< Psalmów 100 >

1 Psalm dla dziękczynienia. Wykrzykajcie Panu, wszystka ziemio!
Salimo. Nyimbo yothokoza. Fuwulani kwa Yehova mwachimwemwe, inu dziko lonse lapansi.
2 Służcie Panu z weselem, przychodźcie przed oblicze jego z radością.
Mulambireni Yehova mosangalala; bwerani pamaso pake ndi nyimbo zachikondwerero.
3 Wiedzcież, żeć Pan jest Bogiem; on uczynił nas, a nie my samych siebie, abyśmy byli ludem jego, i owcami pastwiska jego.
Dziwani kuti Yehova ndi Mulungu. Iye ndiye amene anatipanga ndipo ife ndife ake; ndife anthu ake, nkhosa za pabusa pake.
4 Wnijdźcież w bramy jego z wysławianiem, a do sieni jego z chwałami; wysławiajcież go, dobrorzeczcież imieniowi jego;
Lowani ku zipata zake ndi chiyamiko ndi ku mabwalo ake ndi matamando; muyamikeni ndi kutamanda dzina lake.
5 Albowiem dobry jest Pan, na wieki trwa miłosierdzie jego, a od narodu aż do narodu prawda jego.
Pakuti Yehova ndi wabwino ndipo chikondi chake ndi chamuyaya; kukhulupirika kwake nʼkokhazikika pa mibado ndi mibado.

< Psalmów 100 >