< Zachariasza 14 >

1 Oto przychodzi dzień Pański, a rozdzielone będą korzyści twoje w pośrodku ciebie.
Taonani tsiku la Yehova likubwera pamene zinthu zimene adani ako anakulanda azidzagawana iwe ukuona.
2 Bo zgromadzę wszystkie narody przeciwko Jeruzalemowi na wojnę, a miasto wzięte będzie, i domy rozchwycone będą, i niewiasty pogwałcone będą; a gdy pójdzie część miasta w pojmanie, ostatek ludu nie będzie wygładzony z miasta.
Ndidzasonkhanitsa anthu a mitundu yonse kuti adzathire nkhondo Yerusalemu; mzindawu udzalandidwa, nyumba zidzaphwasulidwa, ndipo akazi adzagwiriridwa. Theka la anthu a mu mzindamu lidzapita ku ukapolo, koma ena onse otsala mu mzindamu sadzachotsedwa.
3 Bo wyjdzie Pan, i będzie walczył przeciwko onym narodom, jako zwykł wojować w dzień potykania.
Pamenepo Yehova adzabwera kudzamenyana ndi mitundu ya anthu imeneyi, ngati mmene amachitira pa nthawi ya nkhondo.
4 I staną nogi jego w on dzień na górze Oliwnej, która jest przeciwko Jeruzalemowi na wschód słońca, a góra Oliwna się na poły rozszczepi, na wschód i na zachód słońca rozpadliną bardzo wielką, i odwali się połowa onej góry na północ, a połowa jej na południe.
Tsiku limenelo adzayimirira pa Phiri la Olivi, kummawa kwa Yerusalemu, ndipo Phiri la Olivilo lidzagawikana pawiri kuyambira kummawa mpaka kumadzulo, kupanga chigwa chachikulu, kuchititsa kuti theka la phiri lisunthire kumpoto ndi linalo kummwera.
5 Tedy ucieczecie przed doliną gór; (bo dolina tych gór dosięże aż do Azal) będziecie, mówię, uciekać, jakoście uciekali przed trzęsieniem ziemi za dni Ozyjasza, króla Judzkiego, gdy przyjdzie Pan, Bóg mój, i wszyscy święci z nim.
Inu mudzathawa podzera mʼchigwa chapakati pa phirilo, pakuti chidzafika mpaka ku Azeli. Mudzathawa monga munachitira pa tsiku la chivomerezi nthawi ya Uziya mfumu ya Yuda. Kenaka Yehova Mulungu wanga adzabwera, pamodzi ndi oyera ake onse.
6 I stanie się dnia onego, że nie będzie światłości drogiej, ani ciemności gęstej;
Tsiku limenelo sipadzakhala kuwala, kuzizira kapena chisanu.
7 Lecz będzie dzień jeden, który jest wiadomy Panu, a nie będzie dnia ani nocy; wszakże czasu wieczornego będzie światło.
Lidzakhala tsiku lapaderadera, silidzakhala usana kapena usiku; tsiku limeneli akulidziwa ndi Yehova yekha. Ikadzafika nthawi ya madzulo, kudzakhala kukuwalabe.
8 A dnia onego wyjdą wody żywe z Jeruzalemu; połowa ich do morza na wschód słońca, a połowa ich do morza ostatniego, a to będzie w lecie i w zimie.
Tsiku limenelo madzi amoyo adzatuluka mu Yerusalemu, theka lidzapita ku nyanja ya kummawa ndipo theka lina ku nyanja ya kumadzulo, nthawi yachilimwe ndi nthawi yozizira yomwe.
9 A Pan będzie królem nad wszystką ziemią; w on dzień będzie Pan jeden, i imię jego jedno.
Ndipo Yehova adzakhala mfumu pa dziko lonse lapansi. Tsiku limenelo padzakhala Ambuye mmodzi yekha, ndipo dzina lidzakhala limodzi lomwelo.
10 I uczyniona będzie ta wszystka ziemia, jako równina od Gabaa aż do Remmon na południe ku Jeruzalemowi, który wywyższony będąc, stać będzie na miejscu swojem od bramy Benjaminowej aż do miejsca bramy pierwszej i aż do bramy węgielnej, a od wieży Chananeel aż do pras królewskich.
Dziko lonse, kuyambira ku Geba mpaka ku Rimoni, kummwera kwa Yerusalemu, lidzakhala ngati Araba. Koma Yerusalemu adzakwezedwa ndipo adzakhala pamalo pakepo, kuyambira ku Chipata cha Benjamini mpaka ku malo amene ali ku Chipata Choyamba, ku Chipata Chapangodya, ndipo kuyambira ku Nsanja ya Hananeli mpaka ku malo opsinyira mphesa za mfumu.
