< II Koryntian 7 >

1 Mając więc te obietnice, najmilsi, oczyśćmy się z wszelkiego brudu ciała i ducha, dopełniając uświęcenia w bojaźni Bożej.
Abwenzi okondedwa, popeza tili ndi malonjezo amenewa, tiyeni tidziyeretse, kusiyana nazo zilizonse zimene zikhoza kudetsa thupi ndi mzimu, ndipo tiyesetse kukhala oyera mtima poopa Mulungu.
2 Przyjmijcie nas; nikogo nie skrzywdziliśmy, nikogo nie zepsuliśmy, nikogo nie wykorzystaliśmy.
Mutipatse malo mʼmitima mwanu. Ife sitinalakwire munthu aliyense, kapena kuyipitsa munthu aliyense, kapena kumuchenjerera munthu aliyense.
3 Nie mówię [tego], aby was potępiać; wcześniej bowiem powiedziałem, że jesteście w naszych sercach na wspólną śmierć i wspólne życie.
Sindikunena izi kuti mupezeke olakwa. Ndinanena kale kuti ife timakuganizirani kwambiri kotero kuti tili pamodzi, ngakhale tikhale moyo kapena timwalire.
4 Mam wielką swobodę w mówieniu do was, bardzo się wami chlubię, jestem pełen pociechy, obfituję w radość w każdym naszym ucisku.
Ndimakukhulupirirani kwambiri ndipo ndimakunyadirani kwambiri. Ndikulimbikitsidwa kwambiri; mʼmasautso athu onse, chimwemwe changa chilibe malire.
5 Kiedy bowiem przybyliśmy do Macedonii, nasze ciało nie zaznało żadnego odpoczynku, ale zewsząd [byliśmy] uciśnieni: na zewnątrz walki, a wewnątrz obawy.
Pakuti titafika ku Makedoniya, sitinapume nʼkomwe, koma tinavutitsidwa mbali zonse. Kunja kunali mikangano, ndipo mʼmitima mwathu munali mantha.
6 Lecz Bóg, który pociesza uniżonych, pocieszył nas przez przybycie Tytusa.
Koma Mulungu, amene amatonthoza mtima wopsinjika, anatitonthoza mtima ndi kufika kwa Tito,
7 A nie tylko przez jego przybycie, ale też przez pociechę, jakiej doznał wśród was, gdy opowiedział nam o waszej tęsknocie, o waszym płaczu, o waszej gorliwości względem mnie, tak że uradowałem się jeszcze bardziej.
sikubwera kwake kokhako, komanso mawu achilimbikitso amene analandira kuchokera kwa inu. Iye anatiwuza kuti mukufuna kundiona, zachisoni chanu chachikulu, ndi kudzipereka kwanu kwa ine, motero chimwemwe changa chinachuluka kuposa kale.
8 Choć bowiem zasmuciłem was listem, nie żałuję [tego], a mimo że żałowałem (bo widzę, że ten list zasmucił was, chociaż tylko na chwilę);
Ngakhale kalata yanga ija inakupwetekani mtima, sindikudandaula kuti ndinalemberanji. Ngakhale zinandikhudza, ndikudziwa kuti kalata yanga inakupwetekani, koma kwa kanthawi kochepa.
9 [To] teraz się raduję, nie dlatego, że byliście zasmuceni, ale że byliście zasmuceni ku pokucie. Zostaliście bowiem zasmuceni według Boga, żebyście w niczym nie ponieśli szkody przez nas.
Koma tsopano ndine wokondwa, osati chifukwa chakuti kalatayo inakupwetekani, koma chifukwa chakuti chisoni chanu chinakuthandizani kutembenuka mtima. Pakuti munamva chisoni monga mmene Mulungu amafunira, choncho simunapwetekedwe mwanjira iliyonse.
10 Bo smutek, [który jest] według Boga, przynosi pokutę ku zbawieniu, czego nikt nie żałuje; lecz smutek [według] świata przynosi śmierć.
Chisoni chimene Mulungu amafuna chimabweretsa kutembenuka mtima komwe kumabweretsa chipulumutso, ndipo sichikhumudwitsa. Koma chisoni cha dziko lapansi chimabweretsa imfa.
11 To bowiem, że byliście zasmuceni według Boga, jakąż wielką wzbudziło w was pilność, jakie uniewinnianie się, jakie oburzenie, jaką bojaźń, jaką tęsknotę, jaką gorliwość, jakie wymierzenie kary! We wszystkim okazaliście się czyści w tej sprawie.
Taonani zimene chisoni chimene Mulungu amafuna chatulutsa mwa inu. Chatulutsa khama lalikulu, chakuthandizani kuti mudzikonze nokha, chakukwiyitsani kwambiri, komanso chakupatsani mantha aakulu. Chakuchititsani kuti mufune kundiona ine, mwakhudzidwa kwambiri ndipo mukufuna kuonetsetsa kuti chilungamo chachitikadi. Pa nkhani yonseyi, mwaonetsadi kuti ndinu osalakwa.
12 Dlatego chociaż pisałem do was, nie [pisałem] z powodu tego, który wyrządził krzywdę, ani z powodu tego, który krzywdy doznał, lecz aby okazać nasze zatroskanie o was przed Bogiem.
Choncho ngakhale ndinakulemberani kalata ija, sindinayilembe ndi chifukwa cha amene analakwayo kapena wolakwiridwa, koma ndinayilemba kuti inuyo muone kudzipereka kwanu kwa ife pamaso a Mulungu.
13 Tak więc zostaliśmy pocieszeni waszą pociechą. A jeszcze bardziej uradowaliśmy się radością Tytusa, bo jego duch został pokrzepiony przez was wszystkich.
Zimenezi zatilimbikitsa kwambiri. Kuwonjezera pa zotilimbikitsazo, tinakondwa kwambiri poona chisangalalo cha Tito, chifukwa nonsenu munamuthandiza kukhazikitsa mtima wake pansi.
14 Bo jeśli w czymś chlubiłem się wami przed nim, nie zostałem zawstydzony. Lecz tak, jak mówiliśmy wam wszystko zgodnie z prawdą, tak też nasza chluba przed Tytusem okazała się prawdziwa.
Ndinamuwuza kuti ndimakunyadirani, ndipo simunandichititse manyazi. Koma monga zonse zimene tinakuwuzani zinali zoona, tsono zomwe ndinawuza Tito zokunyadirani zinali zoona.
15 A jego serce jeszcze bardziej [skłania się] ku wam, gdy wspomina posłuszeństwo was wszystkich [i] to, jak przyjęliście go z bojaźnią i drżeniem.
Ndipo chikondi chake pa inu nʼchachikulu kwambiri akakumbukira kuti nonse munali omvera, munamulandira ndi mantha ndi kunjenjemera.
16 Raduję się więc, że we wszystkim mogę wam ufać.
Ndine wokondwa kuti ndingathe kukukhulupirirani pa zonse.

< II Koryntian 7 >