< II Królewska 10 >
1 Achab zaś miał siedemdziesięciu synów w Samarii. I Jehu napisał list, i wysłał [go] do Samarii do książąt Jizreel – do starszych i do tych, którzy wychowywali [synów] Achaba – ze słowami:
Tsono Ahabu anali ndi ana aamuna 70 a ku Samariya. Ndipo Yehu analemba makalata nawatumiza ku Samariya kwa atsogoleri a mu mzinda wa Yezireeli, kwa akuluakulu ndiponso kwa amene ankalera ana a Ahabu, nati,
2 Jak tylko dotrze do was ten list, a są przecież z wami synowie waszego pana, macie też rydwany, konie, miasto obronne i uzbrojenie;
“Inu mukangolandira kalatayi, popeza ana a mbuye wanu ali ndi inu ndiponso muli ndi magaleta ndi akavalo, mzinda wotetezedwa ndi zida zankhondo,
3 Upatrzcie sobie najlepszego i najodpowiedniejszego z synów waszego pana, posadźcie na tronie jego ojca i walczcie o dom waszego pana.
sankhani mwana wa mbuye wanu amene ndi wooneka bwino ndiponso woyenera, mulowetseni ufumu wa abambo ake. Kenaka muchite nkhondo kuteteza nyumba ya mbuye wanu.”
4 Lecz oni bardzo się przerazili i powiedzieli: Oto dwaj królowie nie ostali się przed nim, a jakże my się ostoimy?
Koma anthuwo anachita mantha kwambiri ndipo anati, “Taonani, mafumu awiri sanathe kulimbana naye, nanga ife tingathe bwanji?”
5 Wtedy ten, który był [postawiony] nad domem, i ten, który był nad miastem, starsi oraz wychowawcy [synów króla] wysłali do Jehu wiadomość: Jesteśmy twoimi sługami. Uczynimy wszystko, co nam rozkażesz. Nie ustanowimy żadnego króla. Czyń, co uznasz za dobre w swoich oczach.
Choncho woyangʼanira nyumba ya mfumu, bwanamkubwa wa mzinda, akuluakulu ena ndiponso olera anawo anatumiza uthenga uwu kwa Yehu: “Ife ndife atumiki anu ndipo tidzachita chilichonse chomwe mutiwuze. Sitidzasankha munthu wina aliyense kukhala mfumu ndipo chitani chimene mukuganiza kuti nʼchabwino kwa inu.”
6 I napisał do nich drugi list ze słowami: Jeśli jesteście moi i chcecie słuchać mego głosu, weźcie głowy synów waszego pana i przyjdźcie do mnie jutro o tym czasie do Jizreel. A synów królewskich było siedemdziesięciu mężczyzn, przebywających u znakomitych obywateli miasta, którzy ich wychowywali.
Ndipo Yehu anawalembera kalata yachiwiri yonena kuti, “Ngati inu muli mbali yanga ndi kuti mudzandimvera, mudule mitu ya ana a mbuye wanu ndipo mubwere nayo kwa ine ku Yezireeli mawa nthawi ngati yomwe ino.” Tsono ana a mfumu onse 70 anali pamodzi ndi akuluakulu a mu mzindamo, amene ankawalera.
7 A gdy doszedł do nich list, wzięli synów królewskich, zabili wszystkich siedemdziesięciu, włożyli ich głowy do koszy i posłali je do niego do Jizreel.
Kalatayo itafika, anthuwo anatenga ana a mfumu 70 aja ndi kuwapha onse. Anayika mitu yawo mʼmadengu ndi kuyitumiza ku Yezireeli kwa Yehu.
8 Posłaniec przyszedł i oznajmił mu: Przyniesiono głowy synów królewskich. A [on] powiedział: Ułóżcie je w dwa stosy u wejścia bramy – aż do poranku.
Mthenga uja atafika, anamuwuza Yehu kuti, “Abweretsa mitu ya ana a mfumu.” Ndipo Yehu analamula kuti, “Unjikani mituyo mʼmilu iwiri pa chipata cha mzinda ndipo ikhale pamenepo mpaka mmawa.”
