< Psalmów 35 >

1 Psalm Dawidowy. Rozpieraj się, Panie! z tymi, którzy się ze mną spierają; a walcz przeciwko tym, którzy walczą przeciwko mnie.
Salimo la Davide. Inu Yehova, mulimbane nawo amene akulimbana nane; mumenyane nawo amene akumenyana nane.
2 Porwij pukierz i tarczę, a powstań na ratunek mój.
Tengani chishango ndi lihawo; dzukani ndipo bwerani mundithandize.
3 Dobądź włóczni, a staw się na drodze przeciwko tym, którzy mię prześladują. Rzeczże duszy mojej: Jam jest zbawieniem twojem.
Tengani mkondo ndi nthungo, kulimbana ndi iwo amene akundithamangitsa. Uzani moyo wanga kuti, “Ine ndine chipulumutso chako.”
4 Niech będą pohańbieni i zawstydzeni, którzy szukają duszy mojej; niech tył podadzą, i niech będą zawstydzeni, którzy mi źle myślą.
Iwo amene akufunafuna moyo wanga anyozedwe ndi kuchita manyazi; iwo amene akukonza kuti moyo wanga uwonongeke abwerere mʼmbuyo mochititsa mantha.
5 Niech będą jako plewy przed wiatrem, a Anioł Pański niechaj ich rozproszy.
Akhale ngati mankhusu owuluka ndi mphepo pamene mngelo wa Yehova akuwapirikitsa.
6 Niech będzie droga ich ciemna i śliska, Anioł Pański niech ich goni.
Njira yawo ikhale ya mdima ndi yoterera pamene mngelo wa Yehova akuwathamangitsa.
7 Albowiem bez przyczyny zastawili na mię w dole sieci swoje, i bez przyczyny ukopali dół duszy mojej.
Popeza ananditchera ukonde popanda chifukwa ndipo popanda chifukwa andikumbira dzenje,
8 Niechaj na nich przyjdzie spustoszenie, którego się nie spodziewali; a sieć ich, którą zastawili, niech ich ułowi na zginienie, a niech w nią wpadną.
chiwonongeko chiwapeza modzidzimutsa ukonde umene iwo abisa uwakole, agwere mʼdzenje kuti awonongedwe.
9 Ale dusza moja niech się rozraduje w Panu, niech się rozweseli w zbawieniu jego.
Pamenepo moyo wanga udzakondwera mwa Yehova ndi kusangalala ndi chipulumutso chake.
10 Tedy wszystkie kości moje rzeką: Panie! któż podobny tobie? który wyrywasz utrapionego od mocniejszego nadeń, a nędznego i ubogiego od drapieżcy jego.
Thupi langa lidzafuwula mokondwera, “Ndani angafanane nanu Yehova? Mumalanditsa osauka kwa amene ali ndi mphamvu zambiri, osauka ndi osowa kwa iwo amene amawalanda.”
11 Powstawają świadkowie fałszywi, a o czem nie wiem, pytają mię.
Mboni zopanda chisoni zinayimirira, zinandifunsa zinthu zimene sindikuzidziwa.
12 Oddawają mi złem za dobre, chcąc mię pozbawić duszy mojej,
Iwo anandibwezera zoyipa pa zabwino ndipo anasiya moyo wanga pa chisoni.
13 Chociażem się ja w wór obłóczył, gdy oni chorowali; trapiłem postem duszę moję, i modliłem się często sam u siebie za nimi.
Koma pamene iwo ankadwala, ine ndinavala chiguduli ndi kudzichepetsa ndekha posala zakudya. Pamene mapemphero anga anabwerera kwa ine osayankhidwa,
14 Jako do przyjaciela, jako do brata mego, ustawiczniem chadzał; poniżałem się jako ten, który się smuci, chodząc po matce w żałobie.
ndinayendayenda ndi kulira maliro, kumulira ngati bwenzi langa kapena mʼbale wanga. Ndinaweramitsa mutu wanga mosweka mtima kukhala ngati ndikulira amayi anga.
15 Lecz oni, gdym ja chorował, weselili się, i zbierali się; zbierali się przeciwko mnie, jakoby byli dla mnie utrapieni, czegom ja nie spostrzegł; szczypali mię, a nie milczeli.
