< I Królewska 15 >

1 W osiemnastym roku króla Jeroboama, syna Nebata, Abijam [zaczął] królować nad Judą.
Mʼchaka cha 18 cha ulamuliro wa Yeroboamu mwana wa Nebati, Abiya anakhala mfumu ya Yuda,
2 Trzy lata królował w Jerozolimie, a jego matka miała na imię Maaka [i była] córką Abiszaloma.
ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka zitatu. Amayi ake anali Maaka, mwana wa Abisalomu.
3 Szedł on śladem wszystkich grzechów swego ojca, które popełnił przed nim. Jego serce nie było doskonałe wobec PANA, swego Boga, jak serce Dawida, jego ojca.
Abiya anachita zoyipa zonse zimene abambo ake anazichita. Sanali wangwiro pamaso pa Yehova Mulungu wake, monga linachitira kholo lake Davide.
4 Jednak ze względu na Dawida PAN, jego Bóg, dał mu pochodnię w Jerozolimie, wzbudzając po nim jego syna i umacniając Jerozolimę;
Komabe chifukwa cha Davide, Yehova Mulungu wake anamupatsa nyale mu Yerusalemu pomupatsa mwana wolowa mʼmalo mwake ndi kumukhazikitsa kukhala wamphamvu mu Yerusalemu;
5 Ponieważ Dawid czynił to, co było prawe w oczach PANA, i nie odstąpił od niczego, co mu rozkazał, przez wszystkie dni swego życia, z wyjątkiem sprawy Uriasza Chetyty.
pakuti Davide anachita zolungama pamaso pa Yehova ndipo sanalephere kusunga chilichonse chimene Yehova anamulamula masiku onse a moyo wake kupatula nkhani ija ya Uriya Mhiti.
6 I trwała wojna między Roboamem a Jeroboamem przez wszystkie dni jego życia.
Panali nkhondo pakati pa Rehobowamu ndi Yeroboamu masiku onse a moyo wa Abiya.
7 A pozostałe dzieje Abijama i wszystko, co czynił, czyż nie są zapisane w kronikach o królach Judy. I trwała wojna między Abijamem a Jeroboamem.
Tsono ntchito zina za Abiya, ndi zina zonse anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda? Panali nkhondo pakati pa Abiya ndi Yeroboamu.
8 Potem Abijam zasnął ze swoimi ojcami i pogrzebano go w mieście Dawida. I jego syn Asa królował w jego miejsce.
Ndipo Abiya anamwalira nayikidwa mʼmanda momwe anayikidwa makolo ake mu Mzinda wa Davide. Ndipo Asa, mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
9 W dwudziestym roku Jeroboama, króla Izraela, Asa królował nad Judą.
Mʼchaka cha makumi awiri cha Yeroboamu mfumu ya Israeli, Asa anakhala mfumu ya Yuda,
10 I królował czterdzieści jeden lat w Jerozolimie. Jego matka miała na imię Maacha [i była] córką Abiszaloma.
ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 41. Agogo ake akazi anali Maaka mwana wa Abisalomu.
11 Asa czynił to, co było prawe w oczach PANA, jak Dawid, jego ojciec.
Asa anachita zolungama pamaso pa Yehova monga anachitira Davide kholo lake.
12 Usunął z ziemi sodomitów i wszystkie bożki, które wykonali jego ojcowie.
Iye anachotsa mʼdzikomo amuna onse ochita zadama pochita chipembedzo chawo ndiponso anachotsa mafano onse amene makolo ake anawapanga.
13 Również Maachę, swoją matkę, odsunął od panowania za to, że sporządziła bożka w gaju. Asa zniszczył więc jej bożka i spalił [go] przy potoku Cedron.
Iye anachotsanso gogo wake Maaka pa udindo wake wa amayi a mfumu, chifukwa choti anapanga fano lonyansa la Asera. Asa anagwetsa fanolo nakalitentha ku Chigwa cha Kidroni.
14 I chociaż wyżyny nie zostały zniszczone, jednak serce Asy było doskonałe wobec PANA przez wszystkie jego dni.
Ngakhale sanachotse malo opembedzerapo mafano, mtima wa Asa unali wodzipereka kwathunthu kwa Yehova masiku onse a moyo wake.
