< Psalmów 125 >

1 Pieśń stopni. Którzy ufają w Panu, są jako góra Syon, która się nie poruszy, ale na wieki zostaje.
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Amene amadalira Yehova ali ngati phiri la Ziyoni, limene silingagwedezeke koma ndi lokhala mpaka muyaya.
2 Jako około Jeruzalemu są góry, tak Pan jest około ludu swego, od tego czasu aż i na wieki.
Monga mapiri azungulira Yerusalemu, momwemonso Yehova azungulira anthu ake kuyambira tsopano mpaka muyaya.
3 Albowiem nie zostanie laska niezbożników nad losem sprawiedliwych, by snać nie ściągnęli sprawiedliwi rąk swych ku nieprawości.
Ndodo yaufumu ya anthu oyipa sidzakhala pa dziko limene lapatsidwa kwa anthu olungama, kuti anthu olungamawo angachite nawonso zoyipa.
4 Dobrze czyń, Panie! dobrym, i tym, którzy są uprzejmego serca.
Yehova chitirani zabwino amene ndi abwino, amene ndi olungama mtima
5 Ale tych, którzy się udawają krzyewemi drogami swemi, niech zapędzi Pan z tymi, którzy czynią nieprawość; lecz pokój niech będzie nad Izraelem.
Koma amene amatembenukira ku njira zokhotakhota, Yehova adzawachotsa pamodzi ndi anthu ochita zoyipa. Mtendere ukhale pa Israeli.

< Psalmów 125 >