< Psalmów 75 >
1 Przedniejszemu śpiewakowi, jako: Nie zatracaj, psalm i pieśń Asafowa. Wysławiamy cię, Boże! wysławiamy: bo bliskie imię twoje; opowiadają to dziwne sprawy twoje.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe, potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Salimo la Asafu. Nyimbo. Tikuthokoza Inu Mulungu, tikuthokoza, pakuti dzina lanu lili pafupi nafe, anthutu amafotokoza za ntchito zanu zodabwitsa.
2 Gdy przyjdzie czas ułożony, ja sprawiedliwie sądzić będę.
Mumati, “Ine ndimayika nthawi yoyenera, ndine amene ndimaweruza mwachilungamo.
3 Rozstąpiła się ziemia, i wszyscy obywatele jej; ale ja utwierdzę słupy jej. (Sela)
Pamene dziko lapansi ndi anthu ake onse anjenjemera, ndine amene ndimagwiriziza mizati yake molimba. (Sela)
4 Rzekę szalonym: Nie szalejcie, a niepobożnym: Nie podnoście rogów.
Kwa odzitama ndikuti, ‘Musadzitamenso,’ ndipo kwa oyipa, ‘Musatukulenso nyanga zanu.
5 Nie podnoście przeciwko Najwyższemu rogów swych, a nie mówcie krnąbrnie,
Musatukule nyanga zanu motsutsana ndi kumwamba; musayankhule ndi khosi losololoka.’”
6 Bo nie od wschodu, ani od zachodu, ani od puszczy przychodzi wywyższenie.
Kugamula milandu sikuchokera kummawa kapena kumadzulo kapena ku chipululu.
7 Ale Bóg sędzia, tego poniża, a owego wywyższa.
Koma ndi Mulungu amene amaweruza: Iyeyo amatsitsa wina, nakwezanso wina.
8 Zaiste kielich jest w rękach Pańskich, a ten wina mętnego nalany; z tegoż nalewać będzie, tak, że i drożdże jego wyssą i wypiją wszyscy niepobożni ziemi.
Mʼdzanja la Yehova muli chikho chodzaza ndi vinyo wochita thovu, wosakanizidwa ndi zokometsera; Iye amamutsanulira pansi ndipo onse oyipa a dziko lapansi amamwa ndi senga zake zonse.
9 Ale ja będę opowiadał sprawy Pańskie na wieki, będę śpiewał Bogu Jakóbowemu.
Kunena za ine, ndidzalengeza izi kwamuyaya; ndidzayimba matamando kwa Mulungu wa Yakobo.
10 A wszystkie rogi niezbożnikom postrącam; ale rogi sprawiedliwego będą wywyższone.
Ndidzadula nyanga za onse oyipa koma nyanga za olungama zidzakwezedwa.