< Pieśń nad Pieśniami 1 >

1 Pieśń najprzedniejsza z pieśni Salomonowych.
Nyimbo ya Solomoni, nyimbo yoposa nyimbo zonse.
2 Niech mię pocałuje pocałowaniem ust swoich; albowiem lepsze są miłości twoje niż wino.
Undipsompsone ndi milomo yako chifukwa chikondi chako nʼchokoma kuposa vinyo.
3 Dla wonności wyborne są maści twoje; imię twoje jest jako olejek rozlany; przetoż cię panienki umiłowały.
Mafuta ako odzola ndi onunkhira bwino; dzina lako lili ngati mafuta onunkhira otsanulidwa. Nʼchifukwa chake atsikana amakukonda!
4 Pociągnijże mię, a pobieżymy za toba. Wprowadził mię król do pokojów swoich; przetoż się w tobie radować i weselić będziemy milości twoje raczej niż wino; bo uprzejmi milują cię.
Nditenge ndipo ndizikutsata, tiye tifulumire! Mfumu indilowetse mʼchipinda chake. Abwenzi Ife timasangalala ndi kukondwera nawe, tidzatamanda chikondi chako kupambana vinyo. Mkazi Amachita bwinotu potamanda iwe!
5 Czarnamci, alem wdzięczna, o córki Jeruzalemskie! Jestem jako namioty Kedarskie, jako opony Salomonowe.
Ndine wakuda, komatu ndine wokongola, inu akazi a ku Yerusalemu, ine ndine wakuda ngati tenti ya ku Kedara, ngati makatani a tenti ya Solomoni.
6 Nie patrzajcie na mię, żem jest śniada; bo mię opalilo słonce. Synowie matki mojej rozpaliwszy się przeciwko mnie, postanowili mię, abym strzegła winnic; a winnicy mojej, którąm miała, nie strzegłam.
Musandiyangʼane monyoza chifukwa ndine wakuda, ndine wakuda chifukwa cha dzuwa. Alongo anga anandikwiyira ndipo anandigwiritsa ntchito mʼminda ya mpesa; munda wangawanga sindinawusamalire.
7 Oznajmijże mi ty, którego miłuje dusza moja, gdzie pasiesz? gdzie trzodzie dajesz odpoczywać w południe? albowiem przeczżebym miała być jako obłąkana przy trzodach towarzyszów twoich?
Ndiwuze iwe, amene ndimakukonda, kumene umadyetsa ziweto zako ndi kumene umagoneka nkhosa zako nthawi yamasana. Ndikhalirenji ngati mkazi wachiwerewere pambali pa ziweto za abwenzi ako?
8 Jeśli nie wiesz, o najpiękniejsza między niewiastami! wynijdźże śladem trzody, a paś koźlatka twoje przy budach pasterzy.
Ngati sukudziwa iwe wokongola kwambiri kuposa akazi ena, ngati sukudziwa, tsatira makwalala a nkhosa ndipo udyetse ana ambuzi pambali pa matenti a abusa.
9 Przyrównywam cię, o przyjaciółko moja! jeździe w wozach Faraonowych.
Iwe bwenzi langa, uli ngati kavalo wamkazi ku magaleta a Farao.
10 Jagody lica twego klejnotami są ozdobione, a szyja twoja łańcuchami.
Masaya ako ndi okongola ndi ndolo zamʼmakutuzo, khosi lako likukongola ndi mikanda yamiyala yamtengowapatali.
11 Naczynimyć klejnotów złotych z nakrapianiem srebrnem.
Tidzakupangira ndolo zagolide zokongoletsedwa ndi mikanda yasiliva.
12 Dotąd, pokąd król jest u stołu, szpikanard mój wydaje wonność swoję.
Pamene mfumu inali pa malo ake odyera, mafuta anga onunkhira anamveka fungo lake.
13 Jako snopek myrry jest mi miły mój na piersiach moich odpoczywający.
Wokondedwa wanga ali ngati kathumba ka mure kwa ine, kamene kamakhala pakati pa mawere angawa.
14 Miły mój jest mi jako grono cyprowe na winnicach, w Engaddy.
Wokondedwa wanga ali ngati mpukutu wa maluwa ofiira, ochokera ku minda ya mpesa ya ku Eni-Gedi.
15 O jakoś ty piękna, przyjaciółko moja, o jakoś ty piękna! oczy twoje jako oczy gołębicy.
Iwe wokondedwa wanga, ndiwe wokongoladi! Ndithu, ndiwe chiphadzuwa, maso ako ali ngati nkhunda.
16 O jakoś ty jest piękny, miły mój! i jako wdzięczny! nawet i to łoże nasze zieleni się.
Iwe bwenzi langa, ndiwe wokongoladi! Ndithu, ndiwe wokongoladi kwambiri! Ndipo malo athu ogonapo ndi msipu wobiriwira.
17 Belki domów naszych są cedrowe, a stropy nasze jodłowe.
Mitanda ya nyumba yathu ndi ya mkungudza, phaso lake ndi la mtengo wa payini.

< Pieśń nad Pieśniami 1 >