15 I wniósł do domu PANA rzeczy poświęcone przez swego ojca i rzeczy, które sam poświęcił: srebro, złoto i naczynia.
Asa anabweretsa ku Nyumba ya Yehova zinthu zimene abambo ake anazipereka, ndiponso zinthu zimene iye mwini anazipereka: zagolide, siliva ndi ziwiya zotengera.
16 I między Asą a Baszą, królem Izraela, trwała wojna przez wszystkie ich dni.
Panali nkhondo pakati pa Asa ndi Baasa mfumu ya Israeli nthawi yonse ya ulamuliro wawo.
17 Basza, król Izraela, nadciągnął przeciwko Judzie i rozbudował Rama, aby [nikomu] nie pozwolić wychodzić od Asy, króla Judy, i przychodzić do niego.
Baasa mfumu ya Israeli anapita kukathira nkhondo dziko la Yuda, ndipo anamangira linga mzinda wa Rama kuletsa kuti wina aliyense asatuluke kapena kulowa mʼdziko la Asa, mfumu ya Yuda.
18 Asa wziął więc całe srebro i złoto, które pozostało w skarbcach domu PANA i w skarbcach domu królewskiego, i dał je w ręce swoich sług. Następnie król Asa posłał ich do Ben-Hadada, syna Tabrimona, syna Chezjona, króla Syrii, który mieszkał w Damaszku, mówiąc:
Tsono Asa anatenga siliva yense pamodzi ndi golide zimene zinatsala ku malo osungira chuma cha ku Nyumba ya Yehova ndiponso ku nyumba yake yaufumu. Anazipereka kwa atumiki ake, nawatuma kupita nazo kwa Beni-Hadadi mwana wa Tabirimoni, mwana wa Heziyoni, mfumu ya Aramu, amene ankakhala ku Damasiko ndipo anakamuwuza kuti,
19 Jest przymierze między mną a tobą, między moim ojcem a twoim ojcem. Oto posyłam ci dar: srebro i złoto. Idź, zerwij swoje przymierze z Baszą, królem Izraela, aby odstąpił ode mnie.
“Tiyeni tigwirizane inu ndi ine, monga panali mgwirizano pakati pa abambo anu ndi abambo anga. Onani, ndikukutumizirani mphatso za siliva ndi golide. Tsopano kathetseni mgwirizano wanu ndi Baasa mfumu ya Israeli kuti andisiye.”
20 I Ben-Hadad posłuchał króla Asy, i posłał dowódców swoich wojsk przeciwko miastom Izraela, napadł na Ijon, Dan i Abel-Bet-Maaka oraz całe Kinerot wraz z całą ziemią Neftalego.
Choncho Beni-Hadadi anamvera zimene ananena mfumu Asa ndipo anatumiza olamulira magulu ake ankhondo ku mizinda ya Israeli. Ndipo iye anagonjetsa Iyoni, Dani, Abeli-Beti-Maaka ndi dera lonse la Kinereti kuphatikiza dziko lonse la Nafutali.
21 Gdy Basza [o tym] usłyszał, przestał rozbudowywać Rama i mieszkał w Tirsie.
Baasa atamva zimenezi, anasiya kumangira linga Rama ndipo anakakhala ku Tiriza.
22 Wtedy król Asa zwołał cały lud Judy, bez wyjątku, a lud zabrał z Rama kamienie i drewno, z których Basza budował. I król Asa rozbudował nimi Gibea Beniamina oraz Mispę.
Pamenepo Mfumu Asa analamula anthu onse a ku Yuda osasiya ndi mmodzi yemwe, ndipo anachotsa ku Rama miyala ndi matabwa amene Baasa ankamangira kumeneko. Zipangizo zimenezi Mfumu Asa inamangira linga la Geba ku Benjamini ndi la ku Mizipa.
23 A pozostałe dzieje Asy, cała jego potęga i wszystko, co czynił, oraz miasta, które zbudował, czyż nie są zapisane w kronikach królów Judy? Jednak w okresie swojej starości zachorował na nogi.
