< II Kronik 26 >

1 Wtedy cały lud Judy wziął Uzjasza, który miał szesnaście lat, i ustanowił go królem w miejsce jego ojca Amazjasza.
Kenaka anthu onse a ku Yuda anatenga Uziya amene anali wa zaka 16, namuyika kukhala mfumu mʼmalo mwa Amaziya abambo ake.
2 Ten odbudował Elat i przywrócił go do Judy, kiedy król już zasnął ze swoimi ojcami.
Iye anamanganso mzinda wa Eloti ndi kuwubwezeranso ku Yuda abambo ake atamwalira.
3 Uzjasz miał szesnaście lat, kiedy zaczął królować, i królował pięćdziesiąt dwa lata w Jerozolimie. Jego matka miała na imię Jekolia, [była] z Jerozolimy.
Uziya anali wa zaka 16 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 70. Dzina la amayi ake linali Yekoliya wa ku Yerusalemu.
4 Czynił on to, co prawe w oczach PANA, według wszystkiego, co czynił jego ojciec Amazjasz.
Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Amaziya abambo ake.
5 I szukał Boga, dopóki żył Zachariasz, który miał rozeznanie w widzeniach Bożych. A przez te wszystkie dni, kiedy szukał PANA, Bóg darzył go powodzeniem.
Iye anapembedza Mulungu nthawi ya Zekariya, amene ankamulangiza za kuopa Mulungu amene anamupatsa chipambano.
6 Wyruszył do walki z Filistynami, zburzył mury Gat, Jabne i Aszdodu, a odbudował miasta w okolicy Aszdodu i [w ziemi] Filistynów.
Iyeyo anapita kukachita nkhondo ndi Afilisti ndipo anagwetsa makoma a Gati, Yabine ndi Asidodi. Ndipo kenaka anamanganso mizinda ya pafupi ndi Asidodi ndi malo ena pafupi ndi Afilisti.
7 Wspomagał go bowiem Bóg [przeciw] Filistynom i Arabom, którzy mieszkali w Gur-Baal, i przeciw Meunitom.
Mulungu anamuthandiza polimbana ndi Afilisti ndi Aarabu amene amakhala ku Guri-Baala ndiponso polimbana ndi Ameuni.
8 Ammonici dawali Uzjaszowi daniny, a [sława] jego imienia rozeszła się aż do wejścia do Egiptu, bo wielce się umocnił.
Aamoni ankabweretsa msonkho kwa Uziya ndipo mbiri yake inamveka mpaka ku malire a dziko la Igupto chifukwa anali wamphamvu kwambiri.
9 I Uzjasz zbudował wieże w Jerozolimie nad Bramą Narożną, nad Bramą Doliny i nad Narożnikiem i umocnił je.
Uziya anamanga nsanja ku Yerusalemu ku Chipata Chapangodya, ku Chigwa cha Chipata ndi pokhotera mpanda, ndipo anayikamo chitetezo.
10 Zbudował też wieże na pustyni i wykopał wiele studni, ponieważ miał bardzo dużo stad, zarówno w dolinach, jak i na równinach, także rolników i uprawiających winnice na górach i na Karmelu. Był bowiem rozmiłowany w uprawie ziemi.
Iye anamanganso nsanja ku chipululu ndi kukumbanso zitsime zambiri chifukwa anali ndi ziweto zambiri mʼmbali mwa phiri ndi ku zigwa. Iye anali ndi anthu amene ankagwira ntchito mʼminda yake ndiponso mʼminda yake ya mphesa mʼphiri ndi malo achonde, pakuti ankakonda nthaka.
11 Uzjasz miał też wojsko [gotowe] do bitwy, które wyruszało na wojnę w odliczonych oddziałach, według spisu dokonanego przez pisarza Jejela i urzędnika Maasejasza, pod nadzorem Chananiasza, [jednego] z dowódców króla.
Uziya anali ndi gulu lankhondo lophunzitsidwa bwino, lokonzekera kupita ku nkhondo mʼmagulu monga mwa chiwerengero chawo chimene mlembi Yeiyeli ndi Maaseya anasonkhanitsa motsogozedwa ndi Hananiya mmodzi mwa akuluakulu a mfumu.
12 Całkowita liczba naczelników rodów [postawionych] nad dzielnymi wojownikami wynosiła dwa tysiące sześciuset.
Chiwerengero chonse cha atsogoleri a mʼmabanja oyangʼanira anthu ochita nkhondo chinali 2,600.
13 A pod ich rozkazami [stało] wojsko [złożone z] trzystu siedmiu tysięcy pięciuset wojowników gotowych do wojny z wielką siłą, aby wesprzeć króla przeciw wrogowi.
Pansi pa ulamuliro wawo panali asilikali 307,500 ophunzitsidwa nkhondo, gulu lamphamvu lothandiza mfumu kulimbana ndi adani ake.
