< Sofoniasza 3 >

1 Biada temu miastu zmazanemu i splugawionemu, gwałty czyniącemu!
Tsoka kwa mzinda wa anthu opondereza, owukira ndi odetsedwa!
2 Nie słucha głosu, ani przyjmuje karności, w Panu nie ufa, do Boga swego nie przybliża się.
Sumvera aliyense, sulandira chidzudzulo. Sumadalira Yehova, suyandikira pafupi ndi Mulungu wake.
3 Książęta jego w pośrodku jego są lwy ryczące, sędziowie jego są wilki wieczorne, które nie gryzą kości aż do poranku.
Akuluakulu ake ali ngati mikango yobuma, olamulira ake ndi olusa ngati mimbulu ya nthawi ya madzulo, zimene pofika mmawa sizisiya chilichonse.
4 Prorocy jego skwapliwi, mężowie przewrotni; kapłani jego splugawili rzeczy święte, zakon gwałcą.
Aneneri ake ndi odzikuza; anthu achinyengo. Ansembe ake amadetsa malo opatulika ndipo amaphwanya lamulo.
5 Pan sprawiedliwy jest w pośród niego, nie czyni nieprawości, każdego dnia sąd swój wydaje na światłość bez przestania; wszakże złośnik wstydzić się nie umie.
Yehova amene ali pakati pawo ndi wolungama; Iye salakwa. Tsiku ndi tsiku amaweruza molungama, ndipo tsiku lililonse salephera, komabe ochita zoyipa sachita manyazi nʼkomwe.
6 Wykorzeniłem narody, spustoszone są zamki ich, obróciłem w pustynię ulice ich, tak, że niemasz, ktoby przez nie chodził; spustoszone są miasta ich, tak, że niemasz ani człowieka ani obywatela.
“Ndachotseratu mitundu ya anthu; ndagwetsa malinga awo. Ndipo sindinasiye ndi mmodzi yemwe mʼmisewu mwawo, popanda aliyense wodutsa. Mizinda yawo yawonongedwa; palibe aliyense adzatsalemo.
7 Rzekłem: Wżdyć się mnie bać będziesz, przyjmiesz karność, aby nie był wytracony przybytek twój, przez to, czemem cię nawiedzić chciał; ale rano wstawszy psują wszystkie przedsięwzięcia swoje.
Ndinati, ‘Ndithudi, anthu a mu mzindawu adzandiopa ndi kumvera kudzudzula kwanga!’ Ndipo sindidzawononga nyumba zawo, kapena kuwalanganso. Koma iwo anali okonzeka kuchita mwachinyengo zinthu zonse zimene amachita.
8 Przetoż oczekiwajcie na mię, mówi Pan, do dnia, którego powstanę do łupu; bo sąd mój jest, abym zebrał narody, i zgromadził królestwa, abym na nie wylał rozgniewanie moje i wszystkę popędliwość gniewu mego; ogniem zaiste gorliwości mojej będzie po żarta ta wszystka ziemia.
Choncho mundidikire,” akutero Yehova, “chifukwa cha tsiku limene ndidzaperekera umboni. Ndatsimikiza kusonkhanitsa pamodzi mitundu ya anthu, kusonkhanitsa maufumu ndi kutsanulira ukali wanga pa iwo; mkwiyo wanga wonse woopsa. Dziko lonse lidzatenthedwa ndi moto wa mkwiyo wa nsanje yanga.
9 Bo na ten czas przywrócę narodom wargi czyste, któremiby wzywali wszyscy imienia Pańskiego, a służyli mu jednomyślnie.
“Pamenepo ndidzayeretsa milomo ya anthu a mitundu yonse kuti anthu onsewo ayitane dzina la Yehova ndi kumutumikira Iye pamodzi.
10 Ci, którzy są za rzekami ziemi Murzyńskiej, pokłon mi oddają z córką rozproszonych moich, przyniosą mi dary.
Kuchokera kutsidya kwa mitsinje ya ku Kusi anthu anga ondipembedza, omwazikana, adzandibweretsera zopereka.
