich, zapytał Elizeusza: Czy mam ich zabić, mój ojcze?
Mfumu ya ku Israeli itawaona, inafunsa Elisa kuti, “Abambo anga, kodi ndiwaphe? Kodi ndiwaphe?”
22 Odpowiedział: Nie zabijaj. Czy zabijasz tych, których pojmałeś swoim mieczem i swoim łukiem? Połóż przed nimi chleb i wodę, aby jedli i pili, i wrócili do swego pana.
Elisa anayankha kuti, “Musawaphe. Kodi mungaphe anthu amene munawagwira pogwiritsa ntchito lupanga ndi uta? Apatseni chakudya ndi madzi kuti adye ndi kumwa kenaka apite kwa mbuye wawo.”
23 Przygotował więc dla nich wielką ucztę. A gdy jedli i pili, odprawił ich i poszli do swego pana. Odtąd bandy Syryjczyków już nie wpadały do ziemi Izraela.
Choncho anawakonzera mphwando lalikulu, ndipo atatsiriza kudya ndi kumwa, anawatumiza kwawo ndipo anabwerera kwa mbuye wawo. Kotero magulu a ankhondo a ku Aramu analeka kuthira nkhondo dziko la Israeli.
24 Potem Ben-Hadad, król Syrii, zebrał całe swoje wojsko, wyruszył i obległ Samarię.
Patapita nthawi, Beni-Hadadi mfumu ya Aramu anasonkhanitsa gulu lake lonse la ankhondo, napita kukazungulira mzinda wa Samariya.
25 I nastał wielki głód w Samarii. Tak bowiem ją oblegali, że głowa osła [kosztowała] osiemdziesiąt srebrników, a ćwierć kaba gołębiego gnoju – pięć srebrników.
Mu mzinda wa Samariya munali njala yoopsa. Ndipo taonani, Aaramu anazungulira mzindawu kwa nthawi yayitali kotero kuti mutu wa bulu ankawugulitsa ndalama za siliva 80, ndipo magalamu 200 a zitosi za nkhunda ankawagulitsa pa mtengo wa masekeli asanu.
26 A gdy król Izraela przechodził po murze, [pewna] kobieta zawołała do niego: Ratuj mnie, mój panie, królu!
Pamene mfumu inkayenda pa khoma la mzindawo, mayi wina anafuwulira mfumuyo kuti, “Thandizeni mbuye wanga mfumu!”
27 Odpowiedział: Jeśli PAN cię nie uratuje, jakże [ja] ciebie uratuję? Czy z klepiska lub z tłoczni?
Mfumu inayankha kuti, “Ngati Yehova sakuthandiza iwe, ine thandizo lako ndingalipeze kuti? Kuchokera ku malo opunthira tirigu kodi? Kuchokera kumalo opsinyira mphesa kodi?”
28 Następnie król zapytał ją: Co ci jest? Odpowiedziała: Ta oto kobieta powiedziała mi: Daj swojego syna, abyśmy go zjadły dzisiaj, a jutro zjemy mojego syna.
Pamenepo mfumuyo inafunsa mayiyo kuti, “Kodi chakuvuta nʼchiyani?” Iye anayankha kuti, “Mayi uyu anandiwuza kuti, ‘Bweretsa mwana wako kuti timudye lero, ndipo mawa tidzadya mwana wangayu.’
29 Ugotowałyśmy więc mojego syna i zjadłyśmy go. Potem powiedziałam jej na drugi dzień: Daj swojego syna, abyśmy go zjadły. Lecz ona ukryła swojego syna.
Choncho tinaphika mwana wanga ndi kumudya. Tsiku lotsatira lakelo ine ndinati, ‘Bweretsa mwana wako kuti timudye,’ koma iye anabisa mwana wakeyo.”
30 A gdy król usłyszał słowa tej kobiety, rozdarł swoje szaty. I kiedy przechodził po murze, lud zobaczył, że pod spodem nosił wór na swoim ciele.
Mfumu itamva mawu a mayiyo, inangʼamba mkanjo wake. Pamene inkayenda pa khoma, anthu anayangʼana, ndipo anaona zovala zamʼkati, pakuti anavala chiguduli.
31 Wtedy [król] powiedział: Niech mi to uczyni Bóg i tamto dorzuci, jeśli głowa Elizeusza, syna Szafata, ostoi się na nim dzisiaj.
Mfumuyo inati, “Mulungu andilange, andilange kwambiri ndikapanda kudula mutu wa Elisa mwana wa Safati lero!”
32 Elizeusz zaś siedział w swoim domu i starsi siedzieli razem z nim. I [król] wysłał przed sobą człowieka. Lecz zanim posłaniec przyszedł do niego, powiedział do starszych: Czy widzicie, że ten syn mordercy posłał, aby mi ucięto głowę? Uważajcie, gdy ten posłaniec przyjdzie, zamknijcie drzwi i zatrzymajcie go przed drzwiami. Czy za nim nie słychać kroków mego pana?
Tsono Elisa nʼkuti atakhala mʼnyumba mwake, ndipo akuluakulu anali naye limodzi. Mfumu inatuma munthu wina kuti imutsogolere, koma asanafike, Elisa anawuza akuluakuluwo kuti, “Kodi simukuona momwe wopha munthu uja watumizira munthu wina kuti adzadule mutu wanga? Taonani mthengayo akafika, mutseke chitseko ndipo muchigwiritsitse kuti asalowe. Kodi ndikumvawo pambuyo pake si mgugu wa mbuye wake?”
33 A gdy jeszcze z nimi rozmawiał, oto posłaniec przybył do niego i powiedział: To nieszczęście jest od PANA. Czego mam jeszcze oczekiwać od PANA?
Elisa akuyankhulabe ndi anthuwo, taonani, wamthengayo anafika kwa iye. Ndipo mfumu inati, “Mavuto amenewa ndi ochokera kwa Yehova. Kodi nʼchifukwa chiyani ine ndiyenera kudikira thandizo lochokera kwa Yehova?”