< Psalmów 122 >

1 Pieśń stopni Dawidowa. Weselę się z tego, że mi powiedziano: Do domu Pańskiego pójdziemy.
Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndinakondwera atandiwuza kuti, “Tiyeni ku nyumba ya Yehova.”
2 Że stanęły nogi nasze w bramach twoich, o Jeruzalemie!
Mapazi athu akuyima mʼzipata zako, Iwe Yerusalemu.
3 O Jeruzalem pięknie pobudowane jako miasto w sobie wespół spojone!
Yerusalemu anamangidwa ngati mzinda umene uli wothithikana pamodzi.
4 Bo tam wstępują pokolenia, pokolenia Pańskie, do świadectwa Izraelowego, aby wysławiały imię Pańskie.
Kumeneko ndiye kumene kumapita mafuko, mafuko a Yehova, umboni wa kwa Israeli, kuti atamande dzina la Yehova.
5 Albowiem tam są postawione stolice na sąd, stolice domu Dawidowego.
Kumeneko anayikako mipando yaufumu yachiweruzo, mipando yaufumu ya nyumba ya Davide.
6 Żądajcież pokoju Jeruzalemowi, mówiąc: Niech się szczęści tym, którzy cię miłują.
Pemphererani mtendere wa Yerusalemu: “Iwo amene amakukonda iwe zinthu ziwayendere bwino.
7 Niech będzie pokój w basztach twoich, a uspokojenie w pałacach twoich.
Mukhale mtendere mʼkati mwa makoma ako, ndipo mʼnyumba zako zaufumu mukhale chitetezo.”
8 Dla braci moich i dla przyjaciół moich teraz ci będę żądał pokoju.
Chifukwa cha abale anga ndi abwenzi anga ndidzati, “Mtendere ukhale mʼkati mwako.”
9 Dla domu Pana, Boga naszego, będę szukał twego dobrego.
Chifukwa cha Nyumba ya Yehova Mulungu wathu, ndidzakufunira zabwino.

< Psalmów 122 >