< Objawienie 12 >

1 I ukazał się cud wielki na niebie: Niewiasta obleczona w słońce, a księżyc pod nogami jej, a na głowie jej była korona z dwunastu gwiazd;
Chizindikiro chachikulu chinaoneka kuthambo; mayi atavala dzuwa, mapazi ake ataponda mwezi, pamutu pake pali chipewa chaufumu chokhala ndi nyenyezi khumi ndi ziwiri.
2 A będąc brzemienna, wołała pracując ku porodzeniu i męczyła się, aby porodziła.
Mayiyo anali woyembekezera ndipo pa nthawi yake yochira analira mokuwa chifukwa cha ululu wakubala.
3 I ukazał się drugi cud na niebie, a oto smok wielki rydzy, mając siedm głów i rogów dziesięć, a na głowach jego siedm koron;
Kenaka ku thambo kunaonekanso chizindikiro china; chinjoka chachikulu kwambiri, chofiira chomwe chinali ndi mitu isanu ndi iwiri ndi nyanga khumi; pamutu uliwonse chitavala chipewa chaufumu.
4 A ogon jego ciągnął trzecią część gwiazd niebieskich i zrzucił je na ziemię; a smok on stanął przed niewiastą, która miała porodzić, aby skoro by porodziła, pożarł dziecię jej.
Mchira wake unakokolola gawo limodzi la magawo atatu a nyenyezi kuzichotsa ku thambo ndi kuziponya pa dziko lapansi. Chinjoka chija chinadzayima patsogolo pa mayi uja amene anali pafupi kuberekayu kuti mwanayo akangobadwa chimudye.
5 I urodziła syna, mężczyznę, który ma rządzić wszystkie narody laską żelazną; i porwane jest dziecię jej do Boga i do stolicy jego,
Mayiyo anabereka mwana wamwamuna amene adzalamulira anthu a mitundu ina yonse ndi ndodo yachitsulo. Ndipo mwanayo analandidwa ku dzanja la mayiyo ndi kupita naye kwa Mulungu ku mpando wake waufumu.
6 A niewiasta uciekła na pustynię, gdzie ma miejsce od Boga zgotowane, aby ją tam żywiono przez dni tysiąc dwieście i sześćdziesiąt.
Mayiyo anathawira ku chipululu ku malo kumene Mulungu anamukonzera, kumene akasamalidweko masiku 1,260.
7 I stała się bitwa na niebie. Michał i Aniołowie jego potykali się z smokiem, smok się też potykał i aniołowie jego.
Zitatero, kumwamba kunayambika nkhondo. Mikayeli ndi angelo ake kumenyana ndi chinjoka chija. Chinjokacho ndi angelo ake anabwezeranso.
8 Ale nie przemogli, ani miejsce ich dalej znalezione jest na niebie.
Koma analibe mphamvu ndipo anagonjetsedwa nathamangitsidwa kumwambako.
9 I zrzucony jest smok wielki, wąż on starodawny, którego zowią dyjabłem i szatanem, który zwodzi wszystek okrąg świata; zrzucony jest na ziemię i aniołowie jego z nim są zrzuceni.
Chinjoka chachikulu chija chinagwetsedwa pansi. Ichocho ndiye njoka yakalekale ija yotchedwa Mdierekezi kapena Satana, amene amasocheretsa anthu a pa dziko lonse lapansi. Chinaponyedwa pa dziko la pansi pamodzi ndi angelo ake.
10 I słyszałem głos wielki mówiący na niebie: Terazci się stało zbawienie i moc, i królestwo Boga naszego, i zwierzchność Chrystusa jego, iż zrzucony jest oskarżyciel braci naszych, który na nich skarżył przed oblicznością Boga naszego we dnie i w nocy.
Kenaka ndinamva mawu ofuwula kumwamba akunena kuti, “Tsopano chipulumutso, mphamvu, ufumu wa Mulungu wathu ndi ulamuliro wa Khristu wake zabwera. Pakuti woneneza abale athu uja, amene amangokhalira kuwaneneza pamaso pa Mulungu usana ndi usiku, wagwetsedwa pansi.
11 Ale go oni zwyciężyli przez krew Baranka i przez słowa świadectwa swego, a nie umiłowali duszy swojej aż do śmierci.
Abale athuwo anamugonjetsa ndi magazi a Mwana Wankhosa ndiponso mawu a umboni wawo. Iwo anadzipereka kwathunthu, moti sanakonde miyoyo yawo.
12 Przetoż rozweselcie się nieba! i wy, którzy mieszkacie na nich. Biada mieszkającym na ziemi i na morzu! iż zstąpił dyjabeł do was, mając wielki gniew, wiedząc, iż krótki czas ma.
Choncho, kondwerani, inu dziko lakumwamba ndi onse okhala kumeneko! Koma tsoka dziko lapansi ndi nyanja chifukwa Mdierekezi wagwetsedwa kwa inu! Iye wadzazidwa ndi ukali chifukwa akudziwa kuti nthawi yake ndi yochepa.”
13 A gdy wiedział smok, iż był zrzucony na ziemię, prześladował niewiastę, która była porodziła mężczyznę.
Pamene chinjokacho chinaona kuti chagwetsedwa pa dziko lapansi, chinayamba kuthamangitsa mayi uja amene anali atabala mwana wamwamunayu.
14 I dano niewieście dwa skrzydła orła wielkiego, aby leciała od obliczności wężowej na pustynię, na miejsce swoje, gdzie by ją żywiono przez czas i czasy, i połowę czasu.
Mayiyo anapatsidwa mapiko awiri a chiwombankhanga chachikulu kuti athawire ku malo ake aja a ku chipululu. Kumeneko adzasamalidwako zaka zitatu ndi theka kuti chinjoka chija chisamupeze.
15 I wypuścił wąż z gęby swojej za niewiastą wodę jako rzekę, chcąc sprawić, aby ją rzeka porwała.
Kenaka chinjoka chija chinalavulira mayiyo madzi ambiri ngati mtsinje, kuti madziwo amukokolole.
16 Ale ziemia ratowała niewiastę; i otworzyła ziemia usta swoje, i wypiła rzekę, którą był wypuścił smok z gęby swojej.
Koma dziko lapansi linamuthandiza mayiyo. Nthaka inatsekuka ndi kumeza mtsinje uja unachokera mʼkamwa mwa chinjokacho.
17 I rozgniewał się smok na niewiastę, i poszedł, aby walczył z drugimi z nasienia jej, którzy zachowują przykazania Boże i mają świadectwo Jezusa Chrystusa. I stanąłem na piasku morskim.
Pamenepo chinjokacho chinamupsera mtima mayiyo ndipo chinachoka kupita kukachita nkhondo ndi ana ena onse a mayiyo, ndiye kuti anthu amene anasunga malamulo a Mulungu ndi kuchitira umboni za Yesu.

< Objawienie 12 >