< Rzymian 5 >

1 Będąc tedy usprawiedliwieni z wiary, pokój mamy z Bogiem przez Pana naszego Jezusa Chrystusa;
Tsopano popeza tayesedwa olungama mwa chikhulupiriro, tili ndi mtendere ndi Mulungu kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu.
2 Przez któregośmy też przystęp otrzymali wiarą ku łasce, w której stoimy i chlubimy się nadzieją chwały Bożej.
Iyeyo ndiye amene anatsekulira njira mwachikhulupiriro yolowera mʼchisomo mʼmene takhazikikamo. Ndipo tikukondwerera chiyembekezo cha ulemerero wa Mulungu.
3 A nie tylko to, ale się też chlubimy z ucisków, wiedząc, iż ucisk cierpliwość sprawuje,
Koma si pokhapo ayi, koma ife tikukondweranso mʼmasautso athu chifukwa tikudziwa kuti masautso amatiphunzitsa kupirira.
4 A cierpliwość doświadczenie, a doświadczenie nadzieję,
Ndipo kupirira kumabweretsa makhalidwe, makhalidwe amabweretsa chiyembekezo.
5 A nadzieja nie pohańbia, przeto iż miłość Boża rozlana jest w sercach naszych przez Ducha Świętego, który nam jest dany.
Ndipo chiyembekezo chimenechi sichitikhumudwitsa chifukwa Mulungu mwa Mzimu Woyera, amene Iye anatipatsa, wadzaza mʼmitima mwathu ndi chikondi chake.
6 Albowiem Chrystus, gdy jeszcze byliśmy mdłymi, według czasu umarł za niepobożne.
Pakuti pa nthawi yake, tikanali ochimwa, Khristu anatifera anthu osapembedzafe.
7 Choć ledwie by kto umarł za sprawiedliwego; wszakże za dobrego snaćby się kto umrzeć ważył.
Sizichitika kawirikawiri kuti munthu wina afere munthu wolungama, ngakhale kuti chifukwa cha munthu wabwino wina atha kulimba mtima kumufera.
8 Lecz zaleca Bóg miłość swoję ku nam, że gdy jeszcze byliśmy grzesznymi, Chrystus za nas umarł.
Koma Mulungu anaonetsa chikondi chake kwa ife chifukwa pamene tinali ochimwabe, Khristu anatifera.
9 Daleko tedy więcej teraz usprawiedliwieni będąc krwią jego, zachowani będziemy przez niego od gniewu.
Popeza chifukwa cha magazi ake ife tapezeka olungama pamaso pa Mulungu, Iyeyo adzatipulumutsa koposa kotani ku mkwiyo wa Mulungu.
10 Bo jeźliże będąc nieprzyjaciołmi, pojednaniśmy z Bogiem przez śmierć Syna jego; daleko więcej będąc pojednani, zachowani będziemy przez żywot jego.
Pakuti pamene tinali adani a Mulungu, tinayanjanitsidwa ndi Iye kudzera mu imfa ya Mwana wake. Nanga tidzapulumutsidwa bwanji kudzera mʼmoyo wake, titayanjanitsidwa naye?
11 A nie tylko to, ale się też chlubimy Bogiem przez Pana naszego Jezusa Chrystusa, przez któregośmy teraz pojednanie otrzymali.
Sikuti izi zili chomwechi chabe, koma timakondweranso mwa Mulungu kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu. Kudzera mwa Iye, ife tsopano tayanjanitsidwa ndi Mulungu.
12 Przetoż jako przez jednego człowieka grzech wszedł na świat, a przez grzech śmierć; tak też na wszystkich ludzi śmierć przyszła, ponieważ wszyscy zgrzeszyli.
Choncho monga momwe tchimo linalowa mʼdziko lapansi kudzera mwa munthu mmodzi, ndi imfa kudzera mu tchimo, mʼnjirayi imfa inafika kwa anthu onse pakuti onse anachimwa.
13 Albowiem aż do zakonu grzech był na świecie; ale grzech nie bywa przyczytany, gdy zakonu nie masz.
Pakuti Malamulo asanaperekedwe, tchimo linali mʼdziko lapansi. Koma pamene palibe Malamulo, tchimo silitengedwa kukhala tchimo.
