< Psalmów 113 >

1 Halleluja. Chwalcie słudzy Pańscy, chwalcie imię Pańskie.
Tamandani Yehova. Mutamandeni, inu atumiki a Yehova, tamandani dzina la Yehova.
2 Niechaj będzie imię Pańskie błogosławione, odtąd aż na wieki.
Yehova atamandidwe, kuyambira tsopano mpaka muyaya.
3 Od wschodu słońca, aż do zachodu jego, niech będzie chwalebne imię Pańskie.
Kuyambira ku matulukiro a dzuwa mpaka ku malowero ake, dzina la Yehova liyenera kutamandidwa.
4 Pan jest nad wszystkie narody wywyższony; chwała jego nad niebiosa.
Yehova wakwezeka pa anthu a mitundu yonse, ulemerero wake ndi woposa mayiko akumwamba.
5 Któż taki, jako Pan Bóg nasz, który mieszka na wysokości?
Ndani wofanana ndi Yehova Mulungu wathu, Iye amene amakhala mwaufumu mmwamba?
6 Który się zniża, aby widział, co jest na niebie i na ziemi.
amene amawerama pansi kuyangʼana miyamba ndi dziko lapansi?
7 Podnosi z prochu nędznego, a z gnoju wywyższa ubogiego,
Iye amakweza munthu wosauka kuchoka pa fumbi ndi kutukula munthu wosowa kuchoka pa dzala;
8 Aby go posadził z książętami, z książętami ludu swego;
amawakhazika pamodzi ndi mafumu, pamodzi ndi mafumu a anthu ake.
9 Który sprawia, że niepłodna w domu bywa matką weselącą się z dziatek. Halleluja.
Amakhazikitsa mayi wosabereka mʼnyumba yake monga mayi wa ana wosangalala. Tamandani Yehova.

< Psalmów 113 >