9 Rano zaś wyszedł, stanął i przemówił do całego ludu: Jesteście sprawiedliwi. Oto uknułem spisek przeciw swemu panu i zabiłem go, ale kto zabił tych wszystkich?
Mmawa mwake Yehu anatuluka. Iye anayimirira pamaso pa anthu onse ndipo anati, “Inu ndinu osalakwa. Ndine amene ndinachita chiwembu mbuye wanu ndi kumupha, koma kodi wapha anthu onsewa ndani?
10 Wiedzcie teraz, że nie upadnie na ziemię [nic] ze słowa PANA, które PAN wypowiedział przeciwko domowi Achaba. PAN bowiem uczynił to, co wypowiedział przez swego sługę Eliasza.
Koma dziwani tsono, kuti mawu amene Yehova anayankhula kunena za banja la Ahabu sadzapita padera. Yehova wachita chimene analonjeza kudzera mwa mtumiki wake Eliya.”
11 Jehu więc zabił wszystkich, którzy pozostali z domu Achaba w Jizreel, wszystkich jego możnych, jego bliskich i jego kapłanów, tak że nie zostawił spośród nich żadnego przy życiu.
Choncho Yehu anapha onse amene anatsala a mʼbanja la Ahabu ku Yezireeli, pamodzinso ndi akuluakulu ake onse, abwenzi ake ndiponso ansembe ake, sanasiyeko ndi mmodzi yemwe wamoyo.
12 Potem wstał, odszedł i wyruszył do Samarii. Po drodze, [gdy] był w domu, gdzie pasterze strzygli owce;
Kenaka Yehu ananyamuka kupita ku Samariya. Atafika pa malo otchedwa Beti-Ekedi wa abusa,
13 Jehu spotkał braci Achazjasza, króla Judy, i zapytał: Kim jesteście? Odpowiedzieli: Jesteśmy braćmi Achazjasza i idziemy pozdrowić synów króla i synów królowej.
Yehu anakumana ndi abale ena a Ahaziya mfumu ya Yuda nawafunsa kuti, “Kodi ndinu yani?” Iwo anayankha kuti, “Ndife abale ake a Ahaziya, ndipo tabwera kulonjera banja la mfumu ndi ana a mfumukazi.”
14 Wtedy rozkazał: Pojmijcie ich żywcem. I pojmali ich żywcem, i zabili przy studni tego domu, gdzie strzyżono owce [w liczbie] czterdziestu dwóch mężczyzn. Nie oszczędził żadnego z nich.
Yehu analamula kuti, “Atengeni amoyo!” Choncho anawatenga amoyo ndipo anakawaphera ku chitsime cha ku malo otchedwa Beti-Ekedi wa abusa; anthu onse 42. Iye sanasiyepo ndi mmodzi yemwe wamoyo.
15 Potem odjechał stamtąd i spotkał Jonadaba, syna Rechaba, idącego mu naprzeciw. Pozdrowił go i zapytał: Czy twoje serce jest tak szczere jak moje serce wobec twojego serca? Jonadab odpowiedział: Jest. A jeśli jest, to daj mi swoją rękę. Wtedy dał mu swą rękę i wziął go do siebie na rydwan.
Yehu atachoka kumeneko anakumana ndi Yehonadabu mwana wa Rekabu, amene amabwera kudzakumana naye. Yehu anamulonjera nati kwa iye, “Kodi mtima wako uli bwino monga momwe mtima wanga ugwirizana nawo mtima wako?” Yehonadabu anayankha kuti, “Inde ndikugwirizana nawe.” Yehu anati, “Ngati ndi choncho, gwire dzanja.” Ndipo iye anaterodi, ndipo Yehu anamugwira dzanja namulowetsa mʼgaleta lake.
16 Potem powiedział: Jedź ze mną i zobaczysz moją gorliwość dla PANA. I wiózł go na swoim rydwanie.
Yehu anati, “Tiye kuno uwone mmene ndikudziperekera kwa Yehova.” Ndipo anayenda naye mʼgaleta mwake.
