< Psalmów 50 >

1 Psalm Asafowi podany. Bóg nad Bogami, Pan mówił i przyzwał ziemię od wschodu słońca aż do zachodu jego.
Salimo la Asafu. Wamphamvuyo, Yehova Mulungu, akuyankhula ndi kuyitanitsa dziko lapansi kuyambira kotulukira dzuwa mpaka kumene limalowera.
2 Objaśnił się Bóg z Syonu w doskonałej ozdobie.
Kuchokera ku Ziyoni, mokongola kwambiri Mulungu akuwala.
3 Przyjdzie Bóg nasz, a nie będzie milczał; ogień przed twarzą jego będzie pożerał, a około niego powstanie wicher gwałtowny.
Mulungu wathu akubwera ndipo sadzakhala chete; moto ukunyeketsa patsogolo pake, ndipo pomuzungulira pali mphepo yamkuntho
4 Przyzwie z góry niebiosa i ziemię, aby sądził lud swój.
Iye akuyitanitsa zamumlengalenga ndi za pa dziko lapansi kuti aweruze anthu ake.
5 Mówiąc: Zgromadźcie mi świętych moich, którzy ze mną uczynili przymierze przy ofierze.
Mundisonkhanitsire okhulupirika anga, amene anachita pangano ndi ine pochita nsembe.
6 Tedy niebiosa opowiedzą sprawiedliwość jego; albowiem sam Bóg jest sędzią. (Sela)
Ndipo mayiko akumwamba akulengeza chilungamo chake, pakuti Mulungu mwini ndi woweruza.
7 Słuchaj, ludu mój! a będę mówił; słuchaj, Izraelu! a oświadczę się przed tobą: Jam Bóg, Bóg twój Jam jest.
Imvani inu anthu anga, ndipo Ine ndidzayankhula, iwe Israeli, ndipo Ine ndidzayankhula mokutsutsa; ndine Mulungu, Mulungu wako.
8 Nie będę cię z ofiar twoich winił, ani całopalenia twego, które są zawsze przedemną.
Sindikudzudzula chifukwa cha nsembe zako, kapena nsembe zako zopsereza zimene zili pamaso panga nthawi zonse.
9 Nie wezmę z domu twojego cielca, ani z okołu twego kozłów.
Ine sindikufuna ngʼombe yayimuna kuchokera mʼkhola lako kapena mbuzi za mʼkhola lako,
10 Albowiem mój jest wszelki zwierz leśny, i tysiące bydła po górach.
pakuti nyama iliyonse yakunkhalango ndi yanga ndiponso ngʼombe za ku mapiri ochuluka.
11 Znam wszystko ptastwo po górach, i zwierz polny jest przedemną.
Ine ndimadziwa mbalame iliyonse mʼmapiri ndiponso zolengedwa zonse zakutchire ndi zanga.
12 Będęli łaknął, nie rzekęć o to; bo mój jest okrąg ziemi, i napełnienie jego.
Ndikanakhala ndi njala sindikanakuwuzani, pakuti dziko lonse ndi zonse zimene zili mʼmenemo ndi zanga.
13 Izali jadam mięso wołowe? albo pijam krew kozłową?
Kodi ndimadya nyama ya ngʼombe zazimuna kapena kumwa magazi a mbuzi?
14 Ofiaruj Bogu chwałę, i oddaj Najwyższemu śluby twoje;
“Pereka nsembe zachiyamiko kwa Mulungu, kwaniritsa malonjezo ako kwa Wammwambamwamba.
15 A wzywaj mię w dzień utrapienia: tedy cię wyrwę, a ty mię uwielbisz.
Ndipo undiyitane pa tsiku lako la masautso; Ine ndidzakulanditsa, ndipo udzandilemekeza.”
16 Lecz niezbożnemu rzekł Bóg: Cóżci do tego, że opowiadasz ustawy moje, a bieżesz przymierze moje w usta twoje?
Koma kwa woyipa, Mulungu akuti, “Kodi uli ndi mphamvu yanji kuti uzinena malamulo anga kapena kutenga pangano langa pa milomo yako?
17 Ponieważ masz w nienawiści karność, i zarzuciłeś słowa moje za się.
Iwe umadana ndi malangizo anga ndipo umaponyera kumbuyo kwako mawu anga.
18 Widziszli złodzieja, bieżysz z nim, a z cudzołożnikami masz skład twój.
Ukaona wakuba umamutsatira, umachita maere ako pamodzi ndi achigololo
19 Usta twoje rozpuszczasz na złe, a język twój składa zdrady.
Umagwiritsa ntchito pakamwa pako pa zinthu zoyipa ndipo umakonza lilime lako kuchita chinyengo.
20 Zasiadłszy mówisz przeciwko bratu twemu, a lżysz syna matki twojej.
Nthawi zonse umayankhula motsutsana ndi mʼbale wako ndipo umasinjirira mwana wa amayi ako enieni.
21 Toś czynił, a Jam milczał; dlategoś mniemał, żem ja tobie podobny, ale będę cię karał, i stawięć to przed oczy twoje.
Wachita zimenezi ndipo Ine ndinali chete; umaganiza kuti ndine wofanana nawe koma ndidzakudzudzula ndipo ndidzakutsutsa pamaso pako.
22 Zrozumiejcież to wżdy teraz, którzy zapominacie Boga, bym was snać nie porwał, a nie będzie ktoby was wyrwał.
“Ganizira izi, iwe amene umayiwala Mulungu kuti ndingakukadzule popanda wokupulumutsa:
23 Kto mi ofiaruje chwałę, uczci mię; a temu, który naprawia drogę swą, ukażę zbawienie Boże.
Iye amene amapereka nsembe yamayamiko amandilemekeza, ndipo amakonza njira zake kuti ndimuonetse chipulumutso cha Mulungu.”

< Psalmów 50 >