< II Królewska 24 >

1 Za jego dni wyruszył Nabuchodonozor, król Babilonu, i Joakim stał się jego sługą przez trzy lata. Potem zbuntował się przeciwko niemu.
Pa nthawi ya ulamuliro wa Yehoyakimu, Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anadzathira nkhondo dzikolo ndipo Yehoyakimu anakhala pansi pa ulamuliro wake zaka zitatu. Koma kenaka anasintha maganizo ake nawukira Nebukadinezara.
2 A PAN posłał przeciwko niemu oddziały Chaldejczyków, oddziały Syryjczyków, oddziały Moabitów i oddziały synów Ammona. Posłał ich na Judę, aby go zniszczyć zgodnie ze słowem PANA, które wypowiedział przez swoje sługi, proroków.
Yehova anatumiza magulu a Ababuloni, Aaramu, Amowabu ndi Aamoni, kudzathira nkhondo Yuda. Iye anawatumiza kudzawononga Yuda molingana ndi mawu amene Yehova ananeneratu kudzera mwa aneneri ake.
3 Owszem, zgodnie z poleceniem PANA spotkało to Judę, aby odrzucić go sprzed jego oblicza za grzechy Manassesa, za to wszystko, co uczynił;
Ndithu, izi zinachitikira Yuda monga momwe Yehova analamulira nʼcholinga choti awachotse pamaso pake chifukwa cha machimo a Manase ndi zonse zimene anachita,
4 A także za krew niewinną, którą przelał, bo napełnił Jerozolimę krwią niewinną, czego PAN nie chciał przebaczyć.
kuphatikizapo kukhetsa magazi a anthu osalakwa. Chifukwa iye anadzaza Yerusalemu ndi magazi a anthu osalakwa ndipo Yehova sanafune kumukhululukira.
5 A pozostałe dzieje Joakima i wszystko, co czynił, czy nie są zapisane w księdze kronik królów Judy?
Ntchito zina za Yehoyakimu ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
6 I Joakim zasnął ze swymi ojcami, a jego syn Joachin królował w jego miejsce.
Yehoyakimu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake. Ndipo Yehoyakini mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
7 A król Egiptu już więcej nie wyruszał ze swojej ziemi, gdyż król Babilonu wziął [wszystko], co należało do króla Egiptu, od rzeki Egiptu aż do rzeki Eufrat.
Mfumu ya Igupto sinatulukenso mʼdziko lake chifukwa mfumu ya Babuloni inalanda mayiko onse kuchokera ku Mtsinje wa ku Igupto mpaka ku Mtsinje wa Yufurate.
8 Joachin miał osiemnaście lat, kiedy zaczął królować, i królował trzy miesiące w Jerozolimie. Jego matka [miała] na imię Nechuszta [i była] córką Elnatana z Jerozolimy.
Yehoyakini anakhala mfumu ali ndi zaka 18 ndipo analamulira mu Yerusalemu miyezi itatu. Amayi ake anali Nehusita mwana wa Elinatani wa ku Yerusalemu.
9 Czynił on to, co złe w oczach PANA, zupełnie tak, jak czynił jego ojciec.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova monga anachitira abambo ake.
10 W tym czasie słudzy Nabuchodonozora, króla Babilonu, wyruszyli przeciw Jerozolimie i przyszło do oblężenia miasta.
Nthawi imeneyo ankhondo a Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anabwera ku Yerusalemu nazinga mzindawo ndi misasa ya nkhondo
11 Potem sam Nabuchodonozor, król Babilonu, nadciągnął przeciw miastu, a jego słudzy je oblegali.
ndipo Nebukadinezara anafika ku mzindawo pamene ankhondo ake anawuzinga.
12 Wtedy Joachin, król Judy, wyszedł do króla Babilonu, on i jego matka, jego słudzy, jego książęta i jego dworzanie. I król Babilonu pojmał go w ósmym roku swego panowania.
Yehoyakini mfumu ya Yuda pamodzi ndi amayi ake, atumiki ake, anthu ake olemekezeka ndiponso akuluakulu onse anadzipereka kwa mfumu ya ku Babuloni. Mfumu ya Babuloni inagwira Yoyakini ukapolo mʼchaka chachisanu ndi chitatu cha ufumu wake.
13 I wyniósł stamtąd wszystkie skarby domu PANA i skarby domu królewskiego i pokruszył wszystkie przedmioty złote, które wykonał Salomon, król Izraela, dla świątyni PANA, tak jak zapowiedział PAN.
Monga ananenera Yehova, Nebukadinezara anachotsa chuma chonse cha mʼNyumba ya Yehova ndiponso cha mʼnyumba ya mfumu ndipo anatenga ziwiya zonse zagolide za ku Nyumba ya Yehova zimene Solomoni mfumu ya Israeli anapanga.
14 I przesiedlił całą Jerozolimę: wszystkich książąt, wszystkich dzielnych wojowników – dziesięć tysięcy jeńców, oraz wszystkich rzemieślników i kowali. Nie pozostał nikt oprócz ubogiego ludu tej ziemi.
Anatenga anthu onse a mu Yerusalemu kupita nawo ku ukapolo. Akuluakulu onse pamodzi ndi anthu ankhondo, anthu onse aluso ndi amisiri osula onse pamodzi analipo 10,000. Osauka okha ndiye anatsala mʼdzikomo.
15 Przeniósł też do Babilonu Joachina. A także matkę króla, żony króla, jego dworzan i dostojników tej ziemi zabrał do niewoli z Jerozolimy do Babilonu.
Nebukadinezara anatenga Yehoyakini ngati kapolo kupita naye ku Babuloni. Mu Yerusalemu anatenganso amayi a mfumu, akazi ake, akuluakulu ake ndiponso anthu olemekezeka mʼdzikomo.
16 Także wszystkich dzielnych mężów [w liczbie] siedmiu tysięcy, tysiąc rzemieślników i kowali oraz wszystkich zdolnych do walki – tych zabrał król Babilonu do niewoli do Babilonu.
Mfumu ya Babuloni inatumizanso ku Babuloni anthu ankhondo 70,000, anthu amphamvu ndi okonzeka kupita ku nkhondo, anthu aluso ndi amisiri osula 1,000.
17 W jego miejsce król Babilonu ustanowił królem jego stryja Mattaniasza i zmienił mu imię na Sedekiasz.
Iye analonga ufumu Mataniya, malume wa Yoyakini mʼmalo mwake ndipo anasintha dzina lake kuti akhale Zedekiya.
18 Sedekiasz miał dwadzieścia jeden lat, kiedy zaczął królować, i królował jedenaście lat w Jerozolimie. Jego matka [miała] na imię Chamutal [i była] córką Jeremiasza z Libny.
Zedekiya anakhala mfumu ali ndi zaka 21 ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 11. Amayi ake anali Hamutali mwana wa Yeremiya wa ku Libina.
19 Czynił on to, co złe w oczach PANA, zupełnie tak, jak czynił Joakim.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova monga anachitira Yehoyakimu.
20 Z powodu gniewu PANA przyszło to na Jerozolimę i Judę, aż odrzucił ich sprzed swego oblicza. A Sedekiasz zbuntował się przeciw królowi Babilonu.
Zonsezi zinachitikira Yerusalemu ndi Yuda chifukwa cha mkwiyo wa Mulungu ndipo pa mapeto pake anawachotsa pamaso pake. Ndipo Zedekiya anawukira mfumu ya Babuloni.

< II Królewska 24 >