< Objawienie 10 >
1 I widziałem drugiego Anioła mocnego, zstępującego z nieba, obłokiem odzianego, a na głowie jego była tęcza, a oblicze jego jako słońce, a nogi jego jako słupy ognia.
Kenaka ndinaona mngelo wina wamphamvu akutsika kuchokera kumwamba. Anavala mtambo ndipo anali ndi utawaleza pamutu pake. Nkhope yake inali ngati dzuwa, ndipo miyendo yake inali ngati mizati yamoto.
2 A miał w ręce swojej książeczki otworzone i postawił nogę swoję prawą na morzu, a lewą na ziemi.
Mʼdzanja lake munali kabuku kakangʼono kotsekulidwa. Phazi lake lamanja linaponda mʼnyanja ndipo phazi lake lamanzere linaponda pa mtunda.
3 I zawołał głosem wielkim, jako lew ryczy; a gdy przestał wołać, mówiło siedm gromów głosy swoje.
Mngeloyo anafuwula kwambiri ngati kubangula kwa mkango. Atangofuwula, kunamveka kugunda kwa mabingu asanu ndi awiri.
4 A gdy odmówiło siedm gromów głosy swoje, miałem pisać; alem usłyszał głos z nieba, mówiący do mnie: Zapieczętuj to, co mówiło siedm gromów, a nie pisz tego.
Mabingu asanu ndi awiriwo atangogunda, ine ndinkati ndizilemba; koma ndinamva mawu kuchokera kumwamba kuti, “Zisunge mu mtima zimene mabingu asanu ndi awiriwo anena ndipo usazilembe.”
5 Tedy Anioł, któregom widział stojącego na morzu i na ziemi, podniósł rękę swoję ku niebu,
Kenaka mngelo amene ndinamuona ataponda mʼnyanja ndi ku mtunda uja, anakweza dzanja lake lamanja kumwamba.
6 I przysiągł przez Żyjącego na wieki wieków, który stworzył niebo i to, co w niem jest, i ziemię, i to, co na niej jest, i morze, i to, co w niem jest, że czasu już nie będzie. (aiōn )
Mngeloyo analumbira mʼdzina la Iye wokhala ndi moyo mpaka muyaya, amene analenga kumwamba ndi zonse zili kumeneko, dziko lapansi ndi zonse zili mʼmenemo, nyanja ndi zonse zili mʼmenemo, nati, “Pasakhalenso zochedwa tsopano! (aiōn )
7 Ale we dni głosu Anioła siódmego, gdy będzie trąbił, dokona się tajemnica Boża, jako opowiedział sługom swoim prorokom.
Koma patsala pangʼono kuti mngelo wachisanu ndi chiwiri uja awombe lipenga lake, chinsinsi cha Mulungu chidzachitika monga momwe analengezera kwa atumiki ake, aneneri.”
8 A głos, którym słyszał z nieba, zasię mówił ze mną i rzekł: Idź, a weźmij te książeczki otworzone z ręki Anioła stojącego na morzu i na ziemi.
Pamenepo mawu amene ndinamva kuchokera kumwamba aja, anandiyankhulanso, anati, “Pita katenge buku lotsekulidwalo mʼdzanja la mngelo amene waponda pa nyanja ndi pa mtundayo.”
9 I szedłem do Anioła, i rzekłem mu: Daj mi te książeczki. I rzekł mi: Weźmij, a zjedz je, a uczynią gorzkość w brzuchu twoim; ale w ustach twoich słodkie będą jako miód.
Choncho ndinapita kwa mngeloyo ndipo ndinamupempha kuti andipatse kabukuko. Iye anati, “Tenga, idya. Mʼmimba mwako kaziwawa koma mʼkamwa mwako kazizuna ngati uchi.”
10 I wziąłem książeczki z ręki Anioła i zjadłem je, a były w ustach moich słodkie jako miód; ale gdym je zjadł, gorzko było w brzuchu moim.
Ndinatenga kabukuko mʼdzanja la mngeloyo ndipo ndinadyadi. Mʼkamwa mwanga kankazuna ngati uchi, koma nditakameza, mʼmimbamu munkawawa.
11 I rzekł mi: Musisz zasię prorokować przed wielą ludzi i narodów, i języków, i królów.
Ndipo anandiwuza kuti, “Iwe uyenera kulalikiranso za mitundu yambiri ya anthu, za mayiko, ziyankhulo ndi za mafumu.”