< Psalmów 2 >

1 Przeczże się poganie buntują, a narody przemyślają próżne rzeczy?
Nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina akufuna kuchita chiwembu? Akonzekeranji zopanda pake anthu?
2 Schodzą się królowie ziemscy, a książęta radzą społem przeciwko Panu, i przeciw pomazańcowi jego, mówiąc:
Mafumu a dziko lapansi akugwirizana nazo; ndipo olamulira asonkhana pamodzi kulimbana ndi Ambuye ndi wodzozedwa wakeyo.
3 Potargajmy związki ich, a odrzućmy od siebie powrozy ich.
Iwo akunena kuti, “Tiyeni timasule magoli awo ndipo titaye zingwe zawo.”
4 Ale ten, który mieszka w niebie, śmieje się; Pan szydzi z nich.
Wokhala mmwamba akuseka; Ambuye akuwanyoza iwowo.
5 Tedy będzie mówił do nich w popędliwości swojej, a w gniewie swoim przestraszy ich,
Ndipo iye awadzudzula mu mkwiyo wake ndi kuwaopseza mu ukali wake, kunena kuti,
6 Mówiąc: Jamci postanowił króla mojego nad Syonem, górą świętą moją.
“Ine ndakhazikitsa mfumu yanga pa Ziyoni, phiri langa loyera.”
7 Opowiem ten dekret: Pan rzekł do mnie: Syn mój jesteś ty, Jam ciebie dziś spłodził.
Ine ndidzalengeza zimene Yehova walamula: Iye anati kwa Ine, “Iwe ndiwe mwana wanga; lero Ine ndakhala Atate ako.
8 Żądaj odemnie, a dam ci narody dziedzictwo twoje; a osiadłość twoję, granice ziemi.
Tandipempha, ndipo ndidzachititsa kuti mitundu ya anthu ikhale cholowa chako; malekezero a dziko lapansi kuti akhale chuma chako.
9 Potrzesz ich laską żelazną, a jako naczynie zduńskie pokruszysz ich.
Iweyo udzawalamulira ndi ndodo yaufumu yachitsulo; udzawaphwanya zidutswazidutswa ngati zowumba zadothi.”
10 Terazże tedy zrozumiejcie, królowie, nauczcie się sędziowie ziemi!
Kotero, inu mafumu, chenjerani; chenjezedwani, inu olamulira a dziko lapansi.
11 Służcie Panu w bojaźni, a rozradujcie się ze drżeniem.
Tumikirani Yehova mwa mantha ndi kukondwerera ulamuliro wake monjenjemera.
12 Pocałujcie syna, by się snać nie rozgniewał, i zginęlibyście w drodze, gdyby się najmniej zapaliła popędliwość jego. Błogosławieni wszyscy, którzy w nim ufają.
Mpsopsoneni mwanayo kuti angakwiye; kuti mungawonongedwe mʼnjira zanu, pakuti ukali wake utha kuuka mʼkanthawi kochepa. Odala ndi onse amene amathawira kwa Iye.

< Psalmów 2 >