Tsono ntchito zina za Asa, za mphamvu zake ndi mizinda imene anayimanga ndi zina zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda? Koma pa nthawi ya ukalamba wake anadwala nthenda ya mapazi.
24 I Asa zasnął ze swoimi ojcami, i został pogrzebany z nimi w mieście Dawida, swego ojca. A jego syn Jehoszafat królował w jego miejsce.
Ndipo Asa anamwalira nayikidwa mʼmanda momwe anayikidwa makolo ake mu mzinda wa Davide kholo lake. Ndipo Yehosafati mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
25 W drugim roku Asy, króla Judy, nad Izraelem zaczął królować Nadab, syn Jeroboama i królował nad Izraelem dwa lata.
Nadabu, mwana wa Yeroboamu anakhala mfumu ya Israeli mʼchaka chachiwiri cha Asa mfumu ya Yuda, ndipo analamulira Israeli zaka ziwiri.
26 I czynił to, co złe w oczach PANA, idąc drogami swego ojca i w jego grzechu, którym doprowadził Izraela do grzechu.
Nadabu anachita zoyipa pamaso pa Yehova, anayenda mʼnjira za abambo ake ndi mu uchimo womwe anachimwitsa nawo Israeli.
27 I Basza, syn Achiasza, z domu Issachara, uknuł spisek przeciw niemu. Basza zabił go w Gibbeton, który należał do Filistynów. Nadab bowiem i cały Izrael oblegali Gibbeton.
Baasa mwana wa Ahiya, wa banja la Isakara anakonzera Nadabuyo chiwembu, ndipo anamukantha ku Gibetoni, mzinda wa Afilisti, pamene Nadabu ndi anthu onse a ku Israeli anali atawuzungulira.
28 Basza zabił go w trzecim roku Asy, króla Judy, i [sam] królował w jego miejsce.
Baasa anapha Nadabu mʼchaka chachitatu cha Asa, mfumu ya ku Yuda ndipo analowa ufumu mʼmalo mwake.
29 Kiedy zaczął królować, wymordował cały dom Jeroboama i nie pozostawił żywej duszy [z rodu] Jeroboama, dopóki nie wytracił go zgodnie ze słowem PANA, które wypowiedział przez swego sługę Achiasza Szilonitę;
Iye atangoyamba kulamulira, anapha anthu onse a banja la Yeroboamu. Sanasiye ndi mmodzi yemwe wamoyo pa banjapo, koma anawononga anthu onse, molingana ndi mawu a Yehova amene anayankhula mwa mtumiki wake Ahiya wa ku Silo
30 Z powodu grzechów Jeroboama, które popełnił i do których skłonił Izraela; z powodu rozdrażnienia, którym pobudził do gniewu PANA, Boga Izraela.
chifukwa cha machimo amene Yeroboamu anachita, ndiponso kuchimwitsa anthu a ku Israeli, naputa mkwiyo wa Yehova Mulungu wa Israeli.
31 A pozostałe dzieje Nadaba i wszystko, co czynił, czyż nie są zapisane w kronikach królów Izraela?
Tsono ntchito za Nadabu ndi zina zonse zimene anazichita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
32 I między Asą a Baszą, królem Izraela, trwała wojna po wszystkie ich dni.
Panali nkhondo pakati pa Asa ndi Baasa mfumu ya Israeli pa nthawi yonse ya ulamuliro wawo.
33 W trzecim roku Asy, króla Judy, nad całym Izraelem zaczął królować w Tirsie Basza, syn Achiasza. [I królował] przez dwadzieścia cztery lata.
Chaka chachitatu cha Asa mfumu ya Yuda, Baasa mwana wa Ahiya anakhala mfumu ya Aisraeli onse ku Tiriza, ndipo analamulira zaka 24.
34 I czynił to, co złe w oczach PANA, idąc drogami Jeroboama i w jego grzechu, do którego skłonił Izraela.
Anachita zoyipa pamaso pa Yehova, nayenda mʼnjira za Yeroboamu ndi kuchita tchimo lake limene linachimwitsa anthu a ku Israeli.

< I Królewska 15 >