< Psalmów 39 >

1 Przedniejszemu śpiewakowi Jedytunowi psalm Dawidowy. Rzekłem: Będę strzegł dróg moich, abym nie zgrzeszył językiem swym; włożę munsztuk w usta moje, póki niepobożny będzie przedemną.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Kwa Yedutuni. Salimo la Davide. Ndinati, “Ndidzasamalira njira zanga ndipo ndidzasunga lilime langa kuti ndisachimwe; ndidzatseka pakamwa panga ndi chitsekerero nthawi yonse imene woyipa ali pamaso panga.”
2 Zaniemiałem milcząc; zamilknąłem i w dobrej sprawie; ale boleść moja bardziej się wzmagała.
Koma pamene ndinali chete osanena ngakhale kanthu kalikonse kabwino mavuto anga anachulukirabe.
3 Rozpaliło się serce moje we wnętrznościach moich; w rozmyślaniu mojem rozżarzył się ogień, ażem tak rzekł językiem swoim:
Mtima wanga unatentha mʼkati mwanga, ndipo pamene ndinkalingalira, moto unayaka; kenaka ndinayankhula ndi lilime langa:
4 Daj mi poznać, Panie! dokończenie moje, i wymiar dni moich jaki jest, abym wiedział, jak długo trwać będę.
“Yehova ndionetseni mathero a moyo wanga ndi chiwerengero cha masiku anga; mundidziwitse kuti moyo wanga ndi wosakhalitsa motani.
5 Otoś na dłoni wymierzył dni moje, a wiek mój jest jako nic przed tobą; zaprawdę szczerą marnością jest wszelki człowiek, choć najduższy. (Sela)
Inu mwachititsa kuti masiku anga akhale ochepa kwambiri, kutalika kwa zaka zanga ndi kopanda phindu pamaso panu; moyo wa munthu aliyense ndi waufupi. (Sela)
6 Zaprawdę pomija człowiek jako cień; zaprawdę próżno się kłopocze, zgromadza, a nie wie, kto to pobierze.
Munthu ali ngati chithunzithunzi chake pamene akuyenda uku ndi uku: Iye amangovutika koma popanda phindu; amadzikundikira chuma, osadziwa kuti chidzakhala chayani.
7 A teraz na cóż oczekuję, Panie? Tyś jest sam oczekiwaniem mojem.
“Koma tsopano Ambuye kodi ndifunanso chiyani? Chiyembekezo changa chili mwa Inu.
8 Przetoż od wszystkich przestępstw moich wybaw mię; na pośmiech głupiemu nie dawaj mię.
Pulumutseni ku zolakwa zanga zonse; musandisandutse chonyozeka kwa opusa.
9 Zaniemiałem, i nie otworzyłem ust moich, przeto, żeś to ty uczynił.
Ine ndinali chete; sindinatsekule pakamwa panga pakuti Inu ndinu amene mwachita zimenezi.
10 Odejmij odemnie karanie twoje; bom od smagania ręki twojej ustał.
Chotsani mkwapulo wanu pa ine; ndagonjetsedwa ndi nkhonya ya dzanja lanu.
11 Gdy ty gromiąc karzesz człowieka dla nieprawości, wnet niszczysz jako mól grzeczność jego; zaisteć marnością jest wszelki człowiek. (Sela)
Inu mumadzudzula ndi kulanga anthu chifukwa cha tchimo lawo; mumawononga chuma chawo monga njenjete; munthu aliyense ali ngati mpweya. (Sela)
12 Wysłuchajże modlitwę moję, Panie! a wołanie moje przyjmij w uszy swoje, nie milcz na łzy moje; bomci ja przychodniem u ciebie, i komornikiem, jako wszyscy ojcowie moi.
“Imvani pemphero langa Inu Yehova, mverani kulira kwanga kopempha thandizo; musakhale chete pamene ndikulirira kwa Inu, popeza ndine mlendo wanu wosakhalitsa; monga anachitira makolo anga onse.
13 Sfolguj mi, abym się posilił, pierwej niżeli odejdę, a nie będzie mię.
Musandiyangʼane mwaukali, choncho ndidzatha kusangalala ndisanafe ndi kuyiwalika.”

< Psalmów 39 >