< Psalmów 60 >

1 Przedniejszemu śpiewakowi na Sussanedut złota pieśń Dawidowa do nauczania; Gdy walczył przeciw Syryjczykom Nacharaim, i przeciw Syryjczykom Soby; gdy się wrócił Joab, poraziwszy Edomczyków w dolinie solnej dwanaście tysięcy. Boże! odrzuciłeś nas, rozproszyłeś nas, i rozgniewałeś się; nawróćże się zasię do nas.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Kakombo wa Pangano.” Mikitamu ya Davide yophunzitsira. Pamene anamenyana ndi Mesopotamiya ndi Aramu-Zoba, ndi pamene Yowabu anabwerera ndi kukantha Aedomu 12,000 mʼChigwa cha Mchere. Inu Mulungu mwatikanatu ife, ndipo mwatiwonongera otiteteza. Inu mwatikwiyira, tsopano tibwezeretseni mwakale!
2 Zatrząsnąłeś był ziemią, i rozsadziłeś ją; uleczże rozpadliny jej, boć się chwieje.
Inu mwagwedeza dziko ndipo mwalingʼamba, konzani mingʼalu yake pakuti ikugwedezeka kwambiri.
3 Okazywałeś ludowi twemu przykre rzeczy, napoiłeś nas winem zawrotu.
Inu mwaonetsa anthu anu nthawi za mavuto; inu mwatipatsa vinyo amene watichititsa kudzandira.
4 Ale teraz dałeś chorągiew tym, którzy się ciebie boją, aby ją wynieśli dla prawdy twej. (Sela)
Koma kwa iwo amene amaopa Inu, Inu mwakweza mbendera kuti tisonkhanireko pothawa uta.
5 Aby byli wybawieni umiłowani twoi; zachowajże ich prawicą twoją, a wysłuchaj mię.
Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja, kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.
6 Bóg ci mówił w świętobliwości swojej; przeto się rozweselę, rozdzielę Sychem, i dolinę Sukkotską pomierzę.
Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika: “Mwakupambana ndidzagawa Sekemu ndipo ndidzayeza malire a chigwa cha Sukoti.
7 Mojeć jest Galaad, mój i Manases, i Efraim moc głowy mojej; Juda zakonodawcą moim.
Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso; Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera, Yuda ndi ndodo yanga yaufumu
8 Moab miednicą do umywania mego; na Edoma wrzucę buty moje; ty, Palestyno! wykrzykaj nademną.
Mowabu ndi mbale yanga yosambira, pa Edomu ndidzaponyapo nsapato yanga, pa Filisitiya ndidzafuwula mwakupambana.”
9 Któż mię wprowadzi do miasta obronnego? kto mię przyprowadzi aż do Edom?
Adzandifikitse ndani ku mzinda wotetezedwa? Ndani adzanditsogolera ku Edomu?
10 Izali nie ty, o Boże! któryś nas był odrzucił, a nie wychodziłeś, Boże! z wojskami naszemi?
Kodi si Inu Mulungu, Inu amene mwatikana ife ndipo simutuluka pamodzi ndi magulu athu ankhondo.
11 Dajże nam ratunek w utrapieniu; boć omylny ratunek ludzki.
Tipatseni chithandizo kuti tilimbane ndi mdani wathu, pakuti thandizo lochokera kwa munthu ndi lopanda phindu.
12 W Bogu mężnie sobie poczynać będziemy, a on podepcze nieprzyjaciół naszych.
Chifukwa cha Mulungu, ife tidzapeza chipambano ndipo tidzapondaponda adani athu.

< Psalmów 60 >