< Psalmów 119 >

1 Błogosławieni, którzy żyją bez nagany, którzy chodzą w zakonie Pańskim,
Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa, amene amayenda monga mwa malamulo a Yehova.
2 Błogosławieni, którzy strzegą świadectw jego, i którzy go ze wszystkiego serca szukają;
Odala ndi amene amasunga malamulo ake, amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse.
3 I którzy nie czynią nieprawości, ale chodzą drogami jego.
Sachita cholakwa chilichonse; amayenda mʼnjira zake.
4 Tyś przykazał, aby pilnie strzeżono rozkazań twoich.
Inu mwapereka malangizo ndipo ayenera kutsatidwa kwathunthu.
5 Oby wyprostowane były drogi moje ku przestrzeganiu praw twoich!
Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika pa kumvera zophunzitsa zanu!
6 Tedy nie będę zawstydzony, gdy się będę oglądał na wszystkie rozkazania twoje.
Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi, poganizira malamulo anu onse.
7 Będę cię wysławiał w szczerości serca, gdy się nauczę praw sprawiedliwości twojej.
Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama, pamene ndikuphunzira malamulo anu olungama.
8 Ustaw twoich z pilnością strzedz będę; tylko mię nie opuszczaj.
Ndidzamvera zophunzitsa zanu; musanditaye kwathunthu.
9 Jakim sposobem oczyści młodzieniec ścieszkę swoję? Gdy się zachowa według słowa twego.
Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake? Akawasamala potsata mawu anu.
10 Ze wszystkiego serca mego szukam cię; nie dopuszczajże mi błądzić od rozkazań twoich.
Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse; musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu.
11 W sercu mojem składam wyroki twoje, abym nie zgrzeszył przeciwko tobie.
Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga kuti ndisakuchimwireni.
12 Błogosławionyś ty, Panie! nauczże mię ustaw twoich.
Mutamandike Inu Yehova; phunzitseni malamulo anu.
13 Wargami mojemi opowiadam wszystkie sądy ust twoich.
Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse amene amachokera pakamwa panu.
14 W drodze świadectw twoich kocham się więcej, niż we wszystkich bogactwach.
Ndimakondwera potsatira malamulo anu monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri.
15 O przykazaniach twoich rozmyślam, i przypatruję się drogom twoim.
Ndimalingalira malangizo anu ndipo ndimaganizira njira zanu.
16 W ustawach twoich kocham się, i nie zapominam słów twoich.
Ndimakondwera ndi malamulo anu; sindidzayiwala konse mawu anu.
17 Daruj to słudze twemu, abym żył, a przestrzegał słów twoich.
Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; kuti tsono ndisunge mawu anu.
18 Odsłoń oczy moje, abym się przypatrzył dziwom z zakonu twego.
Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu.
19 Jestem gościem na ziemi; nie ukrywaj przedemną rozkazań twoich.
Ine ndine mlendo pa dziko lapansi; musandibisire malamulo anu.
20 Omdlewa dusza moja, pragnąc sądów twoich na każdy czas.
Moyo wanga wafowoka polakalaka malamulo anu nthawi zonse.
21 Wytraciłeś pysznych; przeklęci są ci, którzy błądzą od rozkazań twoich.
Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa, amene achoka pa malamulo anu.
22 Oddal odemnie pohańbienie i wzgardę, gdyż strzegę świadecwt twoich.
Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo pakuti ndimasunga malamulo anu.
23 I książęta zasiadają, a mówią przeciwko mnie; wszakże sługa twój rozmyśla w ustawach twoich.
Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza, mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu.
24 Świadectwa twoje zaiste są mojem kochaniem, i radcami mymi.
Malamulo anu amandikondweretsa; ndiwo amene amandilangiza.
25 Przylgnęła do prochu dusza moja; ożywże mię według słowa twego.
Moyo wanga wakangamira fumbi; tsitsimutseni molingana ndi mawu anu.
