< Psalmów 76 >

1 Przedniejszemu śpiewakowi na Neginot, psalm i pieśń Asafowi. Znajomy jest Bóg w Judzkiej ziemi, w Izraelu wielkie imię jego.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Salimo la Asafu. Mulungu amadziwika mu Yuda; dzina lake ndi lotchuka mu Israeli.
2 W Salemie jest przybytek jego, a mieszkanie jego na Syonie.
Tenti yake ili mu Salemu, malo ake okhalamo mu Ziyoni.
3 Tamci połamał ogniste strzały łuków, tarczę, i miecz, i wojnę. (Sela)
Kumeneko Iye anathyola mivi yowuluka, zishango ndi malupanga, zida zankhondo. (Sela)
4 Zacnymeś się stał i dostojnym z gór łupiestwa.
Wolemekezeka ndinu, wamphamvu kuposa mapiri amene ali ndi nyama zambiri.
5 Ci, którzy byli serca mężnego, podani są na łup, zasnęli snem swoim, nie znaleźli mężni rycerze siły w rękach swych.
Anthu owuma mtima amagona atalandidwa chuma, Iwowo amagona tulo tawo totsiriza; palibe mmodzi wamphamvu amene angatukule manja ake.
6 Od gromienia twego, o Boże Jakóbowy! twardo zasnęły i wozy i konie.
Pa kudzudzula kwanu, Inu Mulungu wa Yakobo, kavalo pamodzi ndi galeta zimakhala chete zitagona pansi.
7 Tyś jest, ty bardzo straszliwy; i któż jest, coby się ostał przed obliczem twojem, gdy się zapali gniew twój?
Inu nokha ndiye muyenera kuopedwa. Angathe kuyima pamaso panu ndani mukakwiya?
8 Gdy z nieba dajesz słyszeć sąd swój, ziemia się lęka i ucicha;
Kuchokera kumwamba Inu munalengeza chiweruzo, ndipo dziko linaopa ndi kukhala chete,
9 Gdy Bóg na sąd powstaje, aby wybawił wszystkich pokornych na ziemi. (Sela)
pamene Inu Mulungu munadzuka kuti muweruze, kupulumutsa onse osautsidwa mʼdziko. (Sela)
10 Zaiste i gniew człowieczy chwalić cię musi, a ty ostatek zagniewania skrócisz.
Zoonadi, ukali wanu pa anthu umakubweretserani matamando ndipo opulumuka ku ukali wanu mumawasunga pafupi nanu.
11 Śluby czyńcie, a oddawajcie je Panu, Bogu waszemu, wszyscy, którzyście około niego, wszyscy przynoście dary strasznemu.
Chitani malumbiro kwa Yehova Mulungu wanu ndipo muwakwaniritse; anthu onse omuzungulira abweretse mphatso kwa Iye amene ayenera kuopedwa.
12 Onci odejmuje ducha książętom, a on jest na postrach królom ziemskim.
Iye amaswa mzimu wa olamulira; amaopedwa ndi mafumu a dziko lapansi.

< Psalmów 76 >