< Psalmów 118 >

1 Wysławiajcie Pana, albowiem dobry; albowiem na wieki trwa miłosierdzie jego;
Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.
2 Rzecz teraz, Izraelu! że na wieki miłosierdzie jego.
Israeli anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
3 Rzecz teraz, domie Aaronowy! że na wieki miłosierdzie jego.
Banja la Aaroni linene kuti, “Chikondi chake ndi chosatha.”
4 Rzeczcież teraz, którzy się boicie Pana, że na wieki miłosierdzie jego.
Iwo amene amaopa Yehova anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
5 W ucisku wzywałem Pana; wysłuchał mię, i na przestrzeństwie postawił mię Pan.
Ndili mʼmasautso anga ndinalirira Yehova, ndipo Iye anayankha pondichotsa mʼmasautsowo.
6 Pan jest zemną, nie będę się bał, żeby mi co uczynił człowiek.
Yehova ali nane; sindidzachita mantha. Munthu angandichite chiyani?
7 Pan jest zemną między pomocnikami mymi; przetoż ja oglądam pomstę nad tymi, którzy mię mają w nienawiści.
Yehova ali nane; Iye ndiye thandizo langa. Ndidzayangʼana adani anga mwachipambano.
8 Lepiej mieć nadzieję w Panu, niżeli ufać w człowieku.
Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira munthu.
9 Lepiej mieć nadzieję w Panu, niżeli ufać w książętach.
Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira mafumu.
10 Wszystkie narody ogarnęły mię; ale w imieniu Pańskim wygubiłem ich.
Anthu a mitundu yonse anandizinga, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
11 Częstokroć mię ogarnęły; ale w imieniu Pańskiem wygubiłem ich.
Anandizinga mbali zonse, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
12 Ogarnęły mię jako pszczoły, ale zgasły jako ogień z ciernia; bo w imieniu Pańskiem wytraciłem ich.
Anandizinga ngati njuchi, koma anatha msanga ngati moto wapaminga; mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
13 Bardzoś potężnie na mię nacierał, abym upadł; ale Pan poratował mię.
Anandikankha uku ndi uko ndipo ndinali pafupi kugwa, koma Yehova anandithandiza.
14 Pan jest mocą moją, i pieśnią moją; on był moim wybawicielem.
Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga; Iye wakhala chipulumutso changa.
15 Głos wykrzykania i zbawienia w przybytkach sprawiedliwych, prawica Pańska dokazała mocy;
Mfuwu wachimwemwe ndi chipambano ukumveka mʼmatenti a anthu olungama mtima kuti: “Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!
16 Prawica Pańska wywyższyła się; prawica Pańska dokazała mocy.
Dzanja lamanja la Yehova latukulidwa mmwamba Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!”
17 Nie umrę, ale będę żył, abym opowiadał sprawy Pańskie.
Sindidzafa koma ndidzakhala ndi moyo ndipo ndidzalalika za ntchito ya Yehova.
18 Pokarałci mię Pan srodze; ale mię na śmierć nie podał.
Yehova wandilanga koopsa, koma sanandipereke ku imfa.
19 Otwórzcie mi bramy sprawiedliwości, a wszedłszy w nie będę wysławiał Pana.
Tsekulireni zipata zachilungamo, kuti ndifike kudzayamika Yehova.
20 Tać jest brama Pańska, którą sprawiedliwi wchodzą.
Ichi ndicho chipata cha Yehova chimene olungama mtima okha adzalowerapo.
21 Tuć ja ciebie wysławiać będę; boś mię wysłuchał, i byłeś wybawicielem moim.
Ndidzakuyamikani chifukwa Inu munandiyankha; mwakhala chipulumutso changa.
22 Kamień, którzy odrzucili budujący, uczyniony jest głową węgielną.
Mwala umene amisiri omanga nyumba anawukana wasanduka wapangodya;
23 Od Pana się to stało, a jest dziwno w oczach naszych.
Yehova ndiye wachita zimenezi ndipo nʼzodabwitsa pamaso pathu.
24 Tenci to dzień, który uczynił Pan; rozweselmyż się, a rozradujmy się weń.
Lero ndiye tsiku limene Yehova walipanga; tiyeni tikondwere ndi kusangalala nalo.
25 Proszę, Panie! zachowajże teraz; proszę Panie! zdarz teraz.
Inu Yehova, tipulumutseni; Yehova, tipambanitseni.
26 Błogosławiony, który przychodzi w imię Pańskie; błogosławimy wam z domu Pańskiego.
Wodala amene akubwera mʼdzina la Yehova. Tikukudalitsani kuchokera ku nyumba ya Yehova.
27 Bógci Panem, onci nas oświecił; przywiążcie baranki powrozami ku ofierze aż do rogów ołtarza.
Yehova ndi Mulungu, ndipo kuwala kwake kwatiwunikira Ife. Lowani nawo pa mʼdipiti wa ku chikondwerero mutanyamula nthambi mʼdzanja lanu, mpaka ku nyanga za guwa.
28 Tyś jest Bóg mój; przetoż cię wysławiać będę, Boże mój! wywyższać cię będę.
Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakuyamikani; Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakukwezani.
29 Wysławiajcież Pana, albowiem jest dobry: albowiem na wieki miłosierdzie jego.
Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.

< Psalmów 118 >