26 Drogi moje rozpowiedziałem, a wysłuchałeś mię; naucz mię ustaw twoich.
Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha; phunzitseni malamulo anu.
27 Daj, abym zrozumiał drogę rozkazań twoich, ażebym rozmyślał o dziwnych sprawach twoich.
Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu; pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu.
28 Rozpływa się od smutku dusza moja; utwierdźże mię według słowa twego.
Moyo wanga wafowoka ndi chisoni; limbikitseni monga mwa mawu anu.
29 Drogę kłamliwą oddal odemnie, a zakonem twoim udaruj mię.
Mundichotse mʼnjira zachinyengo; mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.
30 Obrałem drogę prawdy, a sądy twoje przekładam sobie.
Ndasankha njira ya choonadi; ndayika malamulo anu pa mtima panga.
31 Przystałem do świadectw twoich; Panie! nie zawstydzajże mię.
Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
32 Drogą przykazań twoich pobieżę, gdy rozszerzysz serce moje.
Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu, pakuti Inu mwamasula mtima wanga.
33 Naucz mię, Panie! drogi ustaw twoich, a będę jej strzegł aż do końca.
Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu; ndipo ndidzazisunga mpaka kumapeto.
34 Daj mi rozum, abym strzegł zakonu twego, ażebym go przestrzegał ze wszystkiego serca.
Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse.
35 Daj, abym chodził ścieżką przykazań twoich, gdyż w tem jest upodobanie moje.
Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu, pakuti mʼmenemo ndimapezamo chikondwerero changa.
36 Nakłoń serce moje do świadectw twoich, a nie do łakomstwa.
Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu, osati chuma.
37 Odwróć oczy moje, aby nie patrzały na marność; na drodze twojej ożyw mię.
Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe; sungani moyo wanga monga mwa mawu anu.
38 Utwierdź wyrok twój słudze twemu, który się oddał bojaźni twojej.
Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu, kuti Inu muopedwe.
39 Oddal odemnie pohańbienie moje, którego się boję; bo sądy twoje dobre.
Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa, pakuti malamulo anu ndi abwino.
40 Oto pragnę rozkazań twoich; w sprawiedliwości twojej ożyw mię.
Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu! Sungani moyo wanga mʼchilungamo chanu.
41 Niech na mię przyjdą litości twoje, Panie! i zbawienie twoje według wyroku twego.
Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova, chipulumutso chanu monga mwa lonjezo lanu;
42 Tak abym odpowiedź mógł dać samą rzeczą temu, który mi urąga, gdyż ufam w słowie twojem.
ndipo ndidzayankha amene amandinyoza, popeza ndimadalira mawu anu.
43 A nie wyjmuj z ust moich słowa najprawdziwszego; albowiem sądów twoich oczekuję.
Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga, pakuti ndakhazikitsa chiyembekezo changa mʼmalamulo anu.
44 I będę strzegł zakonu twego zawsze, aż na wieki wieczne.
Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse, ku nthawi za nthawi.
45 A ustawicznie będę chodził na przestrzeństwie, bom się dopytał rozkazań twoich.
Ndidzayendayenda mwaufulu, chifukwa ndinafunafuna malangizo anu.
46 Owszem, będę mówił o świadectwach twoich przed królmi, a nie będę zawstydzony.
Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu ndipo sindidzachititsidwa manyazi,
47 Bom się rozkochał w przykazaniach twoich, którem umiłował.
popeza ndimakondwera ndi malamulo anu chifukwa ndimawakonda.
48 Przyłożę i ręce moje do rozkazań twoich, które miłuję, a będę rozmyślał o ustawach twoich.
Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda, ndipo ndimalingalira malangizo anu.
49 Wspomnij na słowo wyrzeczone do sługi twego, któremeś mię ubezpieczył.
Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu, popeza mwandipatsa chiyembekezo.
50 Toć pociecha moja w utrapieniu mojem, że mię wyrok twój ożywia.
Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi: lonjezo lanu limasunga moyo wanga.
