< Psalmów 73 >
1 Psalm Asafowy. Zaisteć dobry jest Bóg Izraelowi, tym, którzy są czystego serca.
Salimo la Asafu. Mulungu ndi wabwino ndithu kwa Israeli, kwa iwo amene ndi oyera mtima.
2 Ale nogi moje mało się były nie potknęły, a blisko tego było, że mało nie szwankowały kroki moje,
Koma kunena za ine, mapazi anga anali pafupi kuterereka; ndinatsala pangʼono kugwa.
3 Gdym był zawiścią poruszon przeciwko szalonym, widząc szczęście niepobożnych.
Pakuti ndinkachitira nsanje odzitamandira, pamene ndinaona mtendere wa anthu oyipa.
4 Bo nie mają związków aż do śmierci, ale w całości zostaje siła ich.
Iwo alibe zosautsa; matupi awo ndi athanzi ndi amphamvu.
5 W pracy ludzkiej nie są, a kaźni, jako inni ludzie, nie doznawają.
Saona mavuto monga anthu ena; sazunzika ngati anthu ena onse.
6 Przetoż otoczeni są pychą, jako łańcuchem złotym, a przyodziani okrutnością, jako szatą ozdobną.
Nʼchifukwa chake kunyada kuli monga mkanda wa mʼkhosi mwawo; amadziveka chiwawa.
7 Wystąpiły od tłustości oczy ich, a więcej mają nad pomyślenie serca.
Mʼmitima yawo yokhota mumachokera zolakwa; zoyipa zochokera mʼmaganizo awo sizidziwa malire.
8 Rozpuścili się, i mówią złośliwie, o uciśnieniu bardzo hardzie mówią.
Iwowo amanyogodola ndi kumayankhula zoyipa; mwa kudzikuza kwawo amaopseza ena nʼkumati, “Tikuponderezani.”
9 Wystawiają przeciwko niebu usta swe, a język ich krąży po ziemi.
Pakamwa pawo pamayankhula monyoza Mulungu kumwamba ndipo lilime lawo limayenda pa dziko lapansi.
10 A przetoż na to przychodzi lud jego, gdy się im wody już wierzchem leją,
Nʼchifukwa chake anthu awo amapita kwa iwowo ndi kumwa madzi mochuluka.
11 Że mówią: Jakoż ma Bóg o tem wiedzieć? albo mali o tem wiadomość Najwyższy?
Iwo amati, “Kodi Mulungu angadziwe bwanji? Kodi Wammwambamwamba angadziwe kalikonse?”
12 Albowiem, oto ci niezbożnymi będąc, mają pokój na świecie, i nabywają bogactw.
Umu ndi mmene oyipa alili; nthawi zonse ali pabwino ndipo chuma chawo chimachulukirachulukira.
13 Próżno tedy w czystości chowam ręce moje, a w niewinności serce moje omywam.
Ndithudi ine ndawusunga pachabe mtima wanga woyera; pachabe ndasamba mʼmanja mwanga mwa kusalakwa kwanga.
14 Ponieważ mię cały dzień biją, a karanie cierpię na każdy poranek.
Tsiku lonse ndapeza mavuto; ndakhala ndi kulangidwa mmawa uliwonse.
15 Rzekęli: Będę też tak o tem mówił, tedy rodzaj synów twoich rzecze, żem im niepraw.
Ndikanati, “Ndidzayankhula motere,” ndikanachita chosakhulupirika kwa ana anu.
16 Chciałemci tego rozumem doścignąć, ale mi się tu trudno zdało;
Pamene ndinayesa kuti ndimvetse zonsezi, zinandisautsa kwambiri
17 Ażem wszedł do świątnicy Bożej, a tum porozumiał dokończenie ich.
kufikira nditalowa mʼmalo opatulika a Mulungu; pamenepo ndinamvetsa mathero awo.
18 Zprawdęś ich na miejscach śliskich postawił, a podajesz ich na spustoszenie.
Zoonadi Inu munawayika pa malo woterera; Mumawagwetsa pansi kuti awonongeke.
19 Oto jakoć przychodzą na spustoszenie! niemal w okamgnieniu niszczeją i giną od strachu.
Mwamsangamsanga iwo amawonongedwa, amasesedwa kwathunthu ndi mantha!
20 Są jako sen temu, co ocucił; Panie! gdy ich obudzisz obraz ich lekce poważysz.
Monga loto pamene wina adzuka, kotero pamene Inu muuka, Inu Ambuye, mudzawanyoza ngati maloto chabe.
21 Gdy zgorzkło serce moje, a nerki moje cierpiały kłucie:
Pamene mtima wanga unasautsidwa ndi kuwawidwa mu mzimu mwanga,
22 Zgłupiałem był, a nicem nie rozumiał, byłem przed tobą jako bydlę.
ndinali wopusa ndi wosadziwa; ndinali chirombo chopanda nzeru pamaso panu.
23 A wszakże zawżdy byłem z tobą; boś mię trzymał za prawą rękę moję.
Komabe ineyo ndili ndi Inu nthawi zonse; mumandigwira dzanja langa lamanja.
24 Według rady swej prowadź mię, a potem do chwały przyjmiesz mię.
Inu mumanditsogolera ndi malangizo anu ndipo pambuyo pake mudzanditenga ku ulemerero.
25 Kogożbym innego miał na niebie? I na ziemi oprócz ciebie w nikim innym upodobania nie mam.
Kodi kumwamba ndili ndi yani kupatula Inu? Ndipo dziko lapansi lilibe chilichonse chimene ndimachilakalaka koposa Inuyo.
26 Choć ciało moje, i serce moje ustanie, jednak Bóg jest skałą serca mego, i działem moim na wieki.
Thupi ndi mtima wanga zitha kufowoka, koma Mulungu ndiye mphamvu ya mtima wanga ndi cholandira changa kwamuyaya.
27 Gdyż oto ci, którzy się oddalają od ciebie, zginą; wytracasz tych, którzy cudzołożą odstępowaniem od ciebie.
Iwo amene ali kutali ndi Inu adzawonongeka; Inu mumawononga onse osakhulupirika pamaso panu.
28 Aleć mnie najlepsza jest trzymać się Boga; przetoż pokładam w Panu panującym nadzieję moję, abym opowiadał wszystkie sprawy jego.
Koma kunena za Ine ndi kwabwino kukhala pafupi ndi Mulungu. Ndatsimikiza kuti Ambuye Yehova ndiwo pothawirapo panga ndipo ndidzalalika ntchito zanu zonse.