< II Królewska 17 >
1 W dwunastym roku Achaza, króla Judy, Ozeasz, syn Eli, zaczął królować w Samarii nad Izraelem [i królował] dziewięć lat.
Mʼchaka cha 12 cha Ahazi mfumu ya Yuda, Hoseya mwana wa Ela anakhala mfumu ya Israeli mu Samariya ndipo analamulira zaka zisanu ndi zinayi.
2 Czynił on to, co złe w oczach PANA, jednak nie tak jak królowie Izraela, którzy byli przed nim.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, koma osafanana ndi mafumu a Israeli amene ankalamulira iye asanalowe ufumuwo.
3 Przeciw niemu wyruszył Salmanaser, król Asyrii, a Ozeasz został jego sługą i płacił mu daninę.
Salimenezeri mfumu ya ku Asiriya anabwera kudzathira nkhondo Hoseya amene anali pansi pa ulamuliro wake ndipo ankapereka msonkho kwa iyeyo.
4 I król Asyrii wykrył spisek Ozeasza. Ten bowiem wyprawił posłańców do So, króla Egiptu, i nie posłał corocznej daniny królowi Asyrii. Król Asyrii więc pojmał go i zamknął w więzieniu.
Koma mfumu ya ku Asiriya inazindikira kuti Hoseya akuwukira, pakuti Hoseyayo anali atatumiza nthumwi kwa So mfumu ya Igupto ndiponso analeka kukhoma msonkho kwa mfumu ya ku Asiriya, monga ankachitira chaka ndi chaka. Choncho Salimenezeri anagwira Hoseya ndi kumuyika mʼndende.
5 Król Asyrii najechał całą ziemię, przybył do Samarii i oblegał ją przez trzy lata.
Mfumu ya ku Asiriya inapita kukathira nkhondo dziko lonse la Israeli ndipo inapita mpaka ku Samariya ndipo inazinga mzindawo kwa zaka zitatu.
6 A w dziewiątym roku Ozeasza król Asyrii zdobył Samarię, uprowadził Izraela do Asyrii i osiedlił ich w Chalach i Chaborze, nad rzeką Gozan, oraz w miastach Medów.
Mʼchaka chachisanu ndi chinayi cha Hoseya, mfumu ya ku Asiriya inalanda Samariya ndipo inatenga Aisraeli ndi kupita nawo ku Asiriya. Anakawakhazika ku Hala ndi Habori mʼmbali mwa mtsinje wa Gozani ndi mʼmizinda ya Amedi.
7 A stało się tak, [dlatego] że synowie Izraela zgrzeszyli przeciw PANU, swemu Bogu, który ich wyprowadził z ziemi Egiptu, spod ręki faraona, króla Egiptu, a bali się obcych bogów;
Zonsezi zinachitika chifukwa Aisraeli anachimwira Yehova Mulungu wawo, amene anawatulutsa mʼdziko la Igupto pansi pa ulamuliro wa Farao mfumu ya Igupto. Iwo ankapembedza milungu ina,
8 Postępując według ustaw pogan, których PAN wypędził sprzed oblicza synów Izraela, oraz [ustaw] królów Izraela, które stwarzali.
ndiponso ankatsatira miyambo ya anthu a mitundu imene Yehova anayichotsa pamene iwo ankafika mʼdzikomo pamodzinso ndi miyambo yonse imene mafumu a Israeli anayambitsa.
9 Synowie Izraela robili potajemnie przeciwko PANU, swemu Bogu, to, co nie było słuszne, i pobudowali sobie wyżyny we wszystkich swoich miastach, od wieży strażników aż do miasta warownego.
Ndipo Aisraeli ankachita zoyipa mwamseri kutsutsana ndi Yehova Mulungu wawo. Kuchokera ku nsanja ya alonda mpaka ku mzinda wotetezedwa, mʼmizinda yawo yonse anamangamo malo opembedzeramo mafano.
10 Ustawiali sobie posągi i gaje na każdym wyniosłym pagórku i pod każdym zielonym drzewem;
Anayimika miyala ya chipembedzo ndi mitengo ya mafano a Asera pa phiri lililonse lalitali ndi pansi pa mtengo uliwonse wa masamba ambiri.
