< Psalmów 116 >

1 Miłuję Pana, iż wysłuchał głos mój, i prośby moje.
Ndimakonda Yehova pakuti Iyeyo amamva mawu anga; Iye amamva kulira kwanga kopempha chifundo.
2 Albowiem nakłonił ucha swego ku mnie, gdym go wzywał za dni moich.
Pakuti ananditchera khutu, ndidzayitana Iye masiku onse a moyo wanga.
3 Ogarnęły mię były boleści śmierci, a utrapienia grobu zjęły mię; ucisk i boleść przyszła na mię. (Sheol h7585)
Zingwe za imfa zinandizinga, zoopsa za ku dziko la anthu akufa zinandigwera; ndinapeza mavuto ndi chisoni. (Sheol h7585)
4 I wzywałem imienia Pańskiego, mówiąc: Proszę, o Panie! wybaw duszę moję.
Pamenepo ndinayitana dzina la Yehova: “Inu Yehova, pulumutseni!”
5 Miłościwy Pan i sprawiedliwy, Bóg nasz litościwy.
Yehova ndi wokoma mtima ndi wolungama Mulungu wathu ndi wodzaza ndi chifundo.
6 Pan prostaczków strzeże; byłem uciśniony, a wspomógł mię.
Yehova amateteza munthu wodzichepetsa mtima; pamene ndinali ndi chosowa chachikulu, Iye anandipulumutsa.
7 Nawróć się, duszo moja! do odpocznienia swego; albowiem ci Pan dobrze uczynił.
Pumula iwe moyo wanga, pakuti Yehova wakuchitira zokoma.
8 Bo wyrwał duszę moję od śmierci, oczy moje od płaczu, nogę moję od upadku.
Pakuti Inu Yehova mwapulumutsa moyo wanga ku imfa, maso anga ku misozi, mapazi anga kuti angapunthwe,
9 Będę chodził ustawicznie przed oblicznością Pańską w ziemi żyjących.
kuti ine ndiyende pamaso pa Yehova mʼdziko la anthu amoyo.
10 Uwierzyłem, dlategom mówił, chociażem bardzo był utrapiony.
Ine ndinakhulupirira; choncho ndinati, “Ndasautsidwa kwambiri.”
11 Jam był rzekł w zatrwożeniu mojem: Wszelki człowiek kłamca.
Ndipo ndili mʼnkhawa yanga ndinati, “Anthu onse ndi abodza.”
12 Cóż oddam Panu za wszystkie dobrodziejstwa jego, które mi uczynił?
Ndingamubwezere chiyani Yehova, chifukwa cha zokoma zake zonse zimene wandichitira?
13 Kielich obfitego zbawienia wezmę, a imienia Pańskiego wzywać będę,
Ndidzakweza chikho cha chipulumutso ndipo ndidzayitana dzina la Yehova.
14 Śluby moje oddam Panu, a to zaraz przed wszystkim ludem jego.
Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse.
15 Droga jest przed oczyma Pańskiemi śmierć świętych jego.
Imfa ya anthu oyera mtima ndi yamtengowapatali pamaso pa Yehova.
16 O mój Panie! żem ja sługą twoim, jam sługą twoim, synem służebnicy twojej, rozwiązałeś związki moje.
Inu Yehova, zoonadi ndine mtumiki wanu: ndine mtumiki wanu, mwana wa mdzakazi wanu; Inu mwamasula maunyolo anga.
17 Tobie ofiarować będę ofiarę chwały, i imienia Pańskiego wzywać będę.
Ndidzapereka nsembe yachiyamiko kwa Inu ndipo ndidzayitanira pa dzina la Yehova.
18 Śluby moje oddam Panu, a to zaraz przed wszystkim ludem jego,
Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse,
19 W przysionkach domu Pańskiego, w pośrodku ciebie, Jeruzalemie! Halleluja.
mʼmabwalo a nyumba ya Yehova, mʼkati mwako iwe Yerusalemu. Tamandani Yehova.

< Psalmów 116 >