< Psalmów 78 >
1 Pieśń wyuczająca podana Asafowi. Słuchaj, ludu mój! zakonu mego; nakłońcież uszów swych do słów ust moich.
Ndakatulo ya Asafu. Inu anthu anga imvani chiphunzitso changa; mvetserani mawu a pakamwa panga.
2 Otworzę w podobieństwie usta moje, a będę opowiadał przypowiastki starodawne.
Ndidzatsekula pakamwa panga mʼmafanizo, ndidzayankhula zinthu zobisika, zinthu zakalekale
3 Cośmy słyszeli, i poznali, i co nam ojcowie nasi opowiadali.
zimene tinazimva ndi kuzidziwa, zimene makolo athu anatiwuza.
4 Nie zataimy tego przed synami ich, którzy przyszłym potomkom swoim opowiadać będą chwały Pańskie, i moc jego, i cuda jego, które uczynił.
Sitidzabisira ana awo, tidzafotokozera mʼbado wotsatira ntchito zotamandika za Yehova, mphamvu zake, ndi zozizwitsa zimene Iye wachita.
5 Bo wzbudził świadectwo w Jakóbie, a zakon wydał w Izraelu; przykazał ojcom naszym, aby to do wiadomości podawali synom swoim,
Iye anapereka mawu wodzichitira umboni kwa Yakobo ndi kukhazikitsa lamulo mu Israeli, zimene analamulira makolo athu kuphunzitsa ana awo,
6 Aby poznał wiek potomny, synowie, którzy się narodzić mieli, a oni zaś powstawszy, aby to opowiadali synom swoim;
kotero kuti mʼbado wotsatira uthe kuzidziwa, ngakhale ana amene sanabadwe, ndi kuti iwo akafotokozere ana awonso.
7 Aby pokładali w Bogu nadzieję swoję, a nie zapominali na sprawy Boże, ale strzegli przykazań jego;
Choncho iwo adzakhulupirira Mulungu ndipo sadzayiwala ntchito zake koma adzasunga malamulo ake.
8 Aby się nie stali jako ojcowie ich narodem odpornym i nieposłusznym, narodem, który nie wygotował serca swego, aby był wierny Bogu duch jego.
Iwo asadzakhale monga makolo awo, mʼbado wosamvera ndi wowukira, umene mitima yake inali yosamvera Mulungu, umene mizimu yake inali yosakhulupirika kwa Iye.
9 Albo jako synowie Efraimowi zbrojni, którzy, choć umieli z łuku strzelać, wszakże w dzień wojny tył podali.
Anthu a ku Efereimu, ngakhale ananyamula mauta, anathawabe pa nthawi ya nkhondo;
10 Bo nie przestrzegali przymierza Bożego, a według zakonu jego zbraniali się chodzić.
iwo sanasunge pangano la Mulungu ndipo anakana kukhala mʼmoyo wotsatira lamulo lake.
11 Zapomnieli na sprawy jego, i na dziwne dzieła jego, które im pokazywał.
Anayiwala zimene Iye anachita, zozizwitsa zimene anawaonetsa.
12 Przed ojcami ich czynił cuda w ziemi Egipskiej, na polu Soan.
Iyeyo anachita zodabwitsa makolo athu akuona, mʼdziko la Igupto, mʼchigawo cha Zowani.
13 Rozdzielił morze, i przeprowadził ich, i sprawił, że stanęły wody jako kupa.
Anagawa nyanja pakati ndi kudutsitsapo iwowo, Iye anachititsa madzi kuyima chilili ngati khoma.
14 Prowadził ich w obłoku we dnie, a każdej nocy w jasnym ogniu.
Anawatsogolera ndi mtambo masana ndi kuwala kwa moto usiku wonse.
15 Rozszczepił skały na puszczy, a napoił ich, jako z przepaści wielkich.
Iye anangʼamba miyala mʼchipululu ndi kuwapatsa madzi ochuluka ngati a mʼnyanja zambiri;
16 Wywiódł strumienie ze skały, a uczynił, że wody ciekły jako rzeki.
Anatulutsa mitsinje kuchokera mʼmingʼalu ya miyala ndi kuyenda madzi ngati mitsinje.
17 A wszakże oni przyczynili grzechów przeciwko niemu, a wzruszyli Najwyższego na puszczy do gniewu;
Komabe iwowo anapitiriza kumuchimwira Iye, kuwukira Wammwambamwamba mʼchipululu.
