< Zachariasza 10 >

1 Żądajcie od Pana dżdżu czasu potrzebnego, a Pan uczyni obłoki dżdżyste, a deszcz obfity da wam i każdemu trawę na polu.
Pemphani mvula kwa Yehova pa nthawi yamphukira; ndi Yehova amene amapanga mitambo ya mvula. Iye amagwetsa mivumbi ya mvula kwa anthu, ndi kumeretsa mbewu za mʼmunda kwa aliyense.
2 Bo obrazy mówią próżność, a wieszczkowie prorokują kłamstwo i sny próżne opowiadają, daremnie cieszą; dlatego poszli w niewolę, jako trzoda, utrapieni są, że nie mieli pasterza.
Mafano amayankhula zachinyengo, owombeza mawula amaona masomphenya abodza; amafotokoza maloto onama, amapereka chitonthozo chopandapake. Choncho anthu amangoyendayenda ngati nkhosa zozunzika chifukwa chosowa mʼbusa.
3 Przeciwko takim pasterzom zapaliła się popędliwość moja, a te kozły nawiedzę; ale trzodę swoję, dom Judzki, nawiedzi Pan zastępów, i wystawi ich jako ubranego konia do boju.
“Ine ndawakwiyira kwambiri abusa, ndipo ndidzalanga atsogoleri; pakuti Yehova Wamphamvuzonse adzasamalira nkhosa zake, nyumba ya Yuda, ndi kuwasandutsa ngati akavalo aulemerero ankhondo.
4 Od niego węgiel, od niego gwóźdź, od niego łuk wojenny, od niego także wynijdzie wszelki poborca;
Mu Yuda mudzachokera mwala wapangodya, mudzachokera chikhomo cha tenti, mudzachokera uta wankhondo, mudzachokera mtsogoleri aliyense.
5 I będą jako mocarze depczący w błoto po ulicach w bitwie, i walczyć będą, bo Pan z nimi; a zawstydzą tych, którzy wsiadaja na koń.
Onse pamodzi adzakhala ngati ngwazi zankhondo zoponda mʼmatope a mʼmisewu nthawi yankhondo. Chifukwa Yehova adzakhala nawo, adzachita nkhondo ndi kugonjetsa okwera pa akavalo.
6 I umocnię dom Judowy, a dom Józefowy wybawię, i w pokoju ich osadzę, bo mam litość nad nimi; i będą, jakobym ich nie odrzucił; bom Ja jest Pan, Bóg ich, a wysłucham ich.
“Ndidzalimbitsa nyumba ya Yuda ndi kupulumutsa nyumba ya Yosefe. Ndidzawabwezeretsa chifukwa ndawamvera chisoni. Adzakhala ngati kuti sindinawakane, chifukwa ndine Yehova Mulungu wawo ndipo ndidzawayankha.
7 I będą Efraimczycy jako mocarz, a rozweseli się jako od wina serce ich; a synowie ich widząc to weselić się będą, i rozraduje się serce ich w Panu.
Aefereimu adzakhala ngati ankhondo amphamvu adzasangalala ngati anthu amene amwa vinyo. Ana awo adzaziona zimenezi ndipo adzasangalala; mʼmitima mwawo adzakondwa mwa Ambuye.
8 Zaświsnę na nich, a zgromadzę ich, bo ich odkupię; i będą rozmnożeni, jako przedtem rozmnożeni byli.
Ndidzaliza mluzu ndi kuwasonkhanitsa pamodzi. Ndithu ndawawombola; adzachulukana ngati poyamba paja.
9 I rozsieję ich między narody, aby na miejscach dalekich wspomnieli na mię, a żywi będąc z synami swoimi nawrócili się.
Ndinawamwaza pakati pa mitundu ina ya anthu, koma ku mayiko akutaliwo adzandikumbukira. Iwo pamodzi ndi ana awo adzapulumuka, ndipo adzabwerera.
10 A tak ich przywiodę z ziemi Egipskiej, i z Assyryi zgromadzę ich, a do ziemi Galaad i do Libanu przywiodę ich; ale im miejsca stawać nie będzie.
Ndidzawabweretsa kuchokera ku Igupto ndipo ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku Asiriya. Ndidzawabwezera ku Giliyadi ndi ku Lebanoni, mpaka malo woti nʼkukhalamo adzatheratu.
11 Przetoż dla ciasności przez morze przejdzie, i rozbije na morzu wały, i wyschną wszystkie głębokości rzeki; tedy będzie zniżona pycha Assyryi, a sceptr od Egiptu odjęty będzie.
Adzawoloka nyanja ya masautso; nyanja yokokoma idzagonja ndipo madzi onse a mu Nailo adzaphwa. Kudzikuza kwa Asiriya kudzatha ndipo ndodo yaufumu ya Igupto idzathyoka.
12 Zmocnię ich też w Panu, a w imieniu jego chodzić będą, mówi Pan.
Ndidzalimbitsa iwo mwa Yehova ndipo adzayenda mʼdzina lake,” akutero Yehova.

< Zachariasza 10 >