< Psalmów 77 >

1 Przedniejszemu śpiewakowi dla Jedytuna psalm Asafowy. Głos mój podnoszę do Boga, kiedy wołam; głos mój podnoszę do Boga, aby mię wysłuchał.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a Yedutuni. Salimo la Asafu. Ndinafuwulira Mulungu kupempha thandizo; ndinafuwula mokweza kwa Mulungu kuti anditcherere khutu.
2 W dzień utrapienia mego szukałem Pana: wyciągałem w nocy ręce moje bez przestania, a nie dała się ucieszyć dusza moja.
Pamene ndinali pa masautso ndinafunafuna Ambuye; usiku ndinatambasula manja mosalekeza ndipo moyo wanga unakana kutonthozedwa.
3 Wspominałem na Boga, a trwożyłem sobą; rozmyślałem, a utrapieniem ściśniony był duch mój. (Sela)
Ndinakumbukira Inu Mulungu, ndipo ndinabuwula; ndinasinkhasinkha ndipo mzimu wanga unalefuka. (Sela)
4 Zatrzymywałeś oczy moje, aby czuły; potartym był, ażem nie mógł mówić.
Munagwira zikope zanga kuti ndisagone ndipo ndinavutika kwambiri kuti ndiyankhule.
5 Przychodziły mi na pamięć dni przeszłe i lata dawne.
Ndinaganizira za masiku akale, zaka zamakedzana;
6 Wspominałem sobie na śpiewanie moje; w nocym w sercu swem rozmyślał, i wywiadywał się o tem duch mój, mówiąc:
Ndinakumbukira nyimbo zanga usiku. Mtima wanga unasinkhasinkha ndipo mzimu wanga unafunsa kuti,
7 Izali mię na wieki odrzuci Pan, a więcej mi już łaski nie ukaże?
“Kodi Ambuye adzatikana mpaka muyaya? Kodi Iwo sadzaonetsanso kukoma mtima kwawo?
8 Izali do końca ustanie miłosierdzie jego, i koniec weźmie słowo od rodzaju aż do rodzaju? Izali zapomniał Bóg zmiłować się?
Kodi Chikondi chake chosatha chija chatheratu? Kodi malonjezo ake alephera nthawi yonse?
9 Izali zatrzymał w gniewie litości swoje? (Sela)
Kodi Mulungu wayiwala kukhala wokoma mtima? Kodi mu mkwiyo wake waleka chifundo chake?”
10 I rzekłem: Toć jest śmierć moja; wszakże prawica Najwyższego uczyni odmianę.
Ndipo ndinaganiza, “Pa izi ine ndidzapemphanso: zaka za dzanja lamanja la Wammwambamwamba.
11 Wspominać sobie będę na sprawy Pańskie, a przypominać sobie będę dziwne sprawy twoje, zdawna uczynione.
Ine ndidzakumbukira ntchito za Yehova; Ine ndidzakumbukira zodabwitsa zanu za kalekale.
12 I będę rozmyślał o wszelkiem dziele twojem, i o uczynkach twoich będę mówił:
Ndidzakumbukira ntchito zanu ndi kulingalira zodabwitsa zanu.”
13 Boże! święta jest droga twoja. Któryż Bóg jest tak wielki, jako Bóg nasz?
Njira zanu Mulungu ndi zoyera. Kodi ndi mulungu uti ali wamkulu kuposa Mulungu wathu?
14 Tyś jest Bóg, który czynisz cuda; podałeś do znajomości między narody moc twoję.
Inu ndinu Mulungu wochita zodabwitsa; Mumaonetsera mphamvu yanu pakati pa mitundu ya anthu.
15 Odkupiłeś ramieniem twojem lud swój, syny Jakóbowe i Józefowe. (Sela)
Ndi dzanja lanu lamphamvu munawombola anthu anu, zidzukulu za Yakobo ndi Yosefe. (Sela)
16 Widziały cię wody, o Boże! widziały cię wody, i ulękły się, i wzruszyły się przepaści.
Madzi anakuonani Mulungu, madzi anakuonani ndipo anachita mantha; nyanja yozama inakomoka.
17 Obłoki wydały powodzi; niebiosa wydały gromy, a strzały twoje tam i sam biegały.
Mitambo inakhuthula madzi ake pansi, mu mlengalenga munamveka mabingu; mivi yanu inawuluka uku ndi uku.
18 Huczało grzmienie twoje po obłokach, błyskawice oświeciły okrąg ziemi, ziemia się wzruszyła i zatrzęsła.
Bingu lanu linamveka mʼmphepo ya kamvuluvulu, mphenzi yanu inawalitsa dziko lonse; dziko lapansi linanjenjemera ndi kugwedezeka.
19 Przez morze była droga twoja, a ścieżki twoje przez wody wielkie, wszakże śladów twoich nie było.
Njira yanu inadutsa pa nyanja, njira yanu inadutsa pa madzi amphamvu, ngakhale zidindo za mapazi anu sizinaoneke.
20 Prowadziłeś lud twój, jako stado owiec, przez rękę Mojżesza i Aarona.
Inu munatsogolera anthu anu ngati gulu la nkhosa mwa dzanja la Mose ndi Aaroni.

< Psalmów 77 >