< Psalmów 137 >

1 Nad rzekami Babilońskiemi, tameśmy siadali i płakali, wspominając na Syon.
Mʼmbali mwa mitsinje ya ku Babuloni tinakhala pansi ndi kulira pamene tinakumbukira Ziyoni.
2 Na wierzbach, które są w nim, zawieszaliśmy harfy nasze.
Kumeneko, pa mitengo ya misondozi tinapachika apangwe athu,
3 A gdy nas tam pytali ci, którzy nas zawiedli w niewolę, o słowa pieśni, ( chociażeśmy byli zawiesili pieśni radości, ) mówiąc: Śpiewajcie nam pieśń z pieśni Syońskich,
pakuti anthu otigwira ukapolo anatipempha kuti tiyimbe nyimbo. Otizunza athu anafuna nyimbo zachisangalalo; iwo anati, “Tiyimbireni imodzi mwa nyimbo za ku Ziyoni!”
4 Odpowiedzieliśmy: Jakoż mamy śpiewać pieśń Pańską w ziemi cudzoziemców?
Tingayimbe bwanji nyimbo za Yehova mʼdziko lachilendo?
5 Jeźliże cię zapomnę, o Jeruzalemie! niech zapomni sama siebie prawica moja.
Ndikakuyiwala iwe Yerusalemu, dzanja langa lamanja liyiwale luso lake.
6 Niech przylgnie język mój do podniebienia mego, jeźlibym na cię nie pomniał, jeźlibym nie przełożył Jeruzalemu nad najwiekszę wesele moje.
Lilime langa limamatire ku nkhama za mʼkamwa mwanga ndikapanda kukukumbukira iwe Yerusalemu, ngati sindiyesa iwe chimwemwe changa chachikulu.
7 Wspomnij, Panie! na synów Edomskich, i na dzień Jeruzalemski, w który mówili: Poburzcie, poburzcie aż do gruntu w nim.
Kumbukirani, Inu Yehova, zimene Aedomu anachita pa tsiku limene Yerusalemu anagonja. Iwowo anafuwula kuti, “Mugwetseni pansi, mugwetseni pansi mpaka pa maziko ake!”
8 O córko Babilońska! i ty będziesz spustoszona. Błogosławiony, któryć odda nagrodę twoję, za to, coś nam złego uczyniła.
Iwe mwana wa mkazi wa Babuloni, woyenera kuwonongedwa, wodalitsika ndi yemwe adzakubwezera pa zimene watichitira.
9 Błogosławiony, który pochwyci i roztrąci dziatki twe o skałę.
Amene adzagwira makanda ako ndi kuwakankhanthitsa pa miyala.

< Psalmów 137 >