< Psalmów 95 >
1 Pójdźcież, śpiewajmy Panu; wykrzykujmy skale zbawienia naszego.
Bwerani, tiyeni timuyimbire Yehova mwachimwemwe, tiyeni tifuwule kwa Thanthwe la chipulumutso chathu
2 Uprzedźmy oblicze jego z chwałą; psalmy mu śpiewajmy.
Tiyeni tibwere pamaso pake ndi chiyamiko ndipo mupembedzeni Iyeyo ndi zida zoyimbira ndi nyimbo.
3 Albowiem Pan jest Bóg wielki, i król wielki nade wszystkich bogów.
Pakuti Yehova ndi Mulungu wamkulu, mfumu yayikulu pamwamba pa milungu yonse.
4 W jegoż rękach są głębokości ziemi, i wierzchy gór jego są.
Mʼmanja mwake muli maziko ozama a dziko lapansi, ndipo msonga za mapiri ndi zake.
5 Jegoż jest morze, bo je on uczynił; i ziemia, którą ręce jego ukształtowały.
Nyanja ndi yake, pakuti anayilenga ndi Iye, ndipo manja ake anawumba mtunda wowuma.
6 Pójdźcie, kłaniajmy się, a upadajmy przed nim; klękajmy przed Panem, stworzycielem naszym.
Bwerani, tiyeni tiwerame pomulambira, tiyeni tigwade pamaso pa Yehova Mlengi wathu;
7 Onci jest zaiste Bóg nasz, a myśmy lud pastwiska jego, i owce rąk jego. Dziś, jeźli głos jego usłyszycie,
pakuti Iye ndiye Mulungu wathu ndipo ife ndife anthu a pabusa pake, ndi nkhosa za mʼdzanja lake. Lero ngati inu mumva mawu ake,
8 Nie zatwardzajcież serca swego, jako w Meryba, a jako czasu kuszenia na puszczy.
musawumitse mitima yanu monga momwe munachitira pa Meriba, monga munachitira tsiku lija pa Masa mʼchipululu.
9 Kiedy mię kusili ojcowie wasi, doświadczylić mię, i widzieli sprawy moje.
Kumene makolo anu anandiyesa ndi kundiputa, ngakhale anaona zimene Ine ndinazichita.
10 Przez czterdzieści lat miałem spór z tym narodem, i rzekłem: Lud ten błądzi sercem, a nie poznali dróg moich;
Kwa zaka makumi anayi ndinali wokwiya ndi mʼbado umenewo; ndipo ndinati, “Iwo ndi anthu amene mitima yawo imasochera ndipo sanadziwe njira zanga.”
11 Którymem przysiągł w popędliwości mojej, że nie wnijdą do odpocznienia mego.
Choncho ndili chikwiyire, ndinalumbira kuti, “Iwowa sadzalowa ku malo anga a mpumulo.”