17 A gdy przyjechał do Samarii, zabił wszystkich, którzy pozostali [z domu] Achaba w Samarii, i wytracił ich według słowa PANA, które wypowiedział do Eliasza.
Yehu atafika ku Samariya, anapha onse amene anatsala a mʼbanja la Ahabu ku Samariya; anawawonongeratu potsata mawu a Yehova amene anayankhula kudzera mwa Eliya.
18 Potem Jehu zebrał cały lud i powiedział do niego: Achab mało służył Baalowi, Jehu będzie mu służył bardziej.
Ndipo Yehu anasonkhanitsa anthu onse pamodzi nawawuza kuti, “Ahabu ankatumikira Baala pangʼono chabe; Yehu adzamutumikira kwambiri.
19 Teraz więc zwołajcie do mnie wszystkich proroków Baala, wszystkie jego sługi i wszystkich jego kapłanów, niech nikogo nie zabraknie. Złożę bowiem wielką ofiarę Baalowi. Ktokolwiek się nie stawi, nie pozostanie przy życiu. Lecz Jehu działał podstępnie, chcąc wytracić czcicieli Baala.
Tsopano itanani aneneri a Baala onse, atumiki ake onse ndi ansembe ake onse. Pasapezeke ndi mmodzi yemwe wotsala chifukwa ine ndidzapereka nsembe yayikulu kwa Baala. Aliyense amene alephere kubwera adzaphedwa.” Koma Yehu anachita zimenezi mwachinyengo ndi cholinga choti awononge atumiki onse a Baala.
20 Jehu dalej rozkazał: Ogłoście święto dla Baala. I obwołano [je].
Yehu anati, “Itanitsani msonkhano wodzalemekeza Baala.” Ndipo analengeza za msonkhanowo.
21 Potem Jehu rozesłał posłańców po całym Izraelu. I zeszli się wszyscy czciciele Baala, tak że nie było [spośród nich] nikogo, kto by nie przyszedł. Weszli do domu Baala i wypełnił się dom Baala od krańca aż do krańca.
Pamenepo Yehu anatumiza mawu ku dziko lonse la Israeli ndipo atumiki onse a Baala anabwera; palibe ndi mmodzi yemwe amene anatsala. Iwo anadzaza nyumba ya Baala. Nyumbayo inadzaziratu kuchokera ku khoma lina mpaka ku khoma lina.
22 Następnie powiedział przełożonemu szatni: Wyłóż szaty dla wszystkich czcicieli Baala. I wyłożył dla nich szaty.
Ndipo Yehu anawuza munthu wosunga mikanjo kuti, “Bweretsa mikanjo yokwanira atumiki onse a Baala.” Ndipo iye anabweretsa mikanjoyo.
23 Wtedy Jehu wraz z Jonadabem, synem Rechaba, wszedł do domu Baala i powiedział czcicielom Baala: Zbadajcie i upewnijcie się, że nie ma z wami nikogo z czcicieli PANA, ale tylko czciciele Baala.
Kenaka Yehu ndi Yehonadabu mwana wa Rekabu analowa mʼnyumba ya Baala. Yehu anawawuza atumiki a Baala kuti, “Yangʼanitsitsani ndipo muone kuti muno musapezeke atumiki a Yehova, koma mukhale atumiki okhawo a Baala.”
24 Weszli więc, aby złożyć ofiary i całopalenia. Lecz Jehu postawił sobie na zewnątrz osiemdziesięciu mężczyzn, którym powiedział: Jeśli ujdzie ktokolwiek z tego ludu, który wydaję w wasze ręce, to wasze życie będzie [zapłatą] za jego życie.
Choncho Yehu analowa kukapereka nsembe zina ndi nsembe zopsereza. Nthawi iyi nʼkuti Yehu atayika anthu 80 kunja kwa nyumbayo ndi chenjezo lakuti, “Ngati wina aliyense wa inu adzathawitsa wina aliyense wa anthu amene ndayika kuti muziwayangʼanira, munthu woteroyo adzaphedwa.”
