< I Kronik 13 >
1 A Dawid odbył naradę z tysiącznikami i setnikami oraz ze wszystkimi dowódcami.
Davide anakambirana ndi akuluakulu ake, atsogoleri a anthu 1,000 ndi atsogoleri a anthu 100.
2 Potem Dawid powiedział do całego zgromadzenia Izraela: [Jeśli] wam się to podoba i jeśli jest to od PANA, naszego Boga, roześlijmy wiadomość wszędzie do naszych braci, którzy pozostali we wszystkich krainach Izraela, a także do kapłanów i Lewitów – po miastach i ich pastwiskach – i niech się zgromadzą u nas;
Ndipo anati kwa gulu lonse la Israeli, “Ngati kukukomerani komanso ngati chili chifuniro cha Yehova Mulungu wathu, tiyeni titumize uthenga kulikonse kumene kuli abale athu ena onse ku dziko lonse la Israeli ndiponso kwa ansembe ndi Alevi amene ali nawo mʼmidzi yawo ndi madera odyetsera ziweto, kuti abwere adzakhale nafe.
3 Abyśmy sprowadzili do nas arkę naszego Boga. Nie pytaliśmy bowiem o nią za czasów Saula.
Tiyeni tibweretsenso Bokosi la Mulungu wathu kuno kwathu, pakuti nthawi ya Sauli sitinafunse za bokosili.”
4 I całe zgromadzenie powiedziało, aby tak czynić, bo ta rzecz podobała się całemu ludowi.
Gulu lonse linavomereza izi, pakuti anthu onse anaona kuti kunali kofunika kutero.
5 Dawid więc zebrał cały Izrael od egipskiego Szichoru aż do wejścia do Chamat, aby sprowadzić arkę Boga z Kiriat-Jearim.
Kotero Davide anasonkhanitsa Aisraeli onse, kuchokera ku mtsinje wa Sihori ku Igupto mpaka ku Lebo Hamati, kuti abweretse Bokosi la Mulungu kuchokera ku Kiriati-Yearimu.
6 Dawid wyruszył wraz z całym Izraelem do Baali, w Kiriat-Jearim, które [znajduje się] w Judzie, aby sprowadzić stamtąd arkę PANA Boga zasiadającego nad cherubinami, gdzie wzywane jest jego imię.
Davide pamodzi ndi Aisraeli onse anapita ku Baalahi (Kiriati-Yearimu) ku Yuda kukatenga Bokosi la Yehova Mulungu, amene amakhala pakati pa akerubi. Limeneli ndiye Bokosi la Chipangano lomwe limadziwika ndi Dzina lake.
7 I wywieźli arkę Boga na nowym wozie z domu Abinadaba, a Uzza i Achio prowadzili wóz.
Iwo anachotsa Bokosi la Mulungu ku nyumba ya Abinadabu pa ngolo yatsopano. Uza ndi Ahiyo ndiwo ankayendetsa ngoloyo.
8 Dawid zaś i cały Izrael grali przed Bogiem ze wszystkich sił, śpiewając przy dźwiękach harf, cytr, bębnów, cymbałów i trąb.
Davide pamodzi ndi Aisraeli onse ankakondwerera ndi mphamvu zawo zonse pamaso pa Mulungu, poyimba nyimbo pogwiritsa ntchito azeze, apangwe, matambolini, maseche ndi malipenga.
9 A gdy przyszli na klepisko Kidona, Uzza wyciągnął rękę, aby przytrzymać arkę, bo woły się potknęły.
Atafika pa malo opunthira tirigu ku Kidoni, Uza anatambalitsa dzanja lake kuti agwire bokosilo, chifukwa ngʼombe zinkafuna kugwa.
10 I zapłonął gniew PANA przeciwko Uzzie i [PAN] go zabił, dlatego że wyciągnął rękę do arki. I umarł tam przed Bogiem.
Yehova anapsera mtima Uza ndipo anamukantha chifukwa chogwira bokosilo. Choncho iyeyo anafera pomwepo pamaso pa Mulungu.
11 I Dawid był wielce niezadowolony, że PAN tak srogo poraził Uzzę, dlatego nazwał to miejsce Peres-Uzza i tak [jest nazywane] do dziś.
Ndipo Davide anakhumudwa chifukwa Yehova anakantha Uza ndipo mpaka lero malowo amatchedwa Perezi Uza.
12 I Dawid zląkł się Boga tego dnia, i powiedział: Jak mam wprowadzić do siebie arkę Boga?
Tsiku limenelo Davide anachita mantha ndi Mulungu ndipo anafunsa kuti, “Kodi Bokosi la Mulungu lingafike bwanji kwathu?”
13 Dlatego Dawid nie wprowadził arki do siebie, do miasta Dawida, lecz wprowadził ją do domu Obed-Edoma Gittyty.
Iye sanapitenso nalo Bokosi la Mulungu ku Mzinda wa Davide. Mʼmalo mwake anapita nalo ku nyumba ya Obedi-Edomu Mgiti.
14 I arka Boga pozostała z domownikami Obed-Edoma w jego domu przez trzy miesiące. A PAN błogosławił domowi Obed-Edoma i wszystkiemu, co miał.
Ndipo Bokosi la Mulungu linakhala mʼbanja la Obedi-Edomu mʼnyumba mwake kwa miyezi itatu ndipo Yehova anadalitsa nyumba yake ndi chilichonse chimene anali nacho.