< Zachariasza 13 >

1 W on dzień będzie otworzona studnica domowi Dawidowemu i obywatelom Jeruzalemskim na omycie grzechu i nieczystości.
“Pa tsiku limenelo nyumba ya Davide adzayitsekulira kasupe wa madzi pamodzi ndi okhala mu Yerusalemu, kuti awachotsere tchimo lawo ndi chodetsa chawo.
2 I stanie się dnia onego, mówi Pan zastępów, że wykorzenię imiona bałwanów z ziemi, tak, że nie będą więcej wspominane; dotego i tych proroków i ducha nieczystego zniosę z ziemi.
“Pa tsiku limenelo, ndidzafafaniziratu mayina a mafano mʼdziko, ndipo sadzawakumbukiranso,” akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Ndidzachotsa mʼdziko aneneri pamodzi ndi mzimu wonyansa.
3 I stanie się, gdyby kto dalej prorokował, że mu rzekną ojciec jego i matka jego, którzy go spłodzili: Nie będziesz żył, przeto żeś kłamstwo mówił w imieniu Pańskiem; i przebiją go ojciec jego i matka jego, którzy go spłodzili, że prorokował.
Ndipo ngati wina aliyense adzafuna kunenera, abambo ndi amayi ake amene anamubereka, adzamuwuza kuti, ‘Uyenera kufa, chifukwa wayankhula bodza mʼdzina la Yehova.’ Pamene anenera, makolo ake omwe adzamubaya.
4 I stanie się dnia onego, że się zawstydzą oni prorocy, każdy za widzenie swoje, gdyby prorokowali, i nie obleką się w suknię kosmatą, aby kłamali;
“Pa tsiku limenelo mneneri aliyense adzachita manyazi chifukwa cha masomphenya ake. Sadzavala chovala chake chaubweya ndi cholinga chonamiza anthu.
5 Ale każdy rzecze: Nie jestem ja prorokiem, ale rolnikiem; bo mię tego nauczono od dzieciństwa mego.
Iye adzati, ‘Sindine mneneri. Ndine mlimi; ndakhala ndi kulima munda kuyambira ubwana wanga.’
6 A jeżeli mu kto rzecze: Cóż to masz za rany na rękach twoich? Tedy rzecze: Temi jestem zraniony w domu tych, którzy mię miłują.
Ngati wina adzamufunsa, ‘Zilonda zili mʼthupi lakoli ndi chiyani?’ Iye adzayankha kuti, ‘Zilondazi ndinazilandira mʼnyumba ya abwenzi anga.’
7 O mieczu! ocknij się na pasterza mego, i na męża towarzysza mego, mówi Pan zastępów; uderz pasterza, a owce rozproszone będą; ale zaś obrócę rękę moję ku maluczkim.
“Dzambatuka iwe lupanga, ukanthe mʼbusa wanga, ukanthe munthu amene ali pafupi ndi Ine!” akutero Yehova Wamphamvuzonse. Kantha mʼbusa ndipo nkhosa zidzabalalika, ndipo ndidzatambalitsa dzanja langa kuwononga zazingʼono.
8 Bo się stanie po tej wszystkiej ziemi, mówi Pan, że dwie części w niej wytracone będą i pomrą, a trzecia zostanie w niej.
Mʼdziko monse, akutero Yehova Wamphamvuzonse, “zigawo ziwiri mwa zigawo zitatu za anthu zidzakanthidwa ndi kuwonongeka; koma chigawo chimodzi chidzatsala mʼdzikomo.
9 I wwiodę i onę trzecią część do ognia, a wypławię je jako pławią srebro, a doświadczać ich będę, jako doświadczają złota; każdy będzie wzywał imienia mego, a Ja go wysłucham: rzekę: Tyś lud mój, a on rzecze: Tyś Pan Bóg mój.
Chigawo chachitatuchi ndidzachiyika pa moto; ndidzawayeretsa monga momwe amayeretsera siliva ndi kuwayesa monga momwe amayesera golide. Adzayitana pa dzina langa ndipo Ine ndidzawayankha; Ine ndidzanena kuti, ‘Awa ndi anthu anga,’ ndipo iwo adzanena kuti, ‘Yehova ndiye Mulungu wathu.’”

< Zachariasza 13 >