< II Kronik 36 >
1 Wtedy lud ziemi wziął Jehoachaza, syna Jozjasza, i ustanowił go królem w miejsce jego ojca w Jerozolimie.
Tsono anthu a mʼdzikomo anatenga Yehowahazi mwana wa Yosiya namuyika kukhala mfumu mu Yerusalemu mʼmalo mwa abambo ake.
2 Jehoachaz miał dwadzieścia trzy lata, kiedy zaczął królować, i królował trzy miesiące w Jerozolimie.
Yowahazi anali wa zaka 23 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa miyezi itatu.
3 Król Egiptu usunął go [z tronu] w Jerozolimie i nałożył na ziemię daninę [w wysokości] stu talentów srebra i jednego talentu złota.
Mfumu ya Igupto inamuchotsa pa udindo wa ufumu mu Yerusalemu ndipo inakhometsa msonkho dziko la Yuda wa makilogalamu 3,400 asiliva ndi agolide.
4 Potem król Egiptu ustanowił Eliakima, jego brata, królem nad Judą i Jerozolimą i zmienił jego imię na Joakim. A jego brata Jehoachaza Necho pojmał i uprowadził do Egiptu.
Mfumu ya Igupto inakhazika Eliyakimu, mʼbale wake wa Yehowahazi kukhala mfumu ya Yuda ndi Yerusalemu ndipo anasintha dzina la Eliyakimu kukhala Yehoyakimu. Koma Neko anatenga Yowahazi mʼbale wake wa Eliyakimu ndi kupita naye ku Igupto.
5 Joakim miał dwadzieścia pięć lat, kiedy zaczął królować, i królował jedenaście lat w Jerozolimie. Czynił on to, co złe w oczach PANA, swego Boga.
Yehoyakimu anali wa zaka 25 pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 11. Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova Mulungu wake.
6 Nadciągnął przeciw niemu Nabuchodonozor, król Babilonu, i związał go łańcuchami, aby go uprowadzić do Babilonu.
Nebukadinezara, mfumu ya ku Babuloni anachita naye nkhondo ndipo anamumanga ndi zingwe zamkuwa ndi kumutenga kupita naye ku Babuloni.
7 Nabuchodonozor zabrał też do Babilonu [część] naczyń z domu PANA i złożył je w swojej świątyni w Babilonie.
Nebukadinezara anatenganso zipangizo za ku Nyumba ya Yehova kupita nazo ku Babuloni ndipo anaziyika mʼnyumba ya Mulungu wake kumeneko.
8 A pozostałe dzieje Joakima i obrzydliwości, które czynił, i cokolwiek się znajdowało w nim, są zapisane w księdze królów Izraela i Judy. A jego syn Joachin królował w jego miejsce.
Zochitika zina za pa ulamuliro wa Yehoyakimu, zinthu zonyansa zimene anachita ndi zonse zinapezeka kuti zinali zomutsutsa zalembedwa mʼbuku la mafumu a Israeli ndi Yuda. Ndipo Yehoyakini mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
9 Joachin miał osiem lat, kiedy zaczął królować, i królował trzy miesiące i dziesięć dni w Jerozolimie. Czynił on to, co złe w oczach PANA.
Yehoyakini anali ndi zaka 21 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa miyezi itatu ndi masiku khumi. Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova.
10 Na początku roku król Nabuchodonozor posłał [po niego] i kazał go przyprowadzić do Babilonu, razem z kosztownymi naczyniami domu PANA, a królem nad Judą i Jerozolimą ustanowił jego brata Sedekiasza.
Nthawi ya mphukira, mfumu Nebukadinezara inayitanitsa Yehoyakini ndipo inapita naye ku Babuloni, pamodzi ndi ziwiya zamtengowapatali za mʼNyumba ya Mulungu wa Yehova, ndipo anayika Zedekiya malume wake kukhala mfumu ya Yuda ndi Yerusalemu.
11 Sedekiasz miał dwadzieścia jeden lat, kiedy zaczął królować, i królował jedenaście lat w Jerozolimie.
Zedekiya anali ndi zaka 21 pamene ankakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 11.
12 Czynił on to, co złe w oczach PANA, swego Boga, i nie ukorzył się przed prorokiem Jeremiaszem, [który mówił] z ust PANA.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova Mulungu wake ndipo sanadzichepetse yekha pamaso pa mneneri Yeremiya amene ankayankhula mawu a Yehova.
13 Zbuntował się również przeciwko królowi Nabuchodonozorowi, który go zaprzysiągł na Boga. Uczynił twardym swój kark i zatwardził swoje serce, aby się nie nawrócić do PANA, Boga Izraela.
Iye anawukiranso mfumu Nebukadinezara amene anamulumbiritsa mʼdzina la Mulungu. Iyeyo anali wosamva ndipo anawumitsa mtima wake. Sanatembenukire kwa Yehova Mulungu wa Israeli.
14 Również wszyscy przedniejsi kapłani oraz lud bardzo mnożyli nieprawości, naśladując wszystkie obrzydliwości pogan, i zbezcześcili dom PANA, który on poświęcił w Jerozolimie.
