< Psalmów 30 >
1 Psalm pieśni przy poświęceniu domu Dwidowego. Panie! wywyższać cię będę; albowiem wywyższyłeś mię, a nie dałeś pociechy nieprzyjaciołom moim ze mnie.
Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba popereka Nyumba ya Mulungu. Ndidzakukwezani Yehova, chifukwa mwanditulutsa kwakuya, ndipo simunalole kuti adani anga akondwere pa ine.
2 Panie, Boże mój! wołałem do ciebie, a uzdrowiłeś mię.
Inu Yehova Mulungu wanga ndinapempha kwa Inu thandizo ndipo Inu munandichiritsa.
3 Panie! wywiodłeś z piekła duszę moję; zachowałeś mię przy żywocie, abym nie zstąpił do grobu. (Sheol )
Inu Yehova, munanditulutsa ku manda, munandisunga kuti ndisatsalire mʼdzenje. (Sheol )
4 Śpiewajcież Panu święci jego, a wysłuchajcie pamiątkę świętobliwości jego.
Imbirani Yehova inu anthu ake okhulupirika; tamandani dzina lake loyera.
5 Albowiem prędko przemija gniew jego, ale po wszystek żywot trwa dobra wola jego; z wieczora bywa płacz, ale z poranku wesele.
Pakuti mkwiyo wake umakhala kwa kanthawi koma kukoma mtima kwake ndi kwa moyo wonse; utha kuchezera kulira usiku wonse, koma chimwemwe chimabwera mmawa.
6 Rzekłem w szczęściu swojem: Nie będę poruszony na wieki.
Pamene ndinaona kuti ndili otetezedwa ndinati, “Sindidzagwedezekanso.”
7 Albowiem ty, Panie! według woli twojej umocniłeś był górę moję mocą; ale skoroś ukrył oblicze swoje, strwożyłem się;
Inu Yehova, pamene munandikomera mtima, munachititsa phiri langa kuyima chilili; koma pamene munabisa nkhope yanu, ndinataya mtima.
8 I wołałem do ciebie, Panie! a Panum się modlił, mówiąc:
Kwa Inu Yehova ndinayitana; kwa Ambuye ndinapempha chifundo;
9 Co za pożytek ze krwi mojej, gdybym zstąpił do dołu? Izali cię proch chwalić będzie? Iazali opowie prawdę twoję?
“Kodi pali phindu lanji powonongeka kwanga ngati nditsikira ku dzenje? Kodi fumbi lidzakutamandani Inu? Kodi lidzalengeza za kukhulupirika kwanu?
10 Wysłuchajże, Panie! a zmiłuj się nademną; Panie! bądź pomocnikiem moim.
Imvani Yehova ndipo mundichitire chifundo; Yehova mukhale thandizo langa.”
11 Tedyś odmienił płacz mój w pląsanie; zdjąłeś ze mnie wór mój, a przepasałeś mię radością.
Inu munasandutsa kulira kwanga kukhala kuvina; munachotsa chiguduli changa ndi kundiveka ndi chimwemwe,
12 Przetoż tobie śpiewać będzie chwała moja, a milczeć nie będzie. Panie, Boże mój! na wieki wysławiać cię będę.
kuti mtima wanga uthe kuyimbira Inu usakhale chete. Yehova Mulungu wanga, ndidzapereka kwa Inu mayamiko kwamuyaya.