< Psalmów 20 >

1 Przedniejszemu śpiewakowi psalm Dawidowy. Niech cię Pan wysłucha w dzień utrapienia; niech cię wywyższy imię Boga Jakóbowego.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Yehova akuyankhe pamene uli pa msautso; dzina la Mulungu wa Yakobo likuteteze.
2 Niech ci ześle ratunek z świątnicy, a z Syonu niech cię podeprze.
Iye atumize thandizo kuchokera ku malo ake opatulika; akugwirizize kuchokera ku Ziyoni.
3 Niech wspomni na wszystkie ofiary twoje, a całopalenia twoje niech w popiół obróci. (Sela)
Iye akumbukire nsembe zako zonse ndipo alandire nsembe zako zopsereza. (Sela)
4 Niech ci da wszystko według serca twego, a wszelką radę twoję niech wypełni.
Akupatse chokhumba cha mtima wako ndipo akuthandize kuti zonse wakonza zichitike.
5 Rozweselimy się w wybawieniu twojem, a w imieniu Boga naszego chorągiew podniesiemy; niech wypełni Pan wszystkie prośby twoje.
Ife tidzafuwula ndi chimwemwe pamene iwe wapambana ndipo tidzanyamula mbendera zathu mʼdzina la Mulungu wathu, Yehova ayankhe zopempha zako zonse.
6 Teraześmy poznali, iż Pan wybawił pomazańca swego, a iż go wysłuchał z nieba swego świętego przez zbawienną moc prawicy swojej.
Tsopano ndadziwa kuti Yehova amapulumutsa wodzozedwa wake; Iye amamuyankha kuchokera kumwamba ku malo ake opatulika ndi mphamvu yopulumutsa ya dzanja lake lamanja.
7 Jedni w wozach, a drudzy w koniach ufają; ale my na imię Pana, Boga naszego, wspominamy.
Ena amadalira magaleta ndipo ena akavalo koma ife tidzadalira dzina la Yehova Mulungu wathu.
8 Onić polegli i upadli, a myśmy powstali, i ostoimy się.
Iwo amagonjetsedwa ndi kugwa, koma ife timadzuka ndi kuyima chilili.
9 Panie! ty nas zachowaj, a król nas niech wysłucha w dzień wołania naszego.
Inu Yehova, pulumutsani mfumu! Tiyankheni pamene tikuyitanani!

< Psalmów 20 >