< I Samuela 3 >

1 A chłopiec Samuel służył PANU przed Helim. W tych dniach słowo PANA było drogocenne i nie było jawnego widzenia.
Samueli ankatumikira Yehova moyangʼaniridwa ndi Eli. Masiku amenewo mawu a Yehova sankamveka pafupipafupi. Kuona zinthu mʼmasomphenya sikunkachitikanso kawirikawiri.
2 Pewnego dnia, gdy Heli leżał na swoim miejscu, a jego oczy już zaczęły słabnąć i nie mógł widzieć;
Tsiku lina Eli, amene maso anali ofowoka ndi kuti sankatha kuona bwino, anagona pa malo ake.
3 A lampa Boża jeszcze nie zgasła w świątyni PANA, gdzie była arka Boga, i Samuel też się położył;
Nthawiyi nʼkuti nyale ya Mulungu isanazimitsidwe. Samueli anali gone mu Nyumba ya Yehova, kumene kunali Bokosi la Chipangano cha Mulungu.
4 PAN zawołał Samuela, a on odpowiedział: Oto jestem.
Yehova anayitana Samueli. Iye anayankha kuti, “Wawa.”
5 I przybiegł do Heliego, i powiedział: Oto jestem, gdyż mnie wołałeś. A on odparł: Nie wołałem, wróć i połóż się. Poszedł więc i położył się.
Ndipo iyeyo anathamangira kwa Eli ndipo anati, “Ndabwera ndamva kuyitana.” Koma Eli anati, “Ine sindinakuyitane, bwerera kagone.” Ndipo iye anapita kukagona.
6 PAN ponownie zawołał Samuela. I Samuel wstał, poszedł do Heliego i powiedział: Oto jestem, gdyż mnie wołałeś. On [mu] odpowiedział: Nie wołałem, mój synu; wróć i połóż się.
Yehova anayitananso, “Samueli!” Ndipo Samueli anadzuka ndi kupita kwa Eli nati, “Ndabwera popeza ndamva mukundiyitana.” Eli nati, “Mwana wanga, ine sindinakuyitane, bwerera kagone.”
7 A Samuel jeszcze nie znał PANA i słowo PANA nie zostało mu jeszcze objawione.
Nthawiyi nʼkuti Samueli asanadziwe Yehova ndipo Mawu a Yehova nʼkuti asanawululidwe kwa iye.
8 I PAN zawołał Samuela po raz trzeci. Wstał więc, poszedł do Heliego i powiedział: Oto jestem, gdyż mnie wołałeś. Wtedy Heli zrozumiał, że PAN wołał chłopca.
Yehova anayitananso Samueli kachitatu ndipo Samueli anadzuka ndikupita kwa Eli ndipo anati, “Ndabwera popeza mwandiyitana ndithu.” Apo Eli anazindikira kuti Yehova ndiye ankayitana mnyamatayo.
9 I Heli powiedział do Samuela: Idź, połóż się, a jeśli cię zawoła, powiedz: Mów, PANIE, bo twój sługa słucha. Samuel poszedł więc i położył się na swoim miejscu.
Tsono Eli anamuwuza Samueli kuti, “Pita ukagone ndipo akakuyitananso ukanene kuti, ‘Yankhulani Yehova, pakuti mtumiki wanu ndikumvetsera.’” Choncho Samueli anapita ndi kukagona pamalo pake.
10 Potem PAN przyszedł, stanął i zawołał tak jak poprzednio: Samuelu, Samuelu! I Samuel odpowiedział: Mów, bo twój sługa słucha.
Yehova anabwera ndi kuyima pomwepo, ndi kuyitana monga nthawi zina zija, “Samueli! Samueli!” Ndipo Samueli anayankha, “Yankhulani, pakuti mtumiki wanu akumvetsera.”
11 Wtedy PAN powiedział do Samuela: Oto uczynię [taką] rzecz w Izraelu, że każdemu, kto o niej usłyszy, zadzwoni w obu uszach.
Ndipo Yehova anati kwa Samueli, “Taona, patsala pangʼono kuti ndichite chinthu china mu Israeli chimene chidzadabwitsa aliyense amene adzamve.
12 W tym dniu dokonam na Helim wszystkiego, co mówiłem przeciwko jego domowi, od początku do końca.
Tsiku limenelo ndidzachitadi zonse zimene ndinayankhula zokhudza banja la Eli kuyambira poyamba mpaka pomaliza.
13 I dałem mu poznać, że osądzę jego dom na wieki za nieprawość, o której wiedział. Jego synowie bowiem postępowali nikczemnie, a on ich nie poskromił.
Pakuti ndinamudziwitsa kuti Ine ndikhoza kulanga banja lake kwamuyaya chifukwa cha zoyipa zimene ana ake ankadziyipitsa nazo. Iye ankadziwa zimenezi koma osawaletsa.
14 Dlatego przysiągłem domowi Heliego, że nieprawość domu Heliego nigdy nie będzie oczyszczona [żadną] ofiarą [krwawą] ani ofiarą pokarmową.
Nʼchifukwa chake ndinalumbira kuti, ‘Zoyipa zimene banja la Eli linandichita sizidzafafanizidwa mpaka muyaya ngakhale adzapereke nsembe kapena zopereka zina.’”
15 I Samuel do rana leżał, po czym otworzył drzwi domu PANA. Samuel jednak bał się oznajmić Heliemu o widzeniu.
Samueli anagona mpaka mmawa. Atadzuka anatsekula zitseko za Nyumba ya Yehova. Iye anachita mantha kumuwuza Eli za masomphenya ake.
16 Wtedy Heli zawołał Samuela: Samuelu, synu mój. Ten odpowiedział: Oto jestem.
Koma Eli anamuyitana nati, “Samueli mwana wanga.” Samueli anayankha kuti, “Wawa.”
17 I zapytał: Cóż to za słowa, które [PAN] ci powiedział? Nie ukrywaj tego, proszę, przede mną. Niech Bóg tak ci uczyni i tamto dorzuci, jeśli ukryjesz przede mną cokolwiek z tego, co ci powiedział.
Tsono Eli anafunsa kuti, “Yehova wakuwuza chiyani? Usandibisire. Mulungu akulange ndithu ngati undibisira chilichonse cha zimene wakuwuza.”
18 Samuel opowiedział mu więc wszystko i nie ukrył [nic] przed nim. A [on] odparł: To PAN. Niech czyni to, co dobre w jego oczach.
Choncho Samueli anamuwuza zonse, sanamubisire kalikonse. Ndipo Eli anati, “Iye ndi Yehova, mulekeni achite chimene chamukomera.”
19 I Samuel rósł, a PAN był z nim i nie pozwolił upaść na ziemię [żadnemu] z jego słów.
Yehova anali ndi Samueli pamene amakula, ndipo zonse zimene ankayankhula zinkachitikadi.
20 A cały Izrael od Dan aż do Beer-Szeby poznał, że Samuel stał się wiernym prorokiem PANA.
Ndipo Aisraeli onse kuyambira ku dera la Dani mpaka ku Beeriseba anazindikira kuti Yehova analozadi chala pa Samueli kuti akhale mneneri wake.
21 PAN zaś ukazywał się znowu w Szilo. PAN bowiem objawił się Samuelowi w Szilo przez słowo PANA.
Yehova anapitiriza kuoneka ku Silo, ndipo kumeneko anadziwulula yekha kwa Samueli mwa mawu ake.

< I Samuela 3 >