< Psalmów 112 >

1 Halleluja. Błogosławiony mąż, który się Pana boi, a w przykazaniach jego ma wielkie kochanie.
Tamandani Yehova. Wodala munthu amene amaopa Yehova, amene amakondwera kwambiri ndi malamulo ake.
2 Możne będzie na ziemi nasienie jego; rodzina szczerych błogosławiona będzie.
Ana ake adzakhala amphamvu mʼdziko; mʼbado wa olungama mtima udzadalitsidwa.
3 Majętność i bogactwa są w domu jego, a sprawiedliwość jego trwa na wieki.
Kulemera ndi chuma zili mʼnyumba yake, ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
4 Szczerym w ciemnościach światłość wschodzi; łaskawy, miłosierny, i sprawiedliwy jest Bóg.
Ngakhale mu mdima kuwala kumatulukira olungama mtima; wokoma mtima, wachifundo ndi wowongoka mtima.
5 Dobry człowiek litościwym jest, i pożycza, a rzeczy swe miarkuje rozsądkiem.
Zinthu zabwino zidzabwera kwa iye amene amapereka mowolowamanja ndi wokongoletsa mwaufulu, amene amachita ntchito yake mwachilungamo.
6 Bo na wieki nie będzie poruszony; w pamięci wiecznej będzie sprawiedliwy.
Ndithu sadzagwedezeka; munthu wolungama sadzayiwalika mpaka muyaya.
7 Słysząc złe nowiny, nie boi się; stateczne serce jego ufa w Panu.
Saopa akamva zoyipa zimene zachitika; mtima wake ndi wokhazikika ndipo amadalira Yehova.
8 Umocnione serce jego nie boi się, aż ogląda pomstę nad nieprzyjaciołmi swymi.
Mtima wake ndi wotetezedwa, sadzakhala ndi mantha; potsiriza pake adzayangʼana adani ake mwachipambano.
9 Rozprasza, i daje ubogim; sprawiedliwość jego trwa na wieki; róg jego wywyższy się w sławie.
Wopereka mphatso zake mowolowamanja kwa osauka, chilungamo chake chimanka mpaka muyaya; nyanga yake idzakwezedwa mwaulemu.
10 Widząc to niepobożny, będzie się gniewał, i zębami swemi zgrzytał, i schnąć będzie; żądość niepobożnych zginie.
Munthu woyipa adzaona zimenezi ndipo adzapsa mtima; adzakukuta mano ake ndipo adzasungunuka. Zolakalaka za anthu oyipa sizidzachitika konse.

< Psalmów 112 >