51 Pyszni bardzo się ze mnie naśmiewają; wszakże się od zakonu twego nie uchylam.
Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa, koma sindichoka pa malamulo anu.
52 Bo pamiętam na sądy twoje wieczne, Panie! któremi się cieszę.
Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale, ndipo mwa iwo ndimapeza chitonthozo.
53 Strach mię ogarnął nad niezbożnymi, którzy opuszczają zakon twój.
Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa amene ataya malamulo anu.
54 Są mi ustawy twoje pieśniami w domu pielgrzymstwa mego.
Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga kulikonse kumene ndigonako.
55 Wspominam sobie i w nocy na imię twoje, Panie! i strzegę zakonu twego.
Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova, ndipo ndidzasunga malamulo anu.
56 Toć mam z tego, że przestrzegam przykazań twoich.
Ichi ndicho ndakhala ndikuchita: ndimasunga malangizo anu.
57 Rzekłem: Panie! to jest cząstka moja, przestrzegać słów twoich.
Yehova, Inu ndiye gawo langa; ndalonjeza kumvera mawu anu.
58 Modlę się przed obliczem twojem ze wszystkiego serca; zmiłujże się nademną według słowa twego.
Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse; mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu.
59 Uważyłem w myślach drogi moje, a obróciłem nogi moje ku świadectwom twoim.
Ndinalingalira za njira zanga ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu.
60 Śpieszę się, a nie omieszkuję przestrzegać rozkazań twoich.
Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza kumvera malamulo anu.
61 Hufy niepobożnych złupiły mię; ale na zakon twój nie zapominam.
Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe, sindidzayiwala lamulo lanu.
62 O północy wstaję, abym cię wysławiał w sądach sprawiedliwości twojej.
Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu chifukwa cha malamulo anu olungama.
63 Jestem towarzyszem wszystkich, którzy się ciebie boją, i tych, którzy przestrzegają przykazań twoich.
Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani, kwa onse amene amatsatira malangizo anu.
64 Panie! pełna jest ziemia miłosierdzia twego; nauczże mię ustaw twoich.
Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika, phunzitseni malamulo anu.
65 Łaskawieś postąpił ze sługą twoim, Panie! według słowa twego.
Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu molingana ndi mawu anu.
66 Dobrego rozumu i umiejętności naucz mię; bom przykazaniom twoim uwierzył.
Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino, pakuti ndimakhulupirira malamulo anu.
67 Pierwej niżem się był uniżył, błądziłem; ale teraz wyroku twego przestrzegam.
Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera, koma tsopano ndimamvera mawu anu.
68 Dobryś ty i dobrotliwy; nauczże mię ustaw twoich.
Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino; phunzitseni malamulo anu.
69 Uknowali hardzi kłamstwo przeciwko mnie; ale ja ze wszystkiego serca strzegę przykazań twoich.
Ngakhale odzikuza andipaka mabodza, ine ndimasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.
70 Serce ich zatyło jako sadło; ale się ja zakonem twoim cieszę.
Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa, koma ine ndimakondwera ndi malamulo anu.
71 Jest mi to ku dobremu, żem był utrapiony, abym się nauczył ustaw twoich.
Ndi bwino kuti ndinasautsidwa kuti ndithe kuphunzira malamulo anu.
72 Lepszy mi jest zakon ust twoich, niżeli tysiące złota i srebra.
Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri kuposa ndalama zambirimbiri za siliva ndi golide.
73 Ręce twoje uczyniły mię, i wykształtowały mię; dajże mi rozum, abym się nauczył przykazań twoich;
Manja anu anandilenga ndi kundiwumba; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu.
74 Aby się radowali bojący się ciebie, ujrzawszy mię, że na słowo twoje oczekuję.
Iwo amene amakuopani akondwere akandiona, chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
75 Znam, Panie! iż są sprawiedliwe sądy twoje, a iżeś mię słusznie utrapił.
Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
76 Niechajże mię, proszę, ucieszy miłosierdzie twoje według wyroku twego, któryś uczynił słudze twemu.
Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa, molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu.
