< Przysłów 8 >

1 Izali mądrość nie woła, i roztropność nie wydaje głosu swego?
Kodi nzeru sikuyitana? Kodi nzeru yomvetsa zinthu sinakweze mawu ake?
2 Na wierzchu wysokich miejsc, przy drodze i na rozstaniu dróg stoi.
Nzeru imayima pa zitunda mʼmbali mwa njira, imayima pa mphambano ya misewu.
3 U bram, kędy się chodzi do miasta, i w wejściu u drzwi woła, mówiąc:
Imafuwula pafupi ndi zipata zolowera mu mzinda, pa makomo olowera imafuwula kuti,
4 Na was wołam, o mężowie! a głos mój obracam do synów ludzkich.
Inu anthu, ndikuyitana inu; ndikuyitanatu anthu onse.
5 Zrozumijcie prostacy ostrożność, a głupi zrozumijcie sercem.
Inu amene simudziwa kanthunu khalani ochenjera; inu amene ndi opusa, khalani ndi mtima womvetsa zinthu.
6 Słuchajcie; bo o wielkich rzeczach będę mówił, a otworzenie warg moich opowie szczerość.
Mverani, pakuti ndikukuwuzani zinthu zofunika kwambiri; ndatsekula pakamwa panga ndipo payankhula zolungama.
7 Zaisteć prawdę mówią usta moje, a niezbożność obrzydliwością jest wargom moim.
Pakamwa panga pamayankhula zoona ndimanyansidwa ndi kuyankhula zoyipa.
8 Sprawiedliwe są wszystkie słowa ust moich; nie masz w nich nic nieprawego ani przewrotnego.
Mawu onse a pakamwa panga ndi olungama; mʼmawu angawo mulibe zokhotakhota kapena zopotoka.
9 Wszystkie są prawe rozumnemu, a uprzejme tym, którzy znajdują umiejętność.
Kwa anthu ozindikira, mawu anga onse ndi woona; kwa anthu amene ali ndi nzeru zomvetsa zinthu, mawu angawo ndi okhoza.
10 Przyjmijcież ćwiczenie moje, a nie srebro, a umiejętność raczej, niż złoto wyborne.
Landirani malangizo anga mʼmalo mwa siliva, nzeru zomvetsa zinthu mʼmalo mwa golide wabwino.
11 Albowiem lepsza jest mądrość niż perły, także wszystkie pożądane rzeczy nie porównają z nią.
Paja nzeru ndi yabwino kwambiri kuposa miyala yamtengowapatali, ndipo zonse zimene ungazifune sizingafanane ndi nzeru.
12 Ja mądrość mieszkam z roztropnością, i umiejętność ostrożności wynajduję.
Ine nzeru, ndimakhala pamodzi ndi kuchenjera. Ine ndimadziwa zinthu ndiponso ndimalingalira zinthu bwino.
13 Bojaźń Pańska jest, mieć w nienawiści złe. Ja nienawidzę pychy, wysokomyślności, i drogi złej, i ust przewrotnych.
Kuopa Yehova ndiko kudana ndi zoyipa. Ine ndimadana ndi kunyada, kudzitama, kuchita zoyipa, ndiponso kuyankhula zonyenga.
14 Przy mnie jest rada, i prawdziwa mądrość; jam jest roztropność, a moc jest moja.
Ndine mwini uphungu ndi maganizo abwino; ndili ndi nzeru yomvetsa zinthu ndiponso mphamvu.
15 Przez mię królowie królują, i książęta stanowią sprawiedliwość.
Ndine amene ndimathandiza mafumu kulamulira. Ndimawathandiza olamulira kukhazikitsa malamulo olungama.
16 Przez mię książęta panują, i wielmożnymi są wszyscy sędziowie ziemi.
Ndine amene ndimathandiza akalonga polamula. Ndinenso amene ndimathandiza akuluakulu onse kulamulira bwino dziko.
17 Ja miłuję tych, którzy mię miłują; a którzy mię szukają rano, znajdują mię.
Ndimakonda amene amandikonda, ndipo amene amandifunafuna amandipeza.
18 Bogactwo i sława przy mnie jest; majętność trwała i sprawiedliwość.
Ine ndili ndi chuma ndi ulemu, chuma ndi kupindula pa ntchito kokhazikika.