11 I będą w nim mieszkać, a nie będzie więcej przeklęstwem, a Jeruzalem bezpiecznie mieszkać będzie.
Mʼmenemo mudzakhala anthu; sadzawonongedwanso. Yerusalemu adzakhala pa mtendere.
12 A tać będzie plaga, którą uderzy Pan wszystkie narody, któreby walczyły przeciwko Jeruzalemowi: Ciało każdego stojącego na nogach swoich schnąć będzie, a oczy ich wypłyną z dołków swoich, i język ich uschnie w ustach ich.
Mliri umene Yehova adzakanthire nawo mitundu yonse ya anthu imene inkamenyana ndi Yerusalemu ndi uwu: Matupi awo adzawola iwo eni akuyenda, maso awo adzawola ali mʼmalo mwake, ndipo malilime awo adzawola ali mʼkamwa mwawo.
13 I stanie się dnia onego wielkie uciśnienie Pańskie między nimi, tak, iż rękę jeden drugiego uchwyci, a ręka jego podniesie się na rękę bliźniego swego.
Pa tsiku limenelo Yehova adzasokoneza anthu akuluakulu. Munthu aliyense adzagwira dzanja la mnzake, ndi kuyamba kumenyana okhaokha.
14 I tyć też, Judo! walczyć będziesz w Jeruzalemie, a zgromadzone będą bogactwa wszystkich narodów okolicznych, złoto i srebro i szat obfitość wielka.
Yuda nayenso adzachita nkhondo ku Yerusalemu. Chuma chonse cha anthu a mitundu yozungulira adzachisonkhanitsa pamodzi; golide, siliva ndi zovala zochuluka kwambiri.
15 A takaż będzie plaga na konie, muły, wielbłądy, i osły, i na wszystkie bydlęta, które będą w onym obozie, jako i ta plaga.
Mliri womwewo udzapha akavalo ndi nyulu, ngamira ndi abulu, pamodzi ndi nyama zonse zokhala ku misasako.
16 A ile ich pozostanie z onych wszystkich narodów, któreby przyciągnęły przeciwko Jeruzalemowi, będą przychodzić od roku do roku, pokłon oddawać królowi, Panu zastępów, i obchodzić święto Kuczek;
Kenaka opulumuka ochokera mwa mitundu yonse ya anthu amene anathira nkhondo Yerusalemu, azidzapita chaka ndi chaka kukapembedza Mfumu Yehova Wamphamvuzonse, ndiponso kukachita Chikondwerero cha Misasa.
17 A ktoby nie szedł z pokolenia ziemi do Jeruzalemu, pokłon oddawać królowi, Panu zastępów, na tych deszcz padać nie będzie.
Ngati mitundu ina ya anthu pa dziko lapansi sidzapita ku Yerusalemu kukapembedza Mfumu Yehova Wamphamvuzonse, idzakhala wopanda mvula.
18 A jeśli pokolenie Egipskie nie wstąpi, i nie przyjdzie, choć na nich deszcz nie pada, przyjdzie jednak ta plaga, którą uderzy Pan narody, które nie przyszły, obchodzić święta Kuczek.
Ndipo ngati anthu a ku Igupto sadzapita ndi kukakhala nawo kumeneko, adzakhala wopanda mvula. Yehova adzabweretsa pa iwo mliri umene analangira mitundu ina ya anthu imene sinapite ku Chikondwerero cha Misasa.
19 A tać będzie kaźń grzechu Egipskiego, i kaźń grzechu wszystkich narodów, któreby nie przychodziły ku obchodzeniu święta Kuczek.
Chimenechi chidzakhala chilango cha Igupto ndiponso mitundu ina yonse imene sidzapita ku Chikondwerero cha Misasa.
20 Dnia onego będzie na rzędach końskich napisane: Świętobliwość Pańska; a kotłów będzie w domu Pańskim, jako miednic przed ołtarzem.
Pa tsiku limenelo pa maberu a akavalo padzalembedwa mawu oti wopatulikira Yehova, ndipo miphika ya mʼNyumba ya Yehova idzakhala yopatulika ngati mbale za ku guwa.
21 Owszem, każdy kocieł w Jeruzalemie i w Judzie poświęcony będzie Panu zastępów; a przychodząc wszyscy, którzy ofiarować mają, brać je i warzyć w nich będą, a nie będzie Chananejczyka więcej w domu Pana zastępów dnia onego.
Mʼphika uliwonse ku Yerusalemu ndi ku Yuda udzakhala wopatulikira Yehova Wamphamvuzonse, ndipo onse amene adzabwera kudzapereka nsembe adzatenga miphika ina ndi kuphikiramo. Ndipo nthawi imeneyo simudzakhalanso Akanaani mʼNyumba ya Yehova Wamphamvuzonse.

< Zachariasza 14 >