< Psalmów 106 >

1 Halleluja. Wysławiajcie Pana; albowiem dobry, albowiem na wieki miłosierdzie jego.
Tamandani Yehova. Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake ndi chosatha.
2 Któż wysłowi niezmierną moc Pańską, a wypowie wszystkę chwałę jego?
Ndani angathe kufotokoza za ntchito zamphamvu za Yehova kapena kumutamanda mokwanira?
3 Błogosławieni, którzy strzegą sądu, a czynią sprawiedliwość na każdy czas.
Odala ndi amene amasunga chilungamo, amene amachita zolungama nthawi zonse.
4 Pamiętaj na mię, Panie! dla miłości ku ludowi swemu; nawiedźże mię zbawieniem swojem,
Mundikumbukire Yehova, pamene mukuonetsa kukoma mtima kwanu kwa anthu anu, bwerani mudzandithandize pamene mukuwapulumutsa iwo,
5 Abym używał dobrego z wybranymi twoimi, a weselił się w radości narodu twego, i chlubił się wespół z dziedzictwem twojem.
kuti ndidzasangalale ndi chuma cha anthu anu osankhika, kuti ndidzakhale nacho chimwemwe cha anthu anu ndi kukhala pamodzi ndi cholowa chanu pa kukutamandani.
6 Zgrzeszyliśmy z ojcami swymi; niesprawiedliwieśmy czynili, i nieprawość popełniali.
Ife tachimwa monga momwe anachitira makolo athu; tachita zolakwa ndipo tachita moyipa.
7 Ojcowie nasi w Egipcie nie zrozumieli cudów twoich, ani pamiętali na wielkość miłosierdzia twego; ale odpornymi byli przy morzu Czerwonem.
Pamene makolo athu anali mu Igupto, sanalingalire za zozizwitsa zanu; iwo sanakumbukire kukoma mtima kwanu kochuluka, ndipo anawukira Inu pa Nyanja Yofiira.
8 A wszakże ich wyswobodził dla imienia swego, aby oznajmił moc swoję.
Komabe Iye anawapulumutsa chifukwa cha dzina lake, kuti aonetse mphamvu zake zazikulu.
9 Bo zgromił morze Czerwone, i wyschło, a przewiódł ich przez przepaści, jako przez puszczę.
Anadzudzula Nyanja Yofiira, ndipo inawuma; anawatsogolera mʼnyanja yakuya ngati akuyenda mʼchipululu.
10 A tak zachował ich od ręki tego, który ich miał w nienawiści, a wykupił ich z ręki nieprzyjacielskiej.
Anawapulumutsa mʼdzanja la amaliwongo; anawawombola mʼdzanja la mdani.
11 W tem okryły wody tych, którzy ich ciążyli; nie został ani jeden z nich.
Madzi anamiza adani awo, palibe mmodzi wa iwo anapulumuka.
12 A choć uwierzyli słowom jego, i wysławiali chwałę jego:
Kenaka iwo anakhulupirira malonjezo ake ndi kuyimba nyimbo zamatamando.
13 Przecież prędko zapomnieli na sprawy jego, i nie czekali na rady jego.
Koma posachedwa anayiwala zimene Iye anachita, ndipo sanayembekezere uphungu wake.
14 Ale zdjęci będąc chciwością na puszczy, kusili Boga na pustyniach.
Mʼchipululu, anadzipereka ku zilakolako zawo; mʼdziko lopanda kanthu anayesa Mulungu.
15 I dał im, czego żądali, a wszakże przepuścił suchoty na nich.
Choncho Iye anawapatsa chimene anapempha, koma anatumiza nthenda yowondetsa.
16 Zatem gdy się wzruszyli zawiścią przeciw Mojżeszowi w obozie, i przeciw Aaronowi, świętemu Pańskiemu:
Mʼmisasa, anachitira nsanje Mose ndi Aaroni, amene Yehova anadzipatulira.
17 Otworzyła się ziemia, i pożarła Datana, i okryła rotę Abironową,
Nthaka inatsekuka ndipo inameza Datani; inakwirira gulu la Abiramu.
18 I zapalił się ogień na zebranie ich; płomień spalił niepobożnych.
Moto unayaka pakati pa otsatira awo; lawi lamoto linapsereza anthu oyipa.
19 Sprawili i cielca na Horebie, i kłaniali się bałwanowi litemu,
Iwo anapanga mwana wangʼombe pa Horebu ndi kulambira fano loyengedwa kuchokera ku chitsulo.
20 I odmienili chwałę swą w podobieństwo wołu, jedzącego trawę.
Anasinthanitsa ulemerero wawo ndi fano la ngʼombe yayimuna imene imadya udzu.
21 Zapomnieli na Boga, wybawiciela swego, który czynił wielkie rzeczy w Egipcie;
Anayiwala Mulungu amene anawapulumutsa, amene anachita zinthu zazikulu mu Igupto,
22 Rzeczy dziwne w ziemi Chamowej, rzeczy straszne przy morzu Czerwonem.
zozizwitsa mʼdziko la Hamu ndi machitidwe ake woopsa pa Nyanja Yofiira.
23 Przetoż rzekł, że ich chciał wytracić, gdyby się był Mojżesz, wybrany jego, nie stawił w onem rozerwaniu przed nim, a nie odwrócił popędliwości jego, aby ich nie tracił.
Choncho Iye anawawuza kuti adzawawononga, pakanapanda Mose, mtumiki wake wosankhidwa, kuyima pamaso pake, ndi kuletsa mkwiyo wake kuti usawawononge.
24 Wzgardzili też ziemią pożądaną, nie wierząc słowu jego.
Motero iwo ananyoza dziko lokoma; sanakhulupirire malonjezo ake.