Koma pamene ndinaphunthwa, iwo anasonkhana mosangalala; ondithira nkhondo anasonkhana kutsutsana nane, ineyo osadziwa. Iwo sanasiye kundiyankhulira mawu onyoza.
16 Z obłudnikami, z naśmiewcami, z pochlebcami zgrzytali na mię zębami swemi.
Monga anthu osapembedza, iwo anandinyoza mwachipongwe; anandikukutira mano awo.
17 Panie! długoż na to patrzeć będziesz? wyrwijże duszę moję od zguby ich, od lwiąt jedynaczkę moję.
Ambuye, mpaka liti mudzakhala mukungoyangʼana? Landitsani moyo wanga ku chiwonongeko chawo, moyo wanga wopambana ku mikango.
18 Będę cię wysławiał w zgromadzeniu wielkiem; między ludem wielkim będę cię chwalił.
Ndidzakuyamikani mu msonkhano waukulu; pakati pa gulu lalikulu la anthu ndidzakutamandani.
19 Niech się nie weselą ze mnie, którzy mi są nieprzyjaciółmi bez przyczyny; którzy mię mają w nienawiści niesłusznie, niech nie mrugają okiem.
Musalole adani anga onyenga akondwere chifukwa cha masautso anga; musalole kuti amene amadana nane popanda chifukwa andiyangʼane chamʼmbali mondinyoza.
20 Albowiem nie mówią o pokoju; ale przeciwko spokojnym na ziemi zdradliwe słowa zmyślają.
Iwowo sayankhula mwamtendere, koma amaganizira zonamizira iwo amene amakhala mwabata mʼdziko.
21 Owszem, rozdzierają na mię gębę swą, mówiąc: Ehej! ehej! widzić to oko nasze.
Iwo amandiseka mofuwula ndipo amati, “Haa! Haa! Ndipo ndi maso athuwa ife taziona.”
22 Widzisz to, Panie! nie milczże Panie! nie oddalaj się odemnie.
Yehova mwaona zimenezi; musakhale chete. Ambuye musakhale kutali ndi ine.
23 Obudźże się, a ocuć dla sądu mego, Boże mój i Panie mój! dla sprawy mojej.
Dzukani, ndipo nyamukani kunditeteza! Mulimbane nawo chifukwa cha ine, Mulungu wanga ndi Ambuye anga.
24 Sądź mnie według sprawiedliwości twojej, Panie Boże mój! a niech się nie weselą nademną.
Onetsani kusalakwa kwanga mwa chilungamo chanu, Inu Yehova Mulungu wanga. Musalole kuti akondwere chifukwa cha mavuto anga.
25 Niech nie mówią w sercu swojem: Ehej, duszo masza! niech nie mówią: Pożarliśmy go.
Musalole kuti aganize kuti, “Amati atani, zachitika monga momwe timafunira!” Kapena kunena kuti, “Tamutha ameneyu basi.”
26 Niechajże będą pohańbieni, i zawstydzeni wszyscy weselący się ze złego mego; niech będą obleczeni w hańbę, i w sromotę, którzy się chlubią przeciwko mnie.
Onse amene amakondwera ndi masautso anga achite manyazi ndi kusokonezeka. Onse amene amadzikweza kufuna kundipambana, avekedwe manyazi ndi mnyozo ngati zovala.
27 Ale ci, którzy się kochają w sprawiedliwości mojej, niech śpiewają i radują się, a niech mówią ustawicznie: Niech będzie uwielbiony Pan, który życzy pokoju słudze swemu.
Koma amene amakondwera chifukwa chakuti ndine wosalakwa, afuwule mwachimwemwe ndi chisangalalo. Nthawi zonse azinena kuti, “Yehova akwezeke, Iye amene amakondwera ndi kupeza bwino kwa mtumiki wake.”
28 A język mój będzie opowiadał sprawiedliwość twoję, i na każdy dzień chwałę twoję.
Pakamwa panga padzayankhula za chilungamo chanu ndi za matamando anu tsiku lonse.

< Psalmów 35 >