18 I kusili Boga w sercu swem, żądając pokarmu według lubości swojej.
Ananyoza Mulungu mwadala pomuwumiriza kuti awapatse chakudya chimene anachilakalaka.
19 A mówili przeciwko Bogu temi słowy: Izali może Bóg zgotować stół na tej puszczy?
Iwo anayankhula motsutsana naye ponena kuti, “Kodi Mulungu angatipatse chakudya mʼchipululu?
20 Oto uderzył w skałę, a wypłynęły wody, i rzeki wezbrały; izali też będzie mógł dać chleb? Izali nagotuje mięsa ludowi swemu?
Iye atamenya thanthwe madzi anatuluka, ndipo mitsinje inadzaza ndi madzi. Koma iye angatipatsenso ife chakudya? Kodi angapereke nyama kwa anthu akewa?”
21 Przetoż usłyszawszy to Pan, rozgniewał się, a ogień się zapalił przeciw Jakóbowi, także i popędliwość powstała przeciw Izraelowi;
Yehova atawamva anakwiya kwambiri; moto wake unayaka kutsutsana ndi Yakobo, ndipo mkwiyo wake unauka kutsutsana ndi Israeli,
22 Przeto, iż nie wierzyli Bogu, a nie mieli nadziei w zbawieniu jego.
pakuti iwo sanakhulupirire Mulungu kapena kudalira chipulumutso chake.
23 Choć był rozkazał obłokom z góry, i forty niebieskie otworzył.
Komabe Iye anapereka lamulo kwa mitambo mmwamba ndi kutsekula makomo a mayiko akumwamba;
24 I spuścił im jako deszcz mannę ku pokarmowi, a pszenicę niebieską dał im.
anagwetsa mana kuti anthu adye, anawapatsa tirigu wakumwamba.
25 Chleb mocarzów jadł człowiek, a zesłał im pokarmów do sytości.
Anthu anadya buledi wa angelo, Iye anawatumizira chakudya chonse chimene akanatha kudya.
26 Obrócił wiatr ze wschodu na powietrzu, a przywiódł mocą swą wiatr z południa;
Anamasula mphepo ya kummwera kuchokera kumwamba, ndi kutsogolera mphepo ya kummwera mwa mphamvu zake.
27 I spuścił na nich mięso jako proch, i ptastwo skrzydlate jako piasek morski;
Iye anawagwetsera nyama ngati fumbi, mbalame zowuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja.
28 Spuścił je w pośród obozu ich, wszędy około namiotów ich.
Anazibweretsa kwa iwo mʼkati mwa misasa yawo, kuzungulira matenti awo onse.
29 I jedli, a nasyceni byli hojnie, i dał im, czego żądali.
Iwo anadya mpaka anatsala nazo zochuluka pakuti Iye anawapatsa zimene anazilakalaka.
30 A gdy jeszcze nie wypełnili żądości swej, gdy jeszcze pokarm był w ustach ich:
Koma iwowo anasiya kudya chakudya anachilakalakacho, chakudya chili mʼkamwa mwawobe,
31 Tedy zapalczywość Boża przypadła na nich, i pobił tłustych ich, a przedniejszych z Izraela poraził.
mkwiyo wa Mulungu unawayakira; Iye anapha amphamvu onse pakati pawo, kugwetsa anyamata abwino kwambiri mu Israeli.
32 Ale w tem wszystkiem jeszcze grzeszyli, i nie wierzyli cudom jego;
Ngakhale zinali chomwechi, iwo anapitirira kuchimwa; ngakhale anaona zozizwitsa zakezo iwowo sanakhulupirirebe.
33 Przetoż sprawił, że marnie dokonali dni swoich, i lat swoich w strachu.
Kotero Mulungu anachepetsa masiku awo kuti azimirire ngati mpweya. Iye anachepetsa zaka zawo kuti zithere mʼmasautso.
34 Gdy ich tracił, jeźliże go szukali, i nawracali się, a szukali z rana Boga,
Mulungu atawapha, iwo amamufunafuna Iyeyo; iwo ankatembenukiranso kwa Iye mwachangu.
35 Przypominając sobie, iż Bóg był skałą ich, a Bóg najwyższy odkupicielem ich:
Ankakumbukira kuti Mulungu ndiye Thanthwe lawo, kuti Mulungu Wammwambamwamba ndiye Mpulumutsi wawo.