77 Niechże na mię przyjdą litości twoje, abym żył; bo zakon twój jest kochaniem mojem.
Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo, popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa.
78 Niech będą zawstydzeni pyszni, przeto, że mię chytrze podwrócić chcieli; ale ja rozmyślać będę w przykazaniach twoich.
Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa; koma ine ndidzalingalira malangizo anu.
79 Niech się obrócą do mnie, którzy się ciebie boją, i którzy znają świadectwa twoje.
Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine, iwo amene amamvetsetsa umboni wanu.
80 Niech będzie serce moje uprzejme przy ustawach twoich, abym nie był zawstydzony.
Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu kuti ndisachititsidwe manyazi.
81 Tęskni dusza moja po zbawieniu twojem, oczekuję na słowo twoje.
Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu, koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
82 Ustały oczy moje, czekając wyroku twego, gdy mówię: Kiedyż mię pocieszysz?
Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu; Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?”
83 Chociażem jest jako naczynie skórzane w dymie, wszakżem ustaw twoich nie zapomniał.
Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi sindiyiwala zophunzitsa zanu.
84 Wieleż będzie dni sługi twego? kiedyż sąd wykonasz nad tymi, którzy mię prześladują?
Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti? Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza?
85 Pyszni pokopali mi doły, co nie jest według zakonu twojego.
Anthu osalabadira za Mulungu, odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu.
86 Wszystkie przykazania twoje są prawdą; bez przyczyny mię prześladują; ratujże mię.
Malamulo anu onse ndi odalirika; thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa.
87 Bez mała mię już wniwecz nie obrócili na ziemi; a wszakżem ja nie opuścił przykazań twoich.
Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi koma sindinataye malangizo anu.
88 Według miłosierdzia twego ożyw mię, abym strzegł świadectwa ust twoich.
Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu.
89 O Panie! słowo twoje trwa na wieki na niebie.
Mawu anu Yehova ndi amuyaya; akhazikika kumwambako.
90 Od narodu do narodu prawda twoja; ugruntowałeś ziemię, i stoi.
Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse; Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe.
91 Według rozrządzenia twego trwa to wszystko aż do dnia tego; wszystko to zaiste jest ku służbie twojej.
Malamulo anu alipobe mpaka lero lino, pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu.
92 By był zakon twój nie był kochaniem mojem, dawnobym był zginął w utrapieniu mojem.
Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa, ndikanawonongeka mʼmasautso anga.
93 Na wieki nie zapomnę na przykazania twoje, gdyżeś mię w nich ożywił.
Ine sindidzayiwala konse malangizo anu, pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga.
94 Twójcim ja, zachowajże mię; bo przykazań twoich szukam.
Ndine wanu, ndipulumutseni; pakuti ndasamala malangizo anu.
95 Czekają na mię niezbożnicy, aby mię zatracili; ale ja świadectwa twoje uważam.
Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge, koma ndidzalingalira umboni wanu.
96 Wszelkiej rzeczy koniec widzę; ale przykazanie twoje bardzo szerokie.
Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire, koma malamulo anu alibe malire konse.
97 O jakom się rozmiłował zakonu twego! tak, iż każdego dnia jest rozmyślaniem mojem.
Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu! Ndimalingaliramo tsiku lonse.
98 Nad nieprzyjaciół moich mędrszym mię czynisz przykazaniem twojem; bo je mam ustawicznie przed sobą.
Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga, popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse.
99 Nad wszystkich nauczycieli moich stałem się rozumniejszym; bo świadectwa twoje są rozmyślaniem mojem.
Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse popeza ndimalingalira umboni wanu.
100 Nad starców jestem roztropniejszy; bo przykazań twoich przestrzegam.
Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba, popeza ndimamvera malangizo anu.
101 Od wszelkiej złej drogi zawściągam nogi swoje, abym strzegł słowa twego.
Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa kuti ndithe kumvera mawu anu.