11 I palili tam kadzidła na wszystkich wyżynach, tak jak narody, które PAN wypędził przed nimi, i popełniali niegodziwe czyny, pobudzając PANA do gniewu;
Pa malo aliwonse opembedzera mafano, anthuwa ankafukiza lubani monga momwe ankachitira anthu a mitundu imene Yehova anayichotsa pamene iwo ankafika. Iwo anachita zinthu zoyipa zomwe zinaputa mkwiyo wa Yehova.
12 Służyli bożkom, o których PAN im powiedział: Nie czyńcie tego.
Ndipo iwowo ankapembedza mafano ngakhale Yehova ananena kuti, “Musadzachite zimenezi.”
13 A PAN świadczył przeciw Izraelowi i przeciw Judzie przez wszystkich proroków [i] wszystkich widzących, mówiąc: Odwróćcie się od swoich złych dróg i przestrzegajcie moich przykazań i moich nakazów według całego prawa, które nadałem waszym ojcom, a które przekazałem wam przez moje sługi, proroków.
Yehova anachenjeza Israeli ndi Yuda kudzera mwa aneneri ake onse ndi alosi kuti, “Lekani mchitidwe wanu woyipawo. Mverani malamulo anga ndi malangizo anga potsatira zonse zolembedwa mʼmalamulo a Mose, zimene ndinalamulira makolo anu kuti azimvere, kudzera mwa aneneri, atumiki anga.”
14 Lecz nie słuchali, ale uczynili twardym swój kark, jak kark ich ojców, którzy nie wierzyli w PANA, swego Boga.
Koma anthuwa sanamvere ndipo anawumitsa khosi ngati momwe analili makolo awo, amene sanadalire Yehova Mulungu wawo.
15 I wzgardzili jego nakazami i przymierzem, które zawarł z ich ojcami, oraz jego świadectwami, którymi świadczył przeciwko nim, i chodzili za marnościami, stali się próżni i naśladowali pogan, którzy ich otaczali, co do których PAN im rozkazał, aby nie czynili tak jak oni.
Anakana malangizo ake ndi pangano anachita ndi makolo awo ndipo ananyoza zochenjeza za Yehova. Iwo anatsatira mafano achabechabe nasanduka achabechabe. Anthuwa anatsanzira mitundu ya anthu owazungulira ngakhale kuti Yehova anawalamula kuti, “Musamachite zomwe iwo amachita,” koma iwo anachita zomwe Yehova anawaletsa.
16 I opuścili wszystkie przykazania PANA, swego Boga, i wykonali sobie lane posągi – dwa cielce. Zrobili sobie też gaje, oddawali pokłon wszystkim zastępom niebieskim i służyli Baalowi.
Iwowo anasiya malamulo onse a Yehova Mulungu wawo, nadzipangira mafano awiri osungunula a ana angʼombe ndiponso fano la Asera, napembedza zonse zamlengalenga ndi kutumikira Baala.
17 Przeprowadzali swoich synów i swoje córki przez ogień, uprawiali wróżbiarstwo i czarnoksięstwo i zaprzedali się, aby czynić to, co złe w oczach PANA, pobudzając go do gniewu.
Ndipo anadutsitsa mʼmoto ana awo aamuna ndi aakazi. Iwo ankawombeza mawula, namachitanso zanyanga ndipo anadzipereka kuchita zoyipa pamaso pa Yehova namukwiyitsa.
18 Dlatego PAN bardzo się rozgniewał na Izraela i odrzucił go sprzed swego oblicza. Nic nie pozostało oprócz samego pokolenia Judy.
Choncho Yehova anakwiya nawo kwambiri Aisraeli ndipo anawachotsa pamaso pake. Palibe amene anatsala kupatula fuko la Yuda lokha.
19 Ale również i Juda nie przestrzegał przykazań PANA, swego Boga, lecz postępował według nakazów, które Izrael stworzył.
Yuda nayenso sanasunge malamulo a Yehova Mulungu wawo. Iwo ankatsatira machitidwe amene Israeli anayambitsa.
20 PAN więc odrzucił całe potomstwo Izraela, trapił ich i wydał w ręce grabieżców, aż [wreszcie] odrzucił ich sprzed swego oblicza.