Kuwonjezera apo, atsogoleri onse a ansembe ndi anthu ena anapitirapitira kukhala osakhulupirika, kutsatira machitidwe onse onyansa a mitundu ina ndi kudetsa Nyumba ya Yehova Mulungu wawo, imene anayipatula mu Yerusalemu.
15 A PAN, Bóg ich ojców, posyłał do nich swoich posłańców, a posyłał, wstając rankiem, ponieważ litował się nad swoim ludem i nad miejscem swego przybytku.
Yehova, Mulungu wa makolo awo, ankatumiza mawu kwa iwo kudzera kwa amithenga ake kawirikawiri, chifukwa ankawamvera chisoni anthu ake ndi malo ake okhalapo.
16 Ale oni szydzili z posłańców Boga, lekceważyli sobie jego słowa i naśmiewali się z jego proroków, aż gniew PANA na jego lud wzmógł się tak, że nie było już żadnego ratunku.
Koma iwo ananyoza amithenga a Mulungu, anapeputsa mawu awo ndipo ankaseka aneneri ake mpaka anawutsa mkwiyo wa Yehova pa anthu ake ndipo panalibenso mankhwala owachiritsa.
17 Sprowadził więc na nich króla Chaldejczyków, który zabił mieczem ich młodzieńców w domu ich świątyni, a nie zlitował się nad młodzieńcem ani panną, ani starcem, ani sędziwym. Wydał wszystkich w jego ręce.
Yehova anabweretsa mfumu ya anthu a ku Babuloni, imene inapha anyamata awo ndi lupanga ku malo opatulika, ndipo sanasiye kaya mnyamata kapena mtsikana, wamkulu kapena wokalamba. Mulungu anapereka onsewo kwa Nebukadinezara.
18 Wszystkie naczynia domu Bożego, wielkie i małe, skarby domu PANA i skarby królewskie, i jego książąt, wszystko to wywiózł do Babilonu.
Iye ananyamula kupita nazo ku Babuloni zipangizo zonse za mʼNyumba ya Yehova Mulungu wawo, zazikulu ndi zazingʼono zomwe, ndi chuma cha mʼNyumba ya Yehova ndiponso chuma cha mfumu ndi akuluakulu ake.
19 Potem spalili dom Boży i zburzyli mur Jerozolimy; wszystkie jej pałace spalili ogniem i wszystkie jej kosztowne naczynia zniszczyli.
Iwo anayatsa moto Nyumba ya Mulungu, ndipo anagwetsa makoma a Yerusalemu. Anatentha moto nyumba zonse zaufumu ndipo anawononga chilichonse chimene chinali chofunika.
20 A tych, którzy ocaleli od miecza, [król] uprowadził do Babilonu, tam byli niewolnikami jego i jego synów aż do panowania króla Persji;
Iye anagwira ukapolo anthu otsala amene anapulumuka ku lupanga ndi kupita nawo ku Babuloni, ndipo anakhala antchito ake ndi ana ake mpaka pamene ufumu wa Peresiya unakhazikitsidwa.
21 Żeby wypełniło się słowo PANA [wypowiedziane] przez usta Jeremiasza, dopóki ziemia nie odprawiła swoich szabatów. Dopóki [bowiem] ziemia leżała odłogiem, wypełniła szabaty, aż się wypełniło siedemdziesiąt lat.
Dziko linakondwera ndi masabata ake. Pa nthawi yonse ya chipasuko chake nthaka inapuma, mpaka zaka 70 zinakwana pokwaniritsa mawu a Yehova amene anayankhula kudzera mwa Yeremiya.
22 A w pierwszym roku Cyrusa, króla Persji – żeby wypełniło się słowo PANA [wypowiedziane] przez usta Jeremiasza – PAN wzbudził ducha Cyrusa, króla Persji, aby nakazał ogłosić i rozpisać po całym swoim królestwie, co następuje:
Mʼchaka choyamba cha Koresi mfumu ya Peresiya, pofuna kukwaniritsa mawu a Yehova amene anayankhula kudzera mwa Yeremiya, Yehova anakhudza mtima wa mfumu ya Peresiya kuti alengeze mu ufumu wake wonse ndipo anazilemba:
23 Tak mówi Cyrus, król Persji: Wszystkie królestwa ziemi dał mi PAN, Bóg nieba, i on rozkazał mi, abym mu zbudował dom w Jerozolimie, która jest w Judzie. Kto z całego jego ludu [jest] wśród was, niech PAN, jego Bóg, będzie z nim, i ten niech wyrusza w drogę.
Chimene mfumu Koresi ya Peresiya ikunena ndi ichi: “Yehova, Mulungu wakumwamba wandipatsa ine mafumu onse a dziko lapansi ndipo wandisankha kuti ndimumangire Nyumba ya Mulungu ku Yerusalemu ku Yuda. Aliyense wa anthu ake pakati panu, Yehova Mulungu wake akhale naye, ndipo apite.”