< Psalmów 43 >

1 Sądź mię, o Boże! a ujmij się o sprawę moję; od narodu niemiłosiernego, i od człowieka zdradliwego i niezbożnego wyrwij mię;
Onetsani kusalakwa kwanga Inu Mulungu; ndipo mundinenere mlandu wanga kutsutsana ndi mtundu wosapembedza; mundilanditse mʼmanja mwa achinyengo ndi anthu oyipa.
2 Boś ty jest Bóg siły mojej. Przeczżeś mię odrzucił? a przecz smutno chodzę dla uciśnienia od nieprzyjaciela?
Pajatu Inu Mulungu ndinu mphamvu zanga. Nʼchifukwa chiyani mwandikana ine? Nʼchifukwa chiyani ndiyenera kuyenda ndikulira, woponderezedwa ndi mdani?
3 Ześlij światłość twoję, i prawdę twoję; te mię poprowadzą, i wprowadzą mię na świętą górę twoję, i do przybytków twoich,
Tumizani kuwunika kwanu ndi choonadi chanu kuti zinditsogolere; mulole kuti zindifikitse ku phiri lanu loyera, kumalo kumene inu mumakhala.
4 Abym przystąpił do ołtarza Bożego, do Boga wesela i radości mojej; i będę cię wysławiał na harfie, o Boże, Boże mój!
Ndipo ndidzapita ku guwa lansembe la Mulungu, kwa Mulungu, chimwemwe changa ndi chikondwerero changa. Ndidzakutamandani ndi zeze, Inu Mulungu wanga.
5 Przeczże się smucisz, duszo moja, a przecz trwożysz sobą we mnie? Czekaj na Boga, albowiem go jeszcze będę wysławiał, gdyż on jest wielkiem zbawieniem twarzy mojej, i Bogiem moim.
Nʼchifukwa chiyani uli ndi chisoni iwe moyo wanga? Nʼchifukwa chiyani wakhumudwa iwe mʼkati mwanga? Khulupirira Mulungu, pakuti ndidzamutamandabe Iye, Mpulumutsi wanga ndi Mulungu wanga.

< Psalmów 43 >