< Psalmów 114 >

1 Gdy wychodził Izrael z Egiptu i dom Jakóbowy z narodu obcego,
Pamene Israeli anatuluka mu Igupto, nyumba ya Yakobo kuchoka ku mtundu wa anthu a chiyankhulo chachilendo,
2 Stał się Juda poświęceniem jego, Izrael panowaniem jego.
Yuda anasanduka malo opatulika a Mulungu, Israeli anasanduka ufumu wake.
3 To widząc morze, uciekło a Jordan wrócił się nazad.
Nyanja inaona ndi kuthawa, mtsinje wa Yorodani unabwerera mʼmbuyo;
4 Góry skakały jako barany, pogórki jako jagnięta.
mapiri analumphalumpha ngati nkhosa zazimuna, timapiri ngati ana ankhosa.
5 Morze! cóż ci się stało, iżeś uciekło? O Jordanie! żeś się nazad wrócił?
Nʼchifukwa chiyani iwe unathawa? iwe mtsinje wa Yorodani unabwereranji mʼmbuyo?
6 Góry! żeście skakały jako barany? pagórki! jako jagnięta?
inu mapiri, munalumphalumphiranji ngati nkhosa zazimuna, inu timapiri, ngati ana ankhosa?
7 Przed obliczem Pańskiem zadrżała ziemia, przed obliczem Boga Jakóbowego.
Njenjemera pamaso pa Ambuye iwe dziko lapansi, pamaso pa Mulungu wa Yakobo,
8 Który obraca opokę w jezioro wód, a krzemień w źródło wód.
amene anasandutsa thanthwe kukhala chitsime, thanthwe lolimba kukhala akasupe a madzi.

< Psalmów 114 >