14 Uzjasz przygotował całemu wojsku tarcze, włócznie, hełmy, pancerze, łuki oraz kamienie do proc.
Uziya anawapangira asilikaliwo zishango, mikondo, zipewa zankhondo, malaya ankhondo achitsulo, mauta ndi miyala yogendera.
15 Sporządził w Jerozolimie machiny wojenne wymyślone przez zdolnych ludzi, aby stały na wieżach i na narożnikach w celu ciskania strzał i wielkich kamieni. Jego sława rozeszła się daleko, ponieważ doznawał cudownej pomocy, aż stał się potężny.
Mu Yerusalemu anapanga makina okonzedwa ndi anthu aluso amene amagwiritsidwa ntchito pa malo otetezera a pa nsanja ndi pa ngodya kuponyera mivi ndi kugubuduzira miyala. Mbiri yake inamveka kutali ndi ponseponse pakuti anathandizidwa kwambiri mpaka anakhala wamphamvu kwambiri.
16 Ale kiedy się umocnił, uniosło się jego serce ku jego własnej zgubie. Zgrzeszył przeciw PANU, swemu Bogu, gdyż wszedł do świątyni PANA, aby palić kadzidło na ołtarzu kadzenia.
Koma pamene Uziya anakhala wamphamvu kwambiri, kunyada kwake kunamuwononga. Iye sanakhulupirike kwa Yehova Mulungu wake, ndipo analowa mʼNyumba ya Yehova kukafukiza lubani pa guwa lofukizira.
17 Wszedł za nim kapłan Azariasz, a z nim osiemdziesięciu kapłanów PANA, odważnych mężczyzn.
Wansembe Azariya pamodzi ndi ansembe a Yehova ena 80 olimba mtima anamutsatira.
18 I sprzeciwili się królowi Uzjaszowi, i powiedzieli mu: Nie do ciebie, Uzjaszu, należy palenie kadzidła PANU, lecz do kapłanów, synów Aarona, którzy są poświęceni, aby palić kadzidło. Wyjdź ze świątyni. Zgrzeszyłeś bowiem i nie [przynosi ci] to chwały od PANA Boga.
Iwo anatsutsana naye ndipo anati, “Sibwino kuti inu mfumu muzifukiza lubani koma zidzukulu za Aaroni, zimene zinapatulidwa kuti zizifukiza lubani. Chokani pa malo opatulika ano, pakuti inu mwakhala osakhulupirika, ndipo simudzalemekezedwa ndi Yehova Mulungu.”
19 Wtedy Uzjasz rozgniewał się, mając w ręku kadzielnicę, by spalić kadzidło. A gdy pałał gniewem na kapłanów, pojawił się trąd na jego czole przed kapłanami w domu PANA, przy ołtarzu kadzenia.
Uziya, amene anali ndi chofukizira mʼmanja mwake wokonzeka kuti afukize lubani, anapsa mtima. Iye anakwiyira ansembewo. Ndipo ansembe aja akuona patsogolo pa guwa lofukizira lubani mʼNyumba ya Mulungu, khate linayamba pamphumi pake.
20 Kiedy najwyższy kapłan Azariasz i wszyscy kapłani spojrzeli na niego, oto miał trąd na czole. Wypchnęli go więc stamtąd, a i on sam spieszył się z wyjściem, bo dotknął go PAN.
Azariya, mkulu wa ansembe pamodzi ndi ansembe ena onse atamuyangʼana anaona kuti anali ndi khate pamphumi pake, ndipo anamutulutsa mofulumira. Ndipo iye mwini anafulumira kutuluka, chifukwa Yehova anamulanga.
21 I tak król Uzjasz był trędowaty aż do dnia swojej śmierci i jako trędowaty mieszkał w domu odosobnienia. Został bowiem wyłączony z domu PANA. W tym czasie jego syn Jotam zarządzał domem królewskim i sądził lud ziemi.
Mfumu Uziya anali ndi khate mpaka tsiku limene anamwalira. Iye amakhala mʼnyumba ya yekha ngati wakhate, ndipo samalowa mʼNyumba ya Yehova. Yotamu mwana wake ndiye amayangʼanira nyumba yaufumu ndipo ankalamulira anthu a mʼdzikomo.
22 A pozostałe dzieje Uzjasza, od pierwszych do ostatnich, opisał prorok Izajasz, syn Amosa.
Ntchito zina za mfumu Uziya, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zinalembedwa ndi mneneri Yesaya mwana wa Amozi.
23 Zasnął więc Uzjasz ze swoimi ojcami i pogrzebali go z nimi na polu grobów królewskich, gdyż mówili: Trędowaty jest. A jego syn Jotam królował w jego miejsce.
Uziya analondola makolo ake, ndipo anamuyika pamodzi ndi makolo ake ku malo a manda a mafumu, koma osati mʼmanda mwawomo poti anthu anati, “Iyeyu anali ndi khate.” Ndipo Yotamu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

< II Kronik 26 >