36 (Aczkolwiek pochlebiali mu usty swemi, i językiem swoim kłamali mu;
Komabe ankamuthyasika ndi pakamwa pawo, kumunamiza ndi malilime awo;
37 A serce ich nie było szczere przed nim, ani wiernymi byli w przymierzu jego.)
Mitima yawo sinali yokhazikika pa Iye, iwo sanakhulupirike ku pangano lake.
38 On jednak będąc miłosierny odpuszczał nieprawości ich, a nie zatracał ich, ale częstokroć odwracał gniew swój, a nie pobudzał wszystkiego gniewu swego;
Komabe Iye anali wachifundo; anakhululukira mphulupulu zawo ndipo sanawawononge. Nthawi ndi nthawi Iye anabweza mkwiyo wake ndipo sanawutse ukali wake wonse.
39 Bo pamiętał, że są ciałem, wiatrem, który odchodzi, a nie wraca się zaś.
Iye anakumbukira kuti iwo anali anthu chabe, mphepo yopita imene sibwereranso.
40 Jako go często draźnili na puszczy, i do boleści przywodzili na pustyniach?
Nthawi zambiri iwo ankamuwukira Iye mʼchipululu ndi kumumvetsa chisoni mʼdziko lopanda kanthu!
41 Bo coraz kusili Boga, a Świętemu Izraelskiemu granice zamierzali.
Kawirikawiri iwo ankamuyesa Mulungu; ankamuputa Woyera wa Israeli.
42 Nie pamiętali na rękę jego, i na on dzień, w który ich wybawił z utrapienia;
Sanakumbukire mphamvu zake, tsiku limene Iye anawawombola kwa ozunza,
43 Gdy czynił w Egipcie znaki swoje, a cuda swe na polu Soan;
tsiku limene Iyeyo anaonetsa poyera zizindikiro zozizwitsa zake mu Igupto, zozizwitsa zake mʼchigawo cha Zowani.
44 Gdy obrócił w krew rzeki ich, i strumienie ich, tak, że z nich pić nie mogli.
Iye anasandutsa mitsinje yawo kukhala magazi; Iwo sanathe kumwa madzi ochokera mʼmitsinje yawo.
45 Przepuścił na nich rozmaite muchy, aby ich kąsały, i żaby, aby ich gubiły:
Iye anawatumizira magulu a ntchentche zimene zinawawononga, ndiponso achule amene anawasakaza.
46 I dał chrząszczom urodzaje ich, a prace ich szarańczy.
Iye anapereka mbewu zawo kwa ziwala, zokolola zawo kwa dzombe.
47 Potłukł gradem szczepy ich, a drzewa leśnych fig ich gradem lodowym.
Iye anawononga mphesa zawo ndi matalala ndiponso mitengo yawo yankhuyu ndi chisanu.
48 I podał gradowi bydło ich, a majętność ich węglu ognistemu.
Iye anapereka ngʼombe zawo ku matalala, zoweta zawo ku zingʼaningʼani.
49 Posłał na nich gniew zapalczywości swojej, popędliwość, i rozgniewanie, i uciśnienie, przypuściwszy na nich aniołów złych.
Anakhuthula moto wa ukali wake pa iwo, anawapsera mtima nawakwiyira nʼkuwabweretsera masautso. Zimenezi zinali ngati gulu la angelo osakaza.
50 Wyprostował ścieżkę gniewowi swemu, nie zachował od śmierci duszy ich, i na bydło ich powietrze dopuścił;
Analolera kukwiya, sanawapulumutse ku imfa koma anawapereka ku mliri.
51 I pobił wszystko pierworodztwo w Egipcie, pierwiastki mocy ich w przybytkach Chamowych;
Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, zipatso zoyamba kucha za mphamvu zawo mʼmatenti a Hamu
52 Ale jako owce wyprowadził lud swój, a wodził ich jako stada po puszczy.
Koma Iye anatulutsa anthu ake ngati ziweto; anawatsogolera ngati nkhosa kudutsa mʼchipululu.
53 Wodził ich w bezpieczeństwie, tak, że się nie lękali, (a nieprzyjaciół ich okryło morze, )
Anawatsogolera bwinobwino kotero kuti analibe mantha koma nyanja inamiza adani awo.