Motero Yehova anakana Aisraeli onse. Iye anawazunza nawapereka mʼmanja mwa anthu ofunkha mpaka Iye atawachotseratu pamaso pake.
21 Oderwał bowiem Izraela od domu Dawida, a oni ustanowili królem Jeroboama, syna Nebata. Jeroboam zaś odwiódł Izraela od naśladowania PANA i przywiódł go do popełnienia wielkiego grzechu.
Yehova atangʼamba Israeli kumuchotsa ku nyumba ya Davide, Aisraeliwo anasankha Yeroboamu mwana wa Nebati kukhala mfumu yawo. Yeroboamu ananyengerera Aisraeli kuti asatsatire Yehova ndipo anawachimwitsa tchimo lalikulu.
22 I synowie Izraela chodzili we wszystkich grzechach Jeroboama, które czynił, a nie odstąpili od nich;
Aisraeli anakakamira machimo onse amene Yeroboamu anachita ndipo sanawasiye
23 Aż PAN odrzucił Izraela sprzed swego oblicza, jak zapowiedział przez wszystkie swoje sługi, proroków. I tak Izrael został uprowadzony ze swojej ziemi do Asyrii, [i tak jest] aż do dziś.
mpaka pamene Yehova anawachotsa pamaso pake monga anawachenjezera kudzera mwa atumiki ake onse, aneneri. Choncho Aisraeli anachotsedwa mʼdziko lawo kupita ku ukapolo ku Asiriya ndipo ali komweko mpaka lero lino.
24 Potem król Asyrii sprowadził [ludzi] z Babilonu, z Kuta, z Awwa i z Chamat, i z Sefarwaim i osiedlił ich w miastach Samarii zamiast synów Izraela. Oni zaś posiedli Samarię i mieszkali w jej miastach.
Mfumu ya ku Asiriya inabweretsa anthu a ku Babuloni, Kuta, Awa, Hamati ndi a ku Sefaravaimu kudzawakhazika mʼmizinda ya Samariya kulowa mʼmalo mwa Aisraeli. Iwo anatenga Samariya ndi kukhala mʼmizinda yake.
25 A gdy zaczęli tam mieszkać, nie bali się PANA. PAN więc zesłał na nich lwy, które ich zabijały.
Iwo atayamba kukhala kumeneko, sanapembedze Yehova choncho Yehova anatumiza mikango pakati pawo ndipo inapha ena mwa iwo.
26 I doniesiono o tym królowi Asyrii: Narody, które uprowadziłeś i osiedliłeś w miastach Samarii, nie znają zwyczajów Boga tej ziemi. Dlatego zesłał na nich lwy, a oto zabijają ich, ponieważ nie znają zwyczajów Boga tej ziemi.
Tsono mfumu ya ku Asiriya inawuzidwa za nkhaniyi kuti, “Anthu amene munawatumiza ndi kuwakhazika mʼmizinda ya Samariya sakudziwa chimene Mulungu wa dzikolo amafuna. Choncho Iye watumiza mikango pakati pawo imene ikuwapha chifukwa anthuwo sadziwa chimene Mulungu wa dzikolo amafuna.”
27 Wtedy król Asyrii rozkazał: Zaprowadźcie tam jednego z kapłanów, których stamtąd uprowadziliście, aby poszedł i tam zamieszkał, i nauczał ich zwyczajów Boga tej ziemi.
Tsono mfumu ya ku Asiriya inalamula kuti, “Tengani wansembe mmodzi mwa amene munawagwira ukapolo, mupite naye kumeneko ndipo akakhale komweko nakaphunzitse anthu zimene Mulungu wa dzikolo amafuna.”
28 Przybył więc jeden z kapłanów, których uprowadzono z Samarii, i zamieszkał w Betel, i nauczał ich, jak mają się bać PANA.
Choncho mmodzi mwa ansembe amene anawatenga ku Samariya anabwera kudzakhala ku Beteli ndipo ankaphunzitsa anthuwo kupembedza Yehova.
29 Jednakże każdy naród czynił sobie własnych bogów i stawiał ich w domach wyżyn, które Samarytanie pobudowali, każdy naród w swoich miastach, w których mieszkał.
Koma mtundu uliwonse wa anthu unkapangabe mafano a milungu yawoyawo mʼmizinda yambiri imene anthuwo ankakhala, ndipo anayika milunguyo mʼnyumba za milungu zimene anthu a ku Samariya anamanga ku malo opembedzera mafano.