25 I szemrząc w namiotach swoich, nie byli posłuszni głosowi Pańskiemu.
Anangʼungʼudza mʼmatenti mwawo ndipo sanamvere Yehova.
26 Przetoż podniósł rękę swoję przeciwko nim, aby ich pobił na puszczy;
Kotero Iye analumbira atakweza dzanja lake, kuti adzachititsa kuti iwowo afere mʼchipululu,
27 A żeby rozrzucił nasienie ich między pogan, i rozproszył ich po ziemiach.
kuchititsa kuti zidzukulu zawo zifere pakati pa anthu a mitundu ina ndi kuwabalalitsa mʼdziko lonse.
28 Sprzęgli się też byli z bałwanem Baalfegorem, a jedli ofiary umarłych.
Iwo anayamba kupembedza Baala-Peori ndi kudya nsembe zoperekedwa kwa milungu yopanda moyo;
29 A tak draźnili Boga sprawami swemi, że się na nich oborzyła plaga;
anaputa mkwiyo wa Yehova pa machitidwe awo oyipa, ndipo mliri unabuka pakati pawo.
30 Aż się zastawił Finees, a pomstę uczynił, i rozerwana jest ona plaga;
Koma Finehasi anayimirira ndi kulowererapo, ndipo mliri unaleka.
31 Co mu poczytano ku sprawiedliwości od narodu do narodu, aż na wieki.
Chimenechi ndicho chinayesedwa chilungamo chake, kwa mibado yosatha imene ikubwera.
32 Znowu go byli wzruszyli do gniewu u wód Meryba, tak, iż się źle działo i z Mojżeszem dla nich.
Pa madzi a ku Meriba iwo anakwiyitsa Yehova ndipo mavuto anabwera kwa Mose chifukwa cha anthuwo,
33 Albowiem rozdraźnili ducha jego, że wyrzekł co niesłuszne usty swemi.
pakuti iwowo anawukira mzimu wa Mulungu, ndipo pa milomo ya Mose panatuluka mawu osayenera.
34 Nadto nie wytracili onych narodów, o których im był Pan powiedział.
Aisraeliwo sanawononge mitundu ya anthu monga momwe Yehova anawalamulira.
35 Ale pomięszawszy się z onemi narodami, nauczyli się spraw ich:
Koma anasakanizana ndi anthu a mitundu inayo ndi kuphunzira miyambo yawo.
36 I służyli bałwanom ich, które im były sidłem.
Ndipo anapembedza mafano awo, amene anakhala msampha kwa iwowo.
37 Albowiem dyjabłom ofiarowali synów swoich, i córki swoje,
Anapereka nsembe ana awo aamuna ndi ana awo aakazi kwa ziwanda.
38 I wylewali krew niewinną, krew synów swoich, i córek swoich, których ofiarowali bałwanom rytym Chananejskim, tak, że splugawiona była ziemia onem krwi rozlaniem.
Anakhetsa magazi a anthu osalakwa, magazi a ana awo aamuna ndi a ana awo aakazi, amene anawapereka nsembe kwa mafano a ku Kanaani, ndipo dziko linayipitsidwa ndi magazi awo.
39 I zmazali się sprawami swemi, a cudzołożyli wynalazkami swemi.
Iwo anadzidetsa okha ndi zimene anachita; ndi machitidwe awo amakhala ngati munthu wachigololo.
40 Przetoż zapaliwszy się Pan w popędliwości przeciw ludowi swemu, obrzydził sobie dziedzictwo swoje,
Tsono Yehova anakwiya ndi anthu ake ndipo ananyansidwa ndi cholowa chake.
41 I podał ich w ręce poganom; a panowali nad nimi, którzy ich mieli w nienawiści;
Iye anawapereka kwa anthu a mitundu ina, ndipo adani awo anawalamulira.
42 I uciskali ich nieprzyjaciele ich, tak, że poniżeni byli pod ręką ich.
Adani awo anawazunza ndi kuwakhazika pansi pa mphamvu yawo.
43 Częstokroć ich wybawiał; wszakże go oni wzruszali do gniewu radami swemi, zaczem poniżeni byli dla nieprawości swoich.
Iye ankawapulumutsa nthawi zambiri, koma iwo ankatsimikiza za kuwukira ndipo anawonongeka mʼmachimo awo.
44 A wszakże wejrzał na ucisk ich, i usłyszał wołanie ich.
Koma Iye anaona kuzunzika kwawo pamene anamva kulira kwawo;
45 Bo sobie wspomniał na przymierze swoje z nimi, a żałował tego według wielkiej litości swojej.
Chifukwa cha iwo Iye anakumbukira pangano lake ndipo anawalezera mtima chifukwa cha kukula kwa chikondi chake.
46 Tak, że im zjednał miłosierdzie przed oczyma wszystkich, którzy ich byli pojmali.
Iye anachititsa kuti amene anawagwira iwo ukapolo awamvere chisoni.
47 Wybawże nas, Panie, Boże nasz! a zgromadź nas z tych pogan, abyśmy wysławiali imię świętobliwości twojej, a chlubili się w chwale twojej.
Tipulumutseni Inu Yehova Mulungu wathu, ndipo mutisonkhanitse kuchoka kwa anthu a mitundu ina kuti tithe kuyamika dzina lanu loyera ndi kunyadira mʼmatamando anu.
48 Błogosławiony Pan, Bóg Izraelski, od wieków aż na wieki; na co niech rzecze wszystek lud: Amen, Halleluja.
Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli, Kuyambira muyaya mpaka muyaya. Anthu onse anene kuti, “Ameni!” Tamandani Yehova.

< Psalmów 106 >