102 Od sądów twoich nie odstępuję, przeto, że ich ty mnie uczysz.
Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu, pakuti Inu mwini munandiphunzitsa.
103 O jako są słodkie słowa twoje podniebieniu memu! nad miód są słodsze ustom moim.
Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa, otsekemera kuposa uchi mʼkamwa mwanga!
104 Z przykazań twoich nabyłem rozumu: przetoż mam w nienawiści wszelką ścieszkę obłędliwą.
Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu; kotero ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
105 Słowo twe jest pochodnią nogą moim, a światłością ścieszce mojej.
Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga ndi kuwunika kwa pa njira yanga.
106 Przysięgłem i uczynię temu dosyć, że będę strzegł sądów sprawiedliwości twojej.
Ndalumbira ndipo ndatsimikiza, kuti ndidzatsatira malamulo anu olungama.
107 Jestem bardzo utrapiony; o Panie! ożyw mię według słowa twego.
Ndazunzika kwambiri; Inu Yehova, sungani moyo wanga molingana ndi mawu anu.
108 Panie! dobrowolne śluby ust moich przyjmij proszę za wdzięczne, a sądów twoich naucz mię.
Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga, ndipo ndiphunzitseni malamulo anu.
109 Dusza moja jest w ustawicznem niebezpieczeństwie; wszakże na zakon twój nie zapominam.
Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi, sindidzayiwala malamulo anu.
110 Sidło na mię niezbożnicy zastawili; lecz ja się od przykazań twoich nie obłądzę.
Anthu oyipa anditchera msampha, koma sindinasochere kuchoka pa malangizo anu.
111 Za dziedzictwo wieczne wziąłem świadectwa twoje; bo są radością serca mego.
Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya; Iwo ndiye chimwemwe cha mtima wanga.
112 Nakłoniłem serca mego ku wykonywaniu ustaw twoich ustawicznie, i aż do końca (żywota).
Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu mpaka kumapeto kwenikweni.
113 Wymysły mam w nienawiści, a zakon twój miłuję.
Ndimadana ndi anthu apawiripawiri, koma ndimakonda malamulo anu.
114 Tyś jest ucieczką moją, i tarczą moją; na słowo twoje oczekuję.
Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
115 Odstąpcież odemnie złośnicy, abym strzegł rozkazania Boga mojego.
Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa, kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga!
116 Utwierdźże mię według słowa twego, abym żył, a nie zawstydzaj mię w oczekiwaniu mojem.
Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; musalole kuti chiyembekezo changa chipite pachabe.
117 Podpieraj mię, abym był zachowany, i rozmyślał w ustawach twoich ustawicznie.
Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa; nthawi zonse ndidzasamalira zophunzitsa zanu.
118 Podeptałeś wszystkich, którzy się obłądzili od ustaw twoich; albowiem jest kłamliwa zdrada ich.
Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu, pakuti chinyengo chawo ndi chopanda phindu.
119 Odrzucasz jako zużelicę wszystkich niezbożników ziemi; dla tego miłuję świadectwa twoje.
Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala; nʼchifukwa chake ndimakonda umboni wanu.
120 Drży od strachu przed tobą ciało moje; bo się sądów twoich lękam.
Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu; ndimachita mantha ndi malamulo anu.
121 Czynię sądy i sprawiedliwość: nie podawajże mię tym, którzy mi gwałt czynią.
Ndachita zolungama ndi zabwino; musandisiye mʼmanja mwa ondizunza.
122 Zastąp sam sługę twego ku dobremu, aby mię hardzi nie potłoczyli.
Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino, musalole kuti anthu odzikuza andipondereze.
123 Oczy moje ustały, czekając na zbawienie twoje, i na wyrok sprawiedliwości twojej.
Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu, kufunafuna lonjezo lanu lolungama.
