< Psalmów 24 >

1 Psalm Dawidowy. Pańska jest ziemia, i napełnienie jej, okrąg ziemi, i którzy mieszkają na nim.
Salimo la Davide. Dziko lapansi ndi la Yehova ndi zonse zimene zili mʼmenemo, dziko ndi onse amene amakhala mʼmenemo;
2 Bo on na morzu ugruntował ją, a na rzekach utwierdził ją.
pakuti Iye ndiye anayika maziko ake pa nyanja ndi kulikhazika pamwamba pa madzi.
3 Któż wstąpi na górę Pańską? a kto stanie na miejscu świętem jego?
Ndani angakwere phiri la Yehova? Ndani angathe kuyima pa malo ake opatulika?
4 Człowiek niewinnych rąk i czystego serca, który nie skłania ku marności duszy swej, a nie przysięga zdradliwie.
Iye amene ali ndi mʼmanja moyera ndi mtima woyera, amene sapereka moyo wake kwa fano kapena kulumbira mwachinyengo.
5 Ten weźmie błogosławieństwo od Pana, i sprawiedliwość od Boga zbawiciela swego.
Iyeyo adzalandira madalitso kwa Yehova ndipo Mulungu mpulumutsi wake adzagamula kuti alibe mlandu.
6 Tenci jest naród szukających go, szukających oblicza twego, Boże Jakóbowy! (Sela)
Umenewo ndiwo mʼbado wa amene amafunafuna Yehova; amene amafunafuna nkhope yanu, Inu Mulungu wa Yakobo. (Sela)
7 Podnieścież, o bramy! wierzchy wasze; podnieście się, wy bramy wieczne! aby wszedł król chwały!
Tukulani mitu yanu inu zipata; tsekukani, inu zitseko zakalekalenu, kuti Mfumu yaulemerero ilowe.
8 Któryż to jest król chwały? Pan mocny i możny, Pan mocny w boju.
Kodi Mfumu yaulemereroyo ndani? Yehova Wamphamvuzonse, Yehova ndiye wamphamvu pa nkhondo.
9 Podnieścież, o bramy! wierzchy wasze; podnieście się, wy bramy wieczne! aby wszedł król chwały.
Tukulani mitu yanu, inu zipata; tsekukani, inu zitseko zakalekalenu, kuti Mfumu yaulemerero ilowe.
10 Który to jest król chwały? Pan zastępów, tenci jest król chwały. (Sela)
Kodi Mfumu yaulemereroyo ndani? Yehova Wamphamvuzonse, Iye ndiye Mfumu yaulemerero. (Sela)

< Psalmów 24 >