< Psalmów 71 >

1 W tobie, Panie! nadzieję mam: niech na wieki pohańbiony nie będę.
Mwa Inu Yehova ine ndathawiramo; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
2 Według sprawiedliwości twej wybaw mię, i wyrwij mię; nakłoń ku mnie ucha twego, i zachowaj mię.
Mundilanditse ndi kundipulumutsa mwa chilungamo chanu, mutchere khutu lanu ndi kundipulumutsa.
3 Bądź mi skałą mieszkania, gdziebym zawżdy uchodził; przykazałeś, aby mię strzeżono; boś ty skałą moją i twierdzą moją.
Mukhale thanthwe langa lothawirapo, kumene ine nditha kupita nthawi zonse; lamulani kuti ndipulumuke, pakuti Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa.
4 Boże mój! wyrwij mię z ręki niezbożnika, z ręki przewrotnego i gwałtownika;
Landitseni Inu Mulungu wanga, kuchoka mʼdzanja la oyipa, kuchoka mʼdzanja la oyipa ndi anthu ankhanza.
5 Albowiemeś ty oczekiwaniem mojem, Panie! Panie! nadziejo moja od młodości mojej.
Pakuti Inu mwakhala chiyembekezo changa, Inu Ambuye Wamphamvuzonse, chilimbikitso changa kuyambira ndili mwana.
6 Na tobiem spoległ zaraz z żywota; tyś mię wywiódł z żywota matki mojej; w tobie chwała moja zawżdy.
Kuyambira pamene ndinabadwa, ndakhala ndikudalira Inu; Inu munanditulutsa mʼmimba mwa amayi anga, ndipo ndidzakupembedzani nthawi zonse.
7 Jako dziwowisko byłem u wielu; wszakże tyś jest mocną nadzieją moją.
Ine ndakhala chinthu chodabwitsa kwa anthu ambiri koma Inu ndinu wonditchinjiriza wamphamvu.
8 Niechaj będą napełnione usta moje chwałą twoją, przez cały dzień sławą twoją.
Pakamwa panga padzaza ndi matamando anu, kulengeza ulemerero wanu tsiku lonse.
9 Nie odrzucajże mię w starości mojej; gdy ustanie siła moja, nie opuszczaj mię.
Musanditaye pamene ndakalamba; musandisiye pamene mphamvu zanga zatha.
10 Albowiem mówili nieprzyjaciele moi przeciwko mnie, a ci, którzy czyhali na duszę moję, radę uczynili społem,
Pakuti adani anga ayankhula motsutsana nane; iwo amene amadikira kuti andiphe amapangana pamodzi.
11 Mówiąc: Bóg go opuścił, gońcież go, a pojmijcie go; boć nie ma, ktoby go wyrwał.
Iwo amati, “Mulungu wamusiya; mutsatireni ndi kumugwira, pakuti palibe amene adzamupulumutse.”
12 Boże! nie oddalajże się odemnie; o Boże mój! pospieszże się na ratunek mój.
Musakhale kutali ndi ine Inu Mulungu, bwerani msanga, Inu Mulungu wanga; thandizeni.
13 Niechże będą zawstydzeni, niech zginą przeciwnicy duszy mojej; niech będą okryci zelżywością i wstydem, którzy mi szukają złego.
Ondineneza anga awonongeke mwa manyazi, iwo amene akufuna kundipweteka avale chitonzo ndi manyazi.
14 Aleć ja zawżdy oczekiwać będę, a tem więcej rozszerzę chwałę twoję.
Koma ine ndidzakhala ndi chiyembekezo mwa Inu nthawi zonse, ndidzakutamandani mowirikizawirikiza.
15 Usta moje opowiadać będą sprawiedliwość twoję, cały dzień zbawienie twoje, aczkolwiek liczby jego nie wiem.
Pakamwa panga padzafotokoza za chilungamo chanu, za chipulumutso chanu tsiku lonse, ngakhale sindikudziwa muyeso wake.
16 Przystąpię do wysławiania wszelakiej mocy Pana panującego, będę wspominał własną sprawiedliwość twoję.
Ndidzabwera ndi kulengeza za machitidwe amphamvu zanu Inu Ambuye Wamphamvuzonse. Ndidzalengeza chilungamo chanu, chanu chokha.
17 Boże! uczyłeś mię od młodości mojej, i opowiadam aż po dziś dzień dziwne sprawy twoje.
Kuyambira ubwana wanga, Inu Mulungu mwakhala mukundiphunzitsa, ndipo mpaka lero ine ndikulengeza za ntchito zanu zodabwitsa
18 A przetoż aż do starości i sędziwości nie opuszczaj mię, Boże! aż opowiem ramię twoje temu narodowi, i wszystkim potomkom moc twoję.
Ngakhale pamene ndakalamba ndipo imvi zili mbuu musanditaye Inu Mulungu, mpaka nditalengeza mphamvu zanu kwa mibado yonse yakutsogolo.
19 Bo sprawiedliwość twoja, Boże! wywyższona jest, czynisz zaiste rzeczy wielkie. Boże! któż jest podobien tobie?
Mphamvu zanu ndi kulungama kwanu zimafika mpaka kumwambamwamba. Ndani wofanana nanu Inu Mulungu, amene mwachita zazikulu?
20 Który, acześ przypuścił na mię wielkie i ciężkie uciski, wszakże zasię do żywota przywracasz mię, a z przepaści ziemskich zasię wywodzisz mię.
Ngakhale mwandionetsa mavuto ambiri owawa, mudzabwezeretsanso moyo wanga; kuchokera kunsi kwa dziko lapansi, mudzandiukitsanso.
21 Rozmnożysz dostojność moję a zasię ucieszysz mię.
Inu mudzachulukitsa ulemu wanga ndi kunditonthozanso.
22 A ja też wysławiać cię będę na instrumentach muzycznych, i prawdę twoję, Boże mój! będęć śpiewał przy harfie, o Święty Izraelski!
Ndidzakutamandani ndi zeze chifukwa cha kukhulupirika kwanu Mulungu, ndidzayimba matamando kwa Inu ndi pangwe, Inu Woyera wa Israeli.
23 Rozradują się wargi moje, gdyć będę śpiewał, i dusza moja, którąś wykupił.
Milomo yanga idzafuwula ndi chimwemwe pamene ndidzayimba matamando kwa Inu amene mwandiwombola.
24 Nadto i język mój będzie opowiadał przez cały dzień sprawiedliwość twoję; bo się zawstydzić, i hańbę odnieść musieli ci, którzy szukali nieszczęścia mego.
Lilime langa lidzafotokoza za ntchito zanu zachilungamo tsiku lonse, pakuti iwo amene amafuna kundipweteka achititsidwa manyazi ndi kusokonezedwa.

< Psalmów 71 >