124 Obchodź się z sługą twoim według miłosierdzia twego, a ustaw twoich naucz mię.
Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
125 Sługamci ja twój, dajże mi zrozumienie; abym umiał świadectwa twoje.
Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa, kuti ndimvetsetse umboni wanu.
126 Czasci już, abyś czynił Panie! albowiem wzruszono zakon twój.
Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu; malamulo anu akuswedwa.
127 Dlatego umiłowałem rozkazania twoje nad złoto, a nad złoto najwyborniejsze.
Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino,
128 Przeto, że wszystkie przykazania twoje, wszystkie prawdziwe być uznaję, a wszelkie ścieżki obłędliwe mam w nienawiści.
ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka, ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
129 Dziwne są świadectwa twoje; przetoż ich strzeże dusza moja.
Maumboni anu ndi odabwitsa nʼchifukwa chake ndimawamvera.
130 Początek słów twoich oświeca i daje rozum prostakom.
Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika; ngakhale anthu wamba amamvetsetsa.
131 Usta moje otwieram i dyszę; albowiemem przykazań twoich pragnął.
Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu, kufunafuna malamulo anu.
132 Wejżyjże na mię, a zmiłuj się nademną weaług prawa tych, którzy miłują imię twoje.
Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo, monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu.
133 Drogi moje utwierdź w słowie twojem, a niech nademną nie panuje żadna nieprawość.
Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu; musalole kuti tchimo lizindilamulira.
134 Wybaw mię od uciśnienia ludzkiego, abym strzegł rozkazań twoich.
Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza, kuti ndithe kumvera malangizo anu.
135 Rozświeć nad sługą twoim oblicze twoje, a naucz mię ustaw twoich.
Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
136 Strumienie wód płyną z oczów moich dla tych, którzy nie strzegli zakonu twego.
Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga, chifukwa anthu sakumvera malamulo anu.
137 Sprawiedliwyś ty, Panie! i prawdziwy w sądach twoich.
Yehova ndinu wolungama, ndipo malamulo anu ndi abwino.
138 Przykazałeś sprawiedliwe świadectwa twoje, i wielce prawdziwe.
Maumboni amene munatipatsa ndi olungama; ndi odalirika ndithu.
139 Zniszczyła mię gorliwość moja, iż zapominają na słowo twoje nieprzyjaciele moi.
Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu.
140 Doskonale są doświadczone słowa twoje; dlatego się sługa twój w nich rozkochał.
Mawu anu ndi woyera kwambiri nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda.
141 Jam maluczki i wzgardzony; wszakże przykazań twoich nie zapominam.
Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka, sindiyiwala malangizo anu.
142 Sprawiedliwość twoja sprawiedliwość wieczna, a zakon twój prawda.
Chilungamo chanu nʼchamuyaya, ndipo malamulo anu nʼchoona.
143 Ucisk i utrapienie przyszło na mię; przykazania twoje są kochaniem mojem.
Mavuto ndi masautso zandigwera, koma ndimakondwera ndi malamulo anu.
144 Sprawiedliwość świadectw twoich trwa na wieki; daj mi rozum, a żyć będę.
Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo.
145 Wołam ze wszystkiego serca, wysłuchajże mię, o Panie! a będę strzegł ustaw twoich.
Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova, ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu.
146 Wołam do ciebie, zachowajże mię, a będę pilen świadectw twoich.
Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni ndipo ndidzasunga umboni wanu.
147 Uprzedzam cię na świtaniu i wołam, na słowo twoje oczekując.
Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
148 Uprzedzają straż nocną oczy moje, przeto, abym rozmyślał o wyrokach twoich.
Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku, kuti ndithe kulingalira malonjezo anu.
149 Panie! głos mój usłysz według miłosierdzia twego; według sądu twego ożyw mię.
Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu.
150 Przybliżają się, którzy naśladują złości, ci, którzy się od zakonu twego oddalili.
Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira, koma ali kutali ndi malamulo anu.
151 Bliskoś ty jest, Panie! a wszystkie przykazania twoje są prawdą.
Koma Inu Yehova muli pafupi, malamulo anu onse ndi woona.
