< Psalmów 79 >

1 Psalm podany Asafowi. O Boże! wtargnęli poganie w dziedzictwo twoje, splugawili kościół twój święty, obrócili Jeruzalem w kupy gruzu.
Salimo la Asafu. Inu Mulungu, anthu a mitundu ina alowerera mʼcholowa chanu; ayipitsa Nyumba yanu yoyera, asandutsa Yerusalemu kukhala bwinja.
2 Dali trupy sług twoich na pokarm ptastwu powietrznemu, ciała świętych twoich bestyjom ziemskim.
Iwo anapereka mitembo ya atumiki anu kwa mbalame zamlengalenga ngati chakudya, matupi a oyera mtima anu kwa zirombo za dziko lapansi.
3 Wylali krew ich jako wodę około Jeruzalemu, a nie był, ktoby ich pochował.
Akhetsa magazi monga madzi kuzungulira Yerusalemu yense, ndipo palibe wina woti ayike mʼmanda anthu akufa.
4 Staliśmy się pohańbieniem u sąsiadów naszych; śmiechowiskiem i igrzyskiem u tych, którzy są około nas.
Ife ndife chinthu chonyozeka kwa anansi athu, choseketsa ndi cholalatiridwa kwa iwo amene atizungulira.
5 Dokądże, o Panie? azaż na wieki gniewać się będziesz? a jako ogień pałać będzie zapalczywość twoja?
Mpaka liti Inu Yehova? Kodi mudzakwiya mpaka muyaya? Kodi mpaka liti nsanje yanu idzayaka ngati moto?
6 Wylij gniew twój na pogan, którzy cię nie znają, i na królestwa, które imienia twego nie wzywają.
Khuthulirani ukali wanu pa anthu a mitundu ina amene sakudziwani Inu, pa maufumu amene sayitana pa dzina lanu;
7 Albowiemci pożarli Jakóba, a mieszkanie jego spustoszyli.
pakuti iwo ameza Yakobo ndi kuwononga dziko lawo.
8 Nie wspominajże nam przeszłych nieprawości naszych; niech nas rychło uprzedzi miłosierdzie twoje, bośmy bardzo znędzeni.
Musatilange chifukwa cha machimo a makolo athu chifundo chanu chibwere msanga kukumana nafe, pakuti tili ndi chosowa chachikulu.
9 Wspomóżże nas, o Boże zbawienia naszego! dla chwały imienia twego, a wyrwij nas, i bądź miłościw grzechom naszym dla imienia twego.
Tithandizeni Inu Mulungu Mpulumutsi wathu, chifukwa cha ulemerero wa dzina lanu; tipulumutseni ndi kutikhululukira machimo athu chifukwa cha dzina lanu.
10 Przeczżeby mieli mówić poganie: Gdzież jest Bóg ich? Bądź znacznym między poganami, przed oczyma naszemi, dla pomsty krwi sług twoich, która jest wylana.
Chifukwa chiyani anthu a mitundu ina akuti, “Ali kuti Mulungu wawo?” Ife tikuona, zidziwike pakati pa anthu a mitundu ina kuti mumabwezera chilango chifukwa cha magazi amene anakhetsedwa a atumiki anu.
11 Niech przyjdzie przed oblicze twoje narzekanie więźniów, a według wielkości ramienia twego zachowaj ostatki tych, co są na śmierć skazani.
Kubuwula kwa anthu a mʼndende kufike pamaso panu; ndi mphamvu ya dzanja lanu muwasunge amene aweruzidwa kuti aphedwe.
12 A oddaj sąsiadom naszym siedmiorako na łono ich za pohańbienie ich, któreć uczynili, o Panie!
Mubwezere kwa anansi athu kasanu nʼkawiri kunyoza kumene ananyoza Inu Ambuye.
13 Ale my lud twój i owce pastwiska twego, będziemy cię wysławiali na wieki; od narodu do narodu będziemy opowiadać chwałę twoję.
Pamenepo ife anthu anu, nkhosa za pabusa panu, tidzakutamandani kwamuyaya, kuchokera mʼbado ndi mʼbado tidzafotokoza za matamando anu.

< Psalmów 79 >