< Pieśń nad Pieśniami 4 >

1 O jakoś ty piękna, przyjaciółko moja; o jakoś ty piękna! Oczy twoje jako oczy gołębicy między kędzierzami twemi; włosy twoje jako trzoda kóz, które widać na górze Galaad.
Ndiwe wokongoladi wokondedwa wanga! Ndithudi, ndiwe wokongola! Maso ako ali ngati nkhunda kumbuyo kwa nsalu yophimba kumutu. Tsitsi lako lili ngati gulu la mbuzi zikutsetsereka kuchokera ku Giliyadi.
2 Zęby twoje jako stado owiec jednakich, gdy wychodzą z kąpieli, z których każda miewa po dwojgu, a niepłodnej niemasz między niemi.
Mano ako ali ngati gulu la nkhosa zomwe zangometedwa kumene, zochokera kozisambitsa kumene. Iliyonse ili ndi ana amapasa; palibe imene ili yokha.
3 Wargi twoje jako sznur karmazynowy, a wymowa twoja wdzięczna; skronie twoje między kędzierzami twemi są jako sztuka jabłka granatowego.
Milomo yako ili ngati mbota yofiira; pakamwa pako ndi pokongola kwambiri. Kukhalira kumbuyo kwa nsalu yako yophimba kumutuyo, masaya ako akuoneka ngati mabandu a makangadza.
4 Szyja twoja jako wieża Dawidowa z obronami wystawiona, w której tysiąc tarczy wisi, i wszystka broń mocarzów.
Khosi lako lili ngati nsanja ya Davide, yomangidwa bwino ndi yosalala; pa nsanja imeneyo pali zishango 1,000, zishango zonsezo za anthu ankhondo.
5 Obie piersi twoje jako dwoje bliźniąt sarnich, które się pasą między lilijami;
Mawere ako ali ngati tiana tiwiri ta nswala, ngati ana amapasa a nswala amene akudya pakati pa maluwa okongola.
6 Ażby się okazał ten dzień, a cienie przeminęły, wnijdę na górę myrry, i na pagórek kadzidła.
Kamphepo kamadzulo kakayamba kuwuzira ndipo mithunzi ikayamba kuthawa, ndidzapita ku phiri la mure ndi ku chitunda cha lubani.
7 Wszystkaś ty jest piękna, przyjaciółko moja! a zmazy niemasz na tobie.
Ndiwe wokongola kwambiri wokondedwa wanga; palibe chilema pa iwe.
8 Pójdziesz ze mną z Libanu, o oblubienico moja! ze mną z Libanu pójdziesz, a spojrzysz z wierzchu góry Amana, z wierzchu góry Sanir i Hermon, z jaskiń lwich, i z gór lampartowych.
Tiye tichoke ku Lebanoni iwe mkwatibwi wanga, tiye tichoke ku Lebanoni, utsikepo pa msonga ya Amana, kuchoka pa msonga ya phiri la Seniri, pamwamba penipeni pa Herimoni, kuchoka ku mapanga a mikango ndiponso kumapiri kumene akambuku amavutitsa.
9 Ujęłaś serce moje, siostro moja, oblubienico moja! ujęłaś serce moje jednem okiem twojem, i jednym łańcuszkiem na szyi twojej.
Iwe mlongo wanga, mkwatibwi wanga, wanditenga mtima, iwe wanditenga mtima ndi kapenyedwe ka maso ako, ndiponso ndi umodzi mwa mikanda ya mʼkhosi mwako.
10 O jakoż są ucieszne miłości twoje, siostro moja! oblubienico moja! O jako daleko zacniejsze miłości twoje, niż wino, a wonność maści twoich nad wszystkie rzeczy wonne!
Iwe mlongo wanga, mkwatibwi wanga, chikondi chako nʼchosangalatsa! Chikondi chako nʼchosangalatsa kwambiri kupambana vinyo, ndiponso fungo la mafuta ako ndi lopambana zonunkhiritsa zonse!
11 Plastrem miodu opływają wargi twoje, oblubienico moja! miód i mleko pod językiem twoim, a wonność szat twoich, jako wonność Libanu.
Iwe mkwatibwi wanga, milomo yako ikuchucha uchi ngati chisa cha njuchi; pansi pa lilime lako pali mkaka ndi uchi. Fungo lonunkhira la zovala zako likumveka ngati fungo la ku Lebanoni.
12 Ogrodem zamknionym jesteś, siostro moja, oblubienico moja! źródło zamknione, zdrój zapieczętowany.
Iwe mlongo wanga, mkwatibwi wanga, ndiwe munda wopiringidzidwa; ndiwe kasupe wotchingidwa, chitsime chotetezedwa.
13 Szczepki twoje są sadem jabłek granatowych z owocem wdzięcznym cyprysu i szpikanardu;
Zomera zako ndi munda wa zipatso za makangadza; muli zipatso zokoma kwambiri, muli hena ndi nadi,
14 Szpikanardu, i szafranu, kasyi, i cynamonu, ze wszystkiemi drzewami kadzidło przynoszącemi! myrry, i aloesu, ze wszystkiemi osobliwemi rzeczami wonnemi.
nadi ndi safiro, kalamusi ndi sinamoni, komanso mtengo uliwonse wonunkhira bwino. Mulinso mure ndi aloe ndi zonunkhiritsa zonse zabwino kwambiri.
15 O źródło ogrodne, zdroju wód żywych, które płyną z Libanu!
Iwe ndiwe kasupe wa mʼmunda, chitsime cha madzi oyenda, mtsinje wa madzi ochokera ku Lebanoni.
16 Powstań wietrze północny, a przyjdź wietrze z południa, przewiej ogród mój; niech płyną wonności jego, niech przjdzie miły mój do ogrodu swego, a niech je rozkoszne owoce swoje.
Dzuka, iwe mphepo yakumpoto, ndipo bwera, iwe mphepo yakummwera! Uzira pa munda wanga, kuti fungo lake lonunkhira lifalikire ponseponse. Bwenzi langa alowe mʼmunda mwake ndi kudya zipatso zake zabwino kwambiri.

< Pieśń nad Pieśniami 4 >