54 Aż ich przywiódł do świętej granicy swojej, na onę górę, której nabyła prawica jego.
Kotero anawafikitsa ku malire a dziko lake loyera, ku dziko lamapiri limene dzanja lake lamanja linawatengera.
55 I wyrzucił przed twarzą ich narody, i sprawił, że im przyszły na sznur dziedzictwa ich, ażeby mieszkały w przybytkach ich pokolenia Izraelskie.
Iye anathamangitsa mitundu ya anthu patsogolo pawo ndipo anapereka mayiko awo kwa Aisraeli kuti akhale awo; Iye anakhazikitsa mafuko a Israeli mʼnyumba zawo.
56 A wszakże przecież kusili i draźnili Boga najwyższego, a świadectwa jego nie strzegli.
Koma iwo anayesa Mulungu ndi kuwukira Wammwambamwamba; sanasunge malamulo ake.
57 Ale się odwrócili, i przewrotnie się obchodzili, jako i ojcowie ich; wywrócili się jako łuk omylny.
Anakhala okanika ndi osakhulupirika monga makolo awo, anapotoka monga uta wosakhulupirika.
58 Bo go wzruszyli do gniewu wyżynami swemi, a rytemi bałwanami swemi pobudzili go do zapalczywości.
Anakwiyitsa Iyeyo ndi malo awo opembedzera mafano; anawutsa nsanje yake ndi mafano awo.
59 Co słysząc Bóg rozgniewał się, i zbrzydził sobie bardzo Izraela,
Pamene Mulungu anamva zimenezi, anakwiya kwambiri; Iye anakana Israeli kwathunthu.
60 Tak, że opuściwszy przybytek w Sylo, namiot, który postawił między ludźmi,
Anasiya nyumba ya ku Silo, tenti imene Iyeyo anayimanga pakati pa anthu.
61 Podał w niewolę moc swoję, i sławę swoję w ręce nieprzyjacielskie.
Anatumiza mphamvu zake ku ukapolo, ulemerero wake mʼmanja mwa adani.
62 Dał pod miecz lud swój, a na dziedzictwo swoje rozgniewał się.
Anapereka anthu ake ku lupanga; anakwiya kwambiri ndi cholowa chake.
63 Młodzieńców jego ogień pożarł, a panienki jego nie były uczczone.
Moto unanyeketsa anyamata awo, ndipo anamwali awo analibe nyimbo za ukwati;
64 Kapłani jego od miecza polegli, a wdowy jego nie płakały.
ansembe awo anaphedwa ndi lupanga, ndipo amayi awo amasiye sanathe kulira.
65 Lecz potem ocucił się Pan jako ze snu, jako mocarz wykrzykający od wina.
Kenaka Ambuye anakhala ngati akudzuka kutulo, ngati munthu wamphamvu wofuwula chifukwa cha vinyo.
66 I zaraził nieprzyjaciół swoich na pośladkach, a na wieczną hańbę podał ich.
Iye anathamangitsa adani ake; anawachititsa manyazi ku nthawi zonse.
67 Ale choć wzgardził namiotem Józefowym, a pokolenia Efraimowego nie obrał,
Kenaka Iye anakana matenti a Yosefe, sanasankhe fuko la Efereimu;
68 Wszakże obrał pokolenie Judowe, i górę Syon, którą umiłował.
Koma anasankha fuko la Yuda, phiri la Ziyoni limene analikonda.
69 I wystawił sobie jako pałac wysoki świątnicę swoję, jako ziemię, którą ugruntował na wieki.
Iye anamanga malo ake opatulika ngati zitunda, dziko limene analikhazikitsa kwamuyaya.
70 I obrał Dawida sługę swego, wziąwszy go z obór owczych;
Anasankha Davide mtumiki wake ndi kumuchotsa pakati pa makola ankhosa;
71 Gdy chodził za owcami kotnemi, przyprowadził go, aby pasł Jakóba, lud jego, i Izraela, dziedzictwo jego;
kuchokera koyangʼanira nkhosa anamubweretsa kuti akhale mʼbusa wa anthu ake, Yakobo, wa Israeli cholowa chake.
72 Który ich pasł w szczerości serca swego, a w roztropności rąk swoich prowadził ich.
Ndipo Davide anawaweta ndi mtima wolungama; ndi manja aluso anawatsogolera.