14 Lecz śmierć królowała od Adama aż do Mojżesza i nad tymi, którzy nie zgrzeszyli, na podobieństwo przestępstwa Adamowego, który jest wzorem onego, który miał przyjść.
Komabe, imfa inalamulira kuyambira nthawi ya Adamu mpaka nthawi ya Mose. Inalamulira ngakhalenso pa iwo amene sanachimwe posamvera Malamulo monga anachitira Adamu. Adamuyo amene anali chifaniziro cha wina amene ankabwera.
15 Ale nie jako upadek, tak i dar z łaski; albowiem jeźli przez upadek jednego wiele ich pomarło, daleko więcej łaska Boża i dar z łaski onego jednego człowieka Jezusa Chrystusa na wiele ich opływała.
Koma sitingafananitse mphatso yaulereyo ndi kuchimwa kwa anthu. Pakuti ngati anthu ambiri anafa chifukwa cha kuchimwa kwa munthu mmodziyo, kuli koposa bwanji nanga chisomo cha Mulungu ndi mphatso zomwe zinabwera ndi chisomo cha munthu mmodzi, Yesu Khristu, ndi kusefukira kwa ambiri!
16 A dar nie jest taki, jako to, co przyszło przez jednego, który zgrzeszył. Albowiem wina jest z jednego upadku ku potępieniu, ale dar z łaski z wielu upadków ku usprawiedliwieniu.
Ndiponso, mphatso ya Mulungu sifanana ndi zotsatira za kuchimwa kwa munthu mmodzi. Chiweruzo chinatsatira tchimo la munthu mmodzi ndi kubweretsa kutsutsidwa koma mphatso inatsatira zolakwa zambiri ndi kubweretsa kulungamitsidwa.
17 Albowiem jeźli dla jednego upadku śmierć królowała przez jednego, daleko więcej, którzy obfitość onej łaski i dar sprawiedliwości przyjmują, w żywocie królować będą przez tegoż jednego Jezusa Chrystusa.
Pakuti ngati, chifukwa cha kulakwa kwa munthu mmodziyo, imfa inalamulira kudzera mwa munthu mmodziyo, kuli koposa bwanji nanga kwa iwo amene adzalandira chisomo chochuluka ndi mphatso yachilungamo, adzalamulira mʼmoyo kudzera mwa munthu mmodzi, Yesu Khristu.
18 Przetoż tedy jako przez jednego upadek na wszystkich ludzi przyszła wina ku potępieniu; tak też przez jednego usprawiedliwienie na wszystkich ludzi przyszedł dar ku usprawiedliwieniu żywota.
Choncho monga tchimo limodzi linabweretsa kutsutsika pa anthu onse, chimodzimodzinso ntchito imodzi yolungama inabweretsa chilungamo kwa anthu onse ndi kuwapatsa moyo.
19 Bo jako przez nieposłuszeństwo jednego człowieka wiele się ich stało grzesznymi; tak przez posłuszeństwo jednego człowieka wiele się ich stało sprawiedliwymi.
Pakuti kusamvera kwa munthu mmodzi kunasandutsa anthu ambiri kukhala ochimwa, chimodzimodzinso anthu ambiri adzasanduka olungama kudzera mwa munthu mmodzinso.
20 A zakon przytem nastąpił, aby obfitował grzech; lecz gdzie się grzech rozmnożył, tam łaska tem więcej obfitowała.
Malamulo a Mulungu anaperekedwa ndi cholinga chakuti anthu onse azindikire kuchuluka kwa machimo awo. Koma pamene machimo anachuluka, chisomo chinachuluka koposa.
21 Aby jako grzech królował ku śmierci, tak też aby łaska królowała przez sprawiedliwość ku żywotowi wiecznemu przez Jezusa Chrystusa, Pana naszego. (aiōnios g166)
Choncho monga momwe tchimo linkalamulira anthu ndi kubweretsa imfa pa iwo, chomwecho kunali koyenera kuti chisomo chilamulire pobweretsa chilungamo kwa anthu, ndi kuwafikitsa ku moyo wosatha mwa Yesu Khristu Ambuye athu. (aiōnios g166)

< Rzymian 5 >