30 Babilończycy zrobili Sukkot-Benota, a ludzie z Kuta zrobili Nergala, a ludzie z Chamat zrobili Aszimę.
Anthu a ku Babuloni anapanga Sukoti-Benoti, anthu a ku Kuti anapanga Nerigali, ndipo anthu a ku Hamati anapanga Asima;
31 Awwici zrobili Nibchaza i Tartaka, a Sefarwaici palili swoje dzieci w ogniu dla Adrameleka i Anameleka, bogów Sefarwaim.
Aava anapanga Nibihazi ndi Taritaki, ndipo Asefaravaimu ankawotcha ana awo pa moto ngati nsembe kwa Adirameleki ndi Anameleki, milungu ya Asefaravaimu.
32 Tak więc bali się PANA i ustanowili spośród siebie kapłanów wyżyn, którzy składali dla nich [ofiary] w domach wyżyn.
Iwo ankapembedza Yehova, koma ankadzisankhira okha pakati pawo anthu wamba kuti akhale ansembe awo ku nyumba za milungu za ku malo opembedzera mafano.
33 Bali się PANA i służyli swoim bogom według zwyczajów tych narodów, skąd zostali uprowadzeni.
Iwowo ankapembedza Yehova, komanso ankatumikira milungu yawo molingana ndi miyambo ya mitundu ya kumene ankachokera.
34 Aż do tego dnia postępują według dawnych zwyczajów. Nie boją się PANA i nie czynią według jego ustaw, nakazów, prawa i przykazania, które PAN nakazał synom Jakuba, któremu nadał imię Izrael.
Mpaka lero lino iwo akupitirizabe kuchita zimene ankachita poyamba. Sapembedza Yehova kapenanso kutsata malangizo ake ndi malamulo ake, chiphunzitso chake monga mwa malamulo amene Yehova anawapereka kwa zidzukulu za Yakobo, amene anamutcha Israeli.
35 PAN zawarł też z nimi przymierze i rozkazał im: Nie bójcie się obcych bogów, nie kłaniajcie się im, nie służcie im ani nie składajcie im ofiar;
Pamene Yehova anachita pangano ndi Aisraeli, Iye anawalamula kuti, “Musapembedze milungu ina kapena kuyigwadira iyo, kuyitumikira kapena kupereka nsembe kwa iyoyo.
36 Lecz PANA, który was wyprowadził z ziemi Egiptu wielką mocą i wyciągniętym ramieniem, jego się bójcie, jemu oddawajcie pokłon i jemu składajcie ofiary.
Koma Yehova amene anakutulutsani mʼdziko la Igupto ndi dzanja lake lamphamvu ndiye amene muyenera kumupembedza.
37 Przestrzegajcie także ustaw, nakazów, prawa i przykazań, które wam napisał, i wypełniajcie je po wszystkie dni, a nie bójcie się innych bogów.
Muyenera kusamalitsa nthawi zonse kusunga malangizo anga ndi malemba anga, chiphunzitso ndi malamulo amene anakulemberani. Musapembedze milungu ina.
38 Nie zapominajcie o przymierzu, które zawarłem z wami, i nie bójcie się innych bogów.
Musayiwale pangano limene ndinapangana nanu ndipo musamapembedze milungu ina.
39 Ale PANA, waszego Boga, bójcie się, a on was wybawi z ręki wszystkich waszych wrogów.
Mʼmalo mwake muzipembedza Yehova Mulungu wanu pakuti ndiye amene adzakulanditsani mʼdzanja la adani anu onse.”
40 Lecz oni nie usłuchali, ale postępowali według dawnych zwyczajów.
Komabe iwo sanamvere ndipo anapitiriza kuchita zomwe ankachita kale.
41 Te narody więc bały się PANA i służyły swoim rytym bożkom, zarówno ich dzieci, jak i dzieci ich dzieci. Jak czynili ich ojcowie, tak i oni czynią aż do dziś.
Ngakhale anthuwo ankapembedza Yehova, ankatumikiranso mafano awo. Mpaka lero lino ana awo ndi zidzukulu zawo zikupitiriza kuchita zomwe ankachita makolo awo.