152 Dawno to wiem o świadectwach twoich, żeś je na wieki ugruntował.
Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya.
153 Obacz utrapienie moje, a wyrwij mię; bom na zakon twój nie zapomniał.
Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
154 Stań przy sprawie mojej, a obroń mię; dla słowa twego ożyw mię.
Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola; sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu.
155 Dalekoć jest od niezbożników zbawienie; bo się nie badają o ustawach twoich.
Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa, pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu.
156 Wielkie są litości twoje, Panie! według sądów twoich ożyw mię.
Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu; sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu.
157 Wieleć jest prześladowców moich i nieprzyjaciół moich; wszakże od świadectw twoich nie uchylam się.
Adani amene akundizunza ndi ambiri, koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu.
158 Widziałem przestępców, i mierziało mię to, że wyroku twego nie przestrzegali.
Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro, popeza samvera mawu anu.
159 Obaczże Panie! iż rozkazania twoje miłuję; według miłosierdzia twego ożyw mię.
Onani momwe ndimakondera malangizo anu; sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika.
160 Najprzedniejsza rzecz słowa twego jest prawda, a na wieki trwa wszelki sąd sprawiedliwości twojej.
Mawu anu onse ndi owona; malamulo anu onse olungama ndi amuyaya.
161 Książęta mię prześladują bez przyczyny; wszakże słów twoich boi się serce moje.
Olamulira amandizunza popanda chifukwa, koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu.
162 Ja się weselę z wyroku twego, tak jako ten, który znajduje wielkie korzyści.
Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu, ngati munthu amene wapeza chuma chambiri.
163 Ale nienawidzę kłamstwa, i brzydzą się niem; ale zakon twój miłuję.
Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho, koma ndimakonda malamulo anu.
164 Chwalę cię siedm kroć przez dzień, dla sądów twoich sprawiedliwych.
Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku pakuti malamulo anu ndi olungama.
165 Pokój wielki dajesz tym, którzy miłują zakon twój, a nie doznawają żadnego obrażenia.
Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu, ndipo palibe chimene chingawapunthwitse
166 Panie! oczekuję zbawienia twego; a przykazania twoje wykonywam.
Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova, ndipo ndimatsatira malamulo anu.
167 Przestrzega dusza moja świadectw twoich; albowiem je bardzo miłuję.
Ndimamvera umboni wanu pakuti ndimawukonda kwambiri.
168 Przestrzegam przykazań twoich i świadectw twoich; albowiem wszystkie drogi moje są przed tobą.
Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu, pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu.
169 Panie! niech się przybliży wołanie moje przed oblicze twoje; według słowa twego daj mi zrozumienie.
Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova; patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu.
170 Niech przyjdzie prośba moja przed twarz twoję, a według obietnicy twojej wyrwij mię.
Kupempha kwanga kufike pamaso panu; pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu.
171 Chwałę wydadzą wargi moje, gdy mię nauczysz ustaw twoich.
Matamando asefukire pa milomo yanga, pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu.
172 Opowiadać będzie język mój wyroki twoje; bo wszystkie przykazania twoje są sprawiedliwość.
Lilime langa liyimbe mawu anu, popeza malamulo anu onse ndi olungama.
173 Niech mi będzie na pomocy ręka twoja, gdyżem sobie obrał przykazania twoje.
Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza pakuti ndasankha malangizo anu.
174 Panie! zbawienia twego pragnę, a zakon twój jest kochaniem mojem.
Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova, ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu.
175 Żyć będzie dusza moja, i będzie cię chwaliła, a sądy twoje będą mi na pomocy.
Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni, ndipo malamulo anu andichirikize.
176 Błądzę jako owca zgubiona, szukajże sługi twego; boć przykazań twoich nie zapominam.
Ndasochera ngati nkhosa yotayika, funafunani mtumiki wanu, pakuti sindinayiwale malamulo anu.

< Psalmów 119 >