< I Królewska 5 >
1 Hiram, król Tyru, wysłał swoje sługi do Salomona, bo usłyszał, że namaszczono go na króla w miejsce jego ojca. Hiram bowiem kochał Dawida przez wszystkie dni.
Hiramu mfumu ya ku Turo atamva kuti Solomoni wadzozedwa kukhala mfumu mʼmalo mwa abambo ake Davide, anatumiza akazembe ake kwa Solomoni, chifukwa mfumu Hiramu inali pa ubale wabwino ndi Davide nthawi zonse.
2 Salomon [też] posłał do Hirama taką wiadomość:
Solomoni anabweza mawu awa kwa Hiramu:
3 Ty wiesz, że mój ojciec Dawid nie mógł budować domu dla imienia PANA, swego Boga, z powodu wojen, które go otaczały, dopóki PAN nie poddał jego [wrogów] pod stopy jego nóg.
“Inu mukudziwa kuti chifukwa cha nkhondo zimene zinkachokera ku mbali zonse kulimbana ndi abambo anga, iwo sanathe kumangira Nyumba Yehova Mulungu wawo, mpaka Yehova atawayika adani awo pansi pa ulamuliro wawo.
4 Lecz teraz PAN, mój Bóg, dał mi zewsząd odpoczynek, nie ma żadnego przeciwnika ani złego wydarzenia.
Koma tsopano Yehova Mulungu wanga wandipatsa mtendere mbali zonse za dziko ndipo ndilibe mdani kapena chovuta chilichonse.
5 Oto postanowiłem zbudować dom dla imienia PANA, swego Boga, zgodnie z tym, co PAN powiedział memu ojcu Dawidowi: Twój syn, którego posadzę po tobie na twoim tronie, on zbuduje dom dla mojego imienia.
Choncho ine ndikufuna kumangira nyumba Yehova Mulungu wanga, monga momwe Iye anawuzira abambo anga Davide kuti, ‘Mwana wako amene ndidzamukhazike pa mpando waufumu mʼmalo mwako ndiye adzandimangire Nyumba.’
6 Teraz więc rozkaż, aby ścięto dla mnie cedry z Libanu, a moi słudzy będą z twoimi sługami. Dam ci zapłatę dla twoich sług, jaką wyznaczysz. Ty wiesz bowiem, że wśród nas nie ma nikogo, kto by umiał rąbać drzewo [tak] jak Sydończycy.
“Choncho lamulani kuti andidulire mikungudza ya ku Lebanoni. Anthu anga adzagwira ntchito imeneyo pamodzi ndi anthu anuwo, ndipo ine ndidzalipira anthu anuwo malipiro amene inu mungakhazikitse. Inu mukudziwa kuti ife tilibe anthu aluso locheka matabwa monga Asidoni.”
7 Gdy Hiram usłyszał słowa Salomona, bardzo się ucieszył i powiedział: Błogosławiony [niech będzie] dzisiaj PAN, który dał Dawidowi mądrego syna, [aby był] nad tym wielkim ludem.
Hiramu anakondwa kwambiri atamva uthenga wa Solomoni ndipo anati, “Lero Yehova atamandike chifukwa wapatsa Davide mwana wanzeru kuti alamulire mtundu waukuluwu.”
8 Wtedy Hiram posłał do Salomona wiadomość: Wysłuchałem tego, co mi przesłałeś. Uczynię wszystko zgodnie z twoim życzeniem co do drewna cedrowego i drewna cyprysowego.
Tsono Hiramu anabweza mawu awa kwa Solomoni: “Ndalandira uthenga umene mwanditumizira ndipo ine ndidzachita zonse zimene mukufuna pokupatsani mitengo ya mkungudza ndi payini.
9 Moi słudzy sprowadzą [je] z Libanu nad morze, a ja każę je złożyć na tratwy [i przeprawić] przez morze aż do miejsca, które mi wskażesz. Tam je rozładują, a ty je zabierzesz. Ty też spełnisz moje życzenie i dostarczysz żywność dla mojego dworu.
Anthu anga adzatsika nayo kuchokera ku Lebanoni mpaka ku nyanja, ndipo adzayiyandamitsa pa nyanja mpaka ku malo amene munene. Kumeneko ndidzayimasula ndipo mudzayitenga. Ndipo inu mudzakwaniritsa chokhumba changa pondipatsa chakudya cha banja langa laufumu.”
10 Hiram dostarczał więc Salomonowi drewno cedrowe i drewno cyprysowe, tyle ile [Salomon] chciał.
Motero Hiramu anapereka kwa Solomoni mitengo yonse ya mkungudza ndi payini imene ankayifuna,
11 Salomon z kolei dostarczał Hiramowi dwadzieścia tysięcy kor pszenicy na żywność dla jego dworu i dwadzieścia kor czystej oliwy. Tyle Salomon dostarczał Hiramowi każdego roku.
ndipo Solomoni anamupatsa Hiramu mitanga ya tirigu 20,000 ngati chakudya cha pa nyumba yake, kuwonjezera pa migolo ya mafuta a olivi yokwana 20,000. Solomoni anapitiriza kupereka zimenezi chaka ndi chaka.
12 A PAN dał Salomonowi mądrość, tak jak mu obiecał. I panował pokój między Hiramem a Salomonem, zawarli też ze sobą przymierze.
Yehova anamupatsa Solomoni nzeru monga momwe analonjezera. Panali ubale wa mtendere pakati pa Solomoni ndi Hiramu, ndipo awiriwa anachita pangano.
13 Potem król Salomon kazał wybrać robotników z całego Izraela, a było tych robotników trzydzieści tysięcy mężczyzn.
Mfumu Solomoni inasonkhanitsa anthu ogwira ntchito ya thangata mʼdziko lonse la Israeli ndipo anthu athangatawo analipo 30,000.
14 Co miesiąc wysyłał ich do Libanu po dziesięć tysięcy na zmianę: miesiąc przebywali w Libanie, a dwa miesiące w domu. Przełożonym tych robotników był Adoniram.
Iye ankatumiza anthu 10,000 ku Lebanoni pa mwezi mosinthanasinthana, kotero kuti ankakhala ku Lebanoniko mwezi umodzi ndipo kwawo ankakhalako miyezi iwiri. Adoniramu ndiye ankayangʼanira ogwira ntchito yathangatayo.
15 Salomon miał też siedemdziesiąt tysięcy ludzi do dźwigania ciężarów oraz osiemdziesiąt tysięcy robotników w kamieniołomach w górach;
Solomoni anali ndi anthu amtengatenga 70,000, anthu 80,000 osema miyala ku mapiri,
16 Oprócz naczelnych urzędników Salomona, którzy nadzorowali pracę, [miał też] trzy tysiące trzystu przełożonych nad ludźmi wykonującymi pracę.
ndi akapitawo 33,000 amene ankayangʼanira ntchitoyi ndiponso anthu ogwira ntchito zina.
17 Król rozkazał również, aby przywieziono kamienie wielkie, kamienie drogie i kamienie ciosane na założenie fundamentów domu.
Molamulidwa ndi mfumu, anakumba ndi kusema miyala ikuluikulu kwambiri yoti akamangire maziko a Nyumba ya Mulungu.
18 Ciosali [je] więc budowniczowie Salomona i Hirama oraz Gibilici. I tak przygotowali drewno i kamienie na budowę domu.
Amisiri a Solomoni ndi a Hiramu ndiponso anthu a ku Gebala anasema miyala ndi kukonza matabwa ndi miyala yomangira Nyumba ya Mulungu.