11 Dnia onego nie zawstydzisz się za żadne uczynki twoje, któremiś wystąpiło przeciwko mnie; bo na ten czas odejmę z pośrodku ciebie tych, którzy się weselą z sławy twojej, a nie będziesz się więcej wywyższało na górze świętobliwości mojej.
Tsiku limenelo simudzachita manyazi chifukwa cha zoyipa zonse munandichitira, popeza ndidzachotsa onse mu mzinda uwu amene amakondwera chifukwa cha kunyada kwawo. Simudzakhalanso odzikuza mʼphiri langa lopatulika.
12 I zostawię w pośrodku ciebie lud ubogi a nędzny, i ufać będą w imieniu Pańskiem.
Koma ndidzasiya pakati panu anthu ofatsa ndi odzichepetsa, amene amadalira dzina la Yehova.
13 Ostatki Izraela nie będą czyniły nieprawości, ani będą mówiły kłamstwa, ani się znajdzie w ustach ich język zdradliwy; ale się paść będą i odpoczywać, a nie będzie, ktoby je przestraszył.
Aisraeli otsala sadzachitanso zolakwika; sadzayankhulanso zonama, ngakhale chinyengo sichidzatuluka mʼkamwa mwawo. Adzadya ndi kugona ndipo palibe amene adzawachititse mantha.”
14 Zaśpiewaj, córko Syońska! wykrzykajcie, Izraelczycy! wesel się a raduj się ze wszystkiego serca, córko Jeruzalemska!
Imba, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni; fuwula mokweza, iwe Israeli! Sangalala ndi kukondwera ndi mtima wako wonse, iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu!
15 Że odjął Pan sądy twoje, uprzątnął nieprzyjaciela twego; król Izraelski jest Panem w pośrodku ciebie, nie oglądasz więcej złego.
Yehova wachotsa chilango chako, wabweza mdani wako. Yehova, Mfumu ya Israeli, ali pakati pako; sudzaopanso chilichonse.
16 Dnia onego rzeką do Jeruzalemu: Nie bój się! a do Syonu: Niech nie mdleją ręce twoje!
Pa tsiku limenelo adzanena kwa Yerusalemu kuti, “Usaope, iwe Ziyoni; usafowoke.
17 Pan, Bóg twój, w pośrodku ciebie mocny zachowa cię, rozweseli się wielce nad tobą, przestanie na miłości swej przeciwko tobie, i rozweseli się nad tobą z śpiewaniem, mówiąc:
Yehova Mulungu wako ali pakati pako, ali ndi mphamvu yopulumutsa. Adzakondwera kwambiri mwa iwe, adzakukhalitsa chete ndi chikondi chake, adzayimba mokondwera chifukwa cha iwe.”
18 Tęskniących po Jeruzalemie zasię zgromadzę, bo z ciebie są i smutni dla brzemienia zelżywości włożonej na cię.
“Ndidzakuchotserani zowawa za pa zikondwerero zoyikika; nʼzolemetsa ndi zochititsa manyazi.
19 Oto Ja koniec uczynię wszystkim, którzy cię trapić będą na on czas, a zachowam chromą, i wygnaną zgromadzę; owszem sposobię im chwałę i imię po wszystkiej ziemi, w której zelżywość ponosili.
Taonani, nthawi imeneyo ndidzathana ndi onse amene anakuponderezani; ndidzapulumutsa olumala ndi kusonkhanitsa amene anamwazika. Ndidzawayamikira ndi kuwachitira ulemu mʼdziko lililonse mmene anachititsidwa manyazi.
20 Wtenczas przywiodę was, wtenczas, mówię, zgromadzę was; albowiem dam wam imię i chwałę między wszystkimi narodami ziemi, gdy zaś przywiodę więźnie wasze przed oczyma waszemi, mówi Pan.
Pa nthawi imeneyo ndidzakusonkhanitsani; pa nthawi imeneyo ndidzakubweretsani ku mudzi kwanu. Ndidzakuyamikirani ndi kukuchitirani ulemu pakati pa mitundu ya anthu a dziko lapansi pamene ndidzabwezeretsa mtendere wanu inu mukuona,” akutero Yehova.

< Sofoniasza 3 >