< Pieśń nad Pieśniami 7 >
1 O jako piękne są nogi twoje w trzewikach, o córko książęca! Opasania biódr twoich są jako zawieszenia, ręką dobrego rzemieślnika urobione.
Iwe namwali waufumu, mapazi ako ngokongola mu nsapato wavalazo! Ntchafu zako nʼzowumbika bwino ngati miyala yamtengowapatali, ntchito ya manja ya mmisiri waluso.
2 Pępek twój jako czasza okrągła, która nie jest bez napoju; brzuch twój jest jako bróg pszenicy osadzony lilijami.
Mchombo wako uli ngati chikho chowumbika bwino chimene nthawi zonse ndi chodzaza ndi vinyo. Chiwuno chako ndi choningʼa ngati mtolo wa tirigu utazunguliridwa ndi maluwa okongola.
3 Obie piersi twoje są jako dwoje bliźniąt młodych sarniąt.
Mawere ako akuoneka ngati ana awiri a mbawala, ngati mphoyo zamapasa.
4 Szyja twoja jako wieża z kości słoniowych; oczy twoje jako sadzawki w Hesebon podle bramy Batrabim; nos twój jako wieża na Libanie, która patrzy ku Damaszkowi.
Khosi lako lili see! ngati nsanja ya mnyanga wa njovu. Maso ako ali ngati mayiwe a ku Hesiboni, amene ali pafupi ndi chipata cha Bati Rabimu. Mphuno yako ili ngati nsanja ya ku Lebanoni, yoyangʼana ku Damasiko.
5 Głowa twoja na tobie jako Karmel, a włosy głowy twojej jako szarłat. Król widząc cię byłby jako przywiązany na gankach swoich.
Mutu wako uli bwinobwino nengʼaa ngati phiri la Karimeli. Tsitsi lako lili ngati nsalu yakuda yaufumu; mfumu yakopeka ndi maonekedwe ake okongola.
6 O jakożeś piękna, i jako wdzięczna, o miłości przerozkoszna!
Ndiwe wokongola kwambiri ndiponso wosangalatsa, iwe wokondedwa, namwali wokondweretsawe!
7 Ten twój wzrost podobny jest palmie, a piersi twoje gronom.
Msinkhu wako uli ngati mtengo wa mgwalangwa, ndipo mawere ako ali ngati phava la zipatso.
8 Rzekłem: Wstąpię na palmę, dosięgnę wierzchów jej. Niechajże mi tedy będą piersi twoje jako grona winne, a wonność nozdrzy twoich jako jabłek wonnych;
Ndinati, “Ndikwera mtengo wa mgwalangwa; ndidzathyola zipatso zake.” Mawere ako ali ngati maphava a mphesa, fungo la mpweya wako lili ngati ma apulosi,
9 A usta twoje jako wino wyborne, które na prost bardzo mile płynie i sprawóje, że mówią wargi śpiących.
ndipo pakamwa pako pali ngati vinyo wokoma kwambiri. Mkazi Tsono vinyo ameneyu amuthirire wachikondi wanga, ayenderere bwino pa milomo yake ndi mano ake.
10 Jam jest miłego mego, a do mnie jest rządza jego.
Wokondedwayo ine ndine wake, ndipo chilakolako chake chili pa ine.
11 Przyjdź, miły mój; wyjdziemy na pole, a przenocujemy we wsiach.
Bwera wachikondi wanga, tiye tipite ku madera a ku midzi, tikagone ku midzi.
12 Rano wstaniemy do winnic; oglądamy, jeźli kwitnie winna macica, jeźli się zawiązują gronka, kwitnąli jabłka granatowe; tam ci oświadczę miłości moje.
Tiye tilawirire mmamawa kupita ku minda ya mpesa, tikaone ngati mitengo ya mpesa yayamba kuphukira, ngati maluwa ake ayamba kuoneka, komanso ngati makangadza ayamba kuonetsa maluwa. Kumeneko ndidzakuonetsa chikondi changa.
13 Polne jabłuszka wydały wonność swoję, a przede drzwiami naszemi są wszystkie owoce wdzięczne, nowe i stare, którem tobie, miły mój! zachowała.
Mitengo ya mankhwala a chisulo ikupereka fungo lake labwino, ndipo pa khomo pathu pali zipatso zonse zokoma, zatsopano ndi zakale zomwe, zimene ndakusungira wokondedwa wanga.