19 Lepszy jest owoc mój, niż złoto, i niż najkosztowniejsze złoto, a dochody moje lepsze, niż srebro wyborne.
Chipatso changa ndi chabwino kuposa golide, ngakhale golide wosalala; zimene ine ndimabereka zimaposa siliva wabwino kwambiri.
20 Prowadzę ścieszką sprawiedliwości, pośrodkiem ścieżek sądu,
Ndimachita zinthu zolungama. Ine sindipatuka mʼnjira za chilungamo.
21 Abym tym, którzy mię miłują, dała w dziedzictwo majętność wieczną, i skarby ich napełniła.
Ndimapereka chuma kwa amene amandikonda ndi kudzaza nyumba zawo zosungiramo chuma.
22 Pan mię miał przy początku drogi swej, przed sprawami swemi, przed wszystkiemi czasy.
“Yehova anandilenga ine nzeru monga ntchito yake yoyamba. Mwa ntchito zake zakalekale yoyamba ndinali ine.
23 Przed wieki jestem zrządzona, przed początkiem; pierwej niż była ziemia;
Ndinapangidwa kalekalelo, pachiyambi penipeni dziko lapansi lisanalengedwe.
24 Gdy jeszcze nie było przepaści, spłodzonam jest, gdy jeszcze nie było źródeł opływających wodami.
Nyanja, akasupe odzaza ndi madzi, zonsezi kulibe pamene ine ndinkabadwa.
25 Pierwej niż góry założone były, niż były pagórki, spłodzonam jest.
Mapiri asanakhazikitsidwe pa malo awo, mapiri angʼonoangʼono asanakhalepo, ine ndinali nditabadwa kale,
26 Jeszcze był nie uczynił ziemi, i równin, ani początku prochu okręgu ziemskiego.
lisanalengedwe dziko lapansi ndi minda yake; lisanalengedwe dothi loyamba la dziko lapansi.
27 Gdy gotował niebiosa, tamem była; gdy rozmierzał okrągłość nad przepaściami;
Ine ndinalipo pamene Yehova ankakhazikitsa mlengalenga, pamene ankalemba malire a nyanja yozama,
28 Gdy utwierdzał obłoki w górze, i umacniał źródła przepaści;
pamene anakhazikitsa mitambo ya mlengalenga ndi kukhazikitsa akasupe a madzi ozama,
29 Gdy zakładał morzu granice jego, i wodom, aby nie przestępowały rozkazania jego; gdy rozmierzał grunty ziemi:
pamene anayikira nyanja malire kuti madzi asadutse malirewo, ndiponso pamene ankayika malire a dziko lapansi.
30 Tedym była u niego jako wychowaniec, i byłam uciechą jego na każdy dzień, grając przed nim na każdy czas.
Tsono ine ndinali pambali pake ngati mmisiri; ndikumukondweretsa tsiku ndi tsiku, kusangalala nthawi zonse pamaso pake.
31 Gram na okręgu ziemi jego, a rozkoszy moje, mieszkać z synami ludzkimi.
Ndinkasangalala ndi dziko lake lonse ndiponso kumakondwera nawo anthu onse.”
32 Słuchajcież mię tedy teraz, synowie! albowiem błogosławieni, którzy strzegą dróg moich.
“Ndiye tsono ana inu, ndimvereni; odala anthu amene amasunga njira zanga.
33 Słuchajcie ćwiczenia, nabądźcie rozumu, a nie cofajcie się.
Mverani malangizo anga kuti mukhale ndi nzeru; musanyozere mawu anga.
34 Błogosławiony człowiek, który mię słucha, czując u wrót moich na każdy dzień, a strzegąc podwoi drzwi moich.
Wodala munthu amene amandimvera, amene amakhala pa khomo panga tsiku ndi tsiku, kudikirira pa chitseko changa.
35 Bo kto mię znajduje, znajduje żywot, a otrzymuje łaskę od Pana.
Paja aliyense amene apeza ine wapeza moyo ndipo Yehova amamukomera mtima.
36 Ale kto grzeszy przeciwko mnie, krzywdę czyni duszy swojej; wszyscy, którzy mię nienawidzą, miłują śmierć.
Koma amene alephera kundipeza, amadzipweteka yekha; onse amene amandida amakonda imfa.”

< Przysłów 8 >