25 A gdy dokończono składanie całopalenia, Jehu powiedział żołnierzom i dowódcom: Wejdźcie i zabijajcie ich, [aby] nikt nie uszedł. Zabili więc [ich] ostrzem miecza i żołnierze i dowódcy powyrzucali ich. Potem poszli do miasta domu Baala.
Yehu atangotsiriza kupereka nsembe yopsereza, analamula alonda ndi akulu a ankhondo kuti, “Lowani ndipo mukawaphe ndipo musalole kuti wina athawe.” Choncho iwo anawapha ndi lupanga. Alonda ndi akulu a ankhondo anaponya mitembo ya anthuwo panja ndipo anakalowa mʼkati mwenimweni mwa nyumba ya Baala.
26 Wyrzucili posągi z domu Baala i spalili je.
Iwo anakatulutsa mwala wopatulika umene unali mʼnyumba ya Baala ndipo anawutentha.
27 Rozbili też posąg Baala, zburzyli dom Baala i uczynili z niego wychodek, [i jest tak] aż do dziś.
Anawononga mwala wopatulika wa Baala ndi kugwetsa nyumba ya Baala, ndipo anthu anayisandutsa chimbudzi mpaka lero lino.
28 W ten sposób Jehu wytępił Baala z Izraela.
Motero Yehu anawononga Baala mu Israeli.
29 Nie odstąpił jednak od grzechów Jeroboama, syna Nebata, który do grzechu przywiódł Izraela – od złotych cielców, które [były] w Betel i w Dan.
Koma Yehuyo sanaleke machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati amene anachimwitsa nawo Israeli kupembedza mafano a golide a ana angʼombe ku Beteli ndi ku Dani.
30 Wtedy PAN powiedział do Jehu: Ponieważ dobrze postąpiłeś, wykonując to, co słuszne w moich oczach, i uczyniłeś domowi Achaba według wszystkiego, co było w moim sercu, to twoi synowie aż do czwartego pokolenia będą zasiadać na tronie Izraela.
Yehova anati kwa Yehu, “Chifukwa wachita bwino pokwaniritsa kuchita zabwino pamaso panga ndipo wachitira banja la Ahabu zonse zimene zinali mʼmaganizo anga, zidzukulu zako zidzakhala pa mpando waufumu wa Israeli mpaka mʼbado wachinayi.”
31 Lecz Jehu nie pilnował [tego], aby postępować z całego swego serca według prawa PANA, Boga Izraela. Nie odstąpił od grzechów Jeroboama, który przywiódł Izraela do grzechu.
Komatu Yehu sanasamalire kusunga lamulo la Yehova Mulungu wa Israeli ndi mtima wake wonse. Iyeyo sanaleke machimo a Yeroboamu amene anachimwitsa nawo Israeli.
32 W tych dniach PAN zaczął umniejszać Izrael: Chazael pobił ich na całym obszarze Izraela;
Masiku amenewo Yehova anayamba kuchepetsa dziko la Israeli. Hazaeli anagonjetsa Aisraeli,
33 Od Jordanu ku wschodowi, całą ziemię Gileadu, Gadytów, Rubenitów i Manassytów, od Aroeru, który leży nad rzeką Arnon – Gilead i Baszan.
kuyambira kummawa kwa Yorodani, dziko lonse la Giliyadi (chigawo cha Gadi, Rubeni ndi Manase), kuchokera ku Aroeri pafupi ndi chigwa cha Arinoni kudutsa Giliyadi mpaka ku Basani.
34 A pozostałe dzieje Jehu i wszystko, co czynił, cała jego potęga, czy nie są zapisane w kronikach królów Izraela?
Ntchito zina za Yehu ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a ku Israeli?
35 I Jehu zasnął ze swymi ojcami, i pogrzebano go w Samarii. A w jego miejsce królował jego syn Jehoachaz.
Yehu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake ku Samariya. Ndipo Yehowahazi mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
36 A czas, w którym Jehu królował nad Izraelem w Samarii, [wynosił] dwadzieścia osiem lat.
Yehu analamulira